< 2 Samueli 19 >

1 Yowabu anawuzidwa kuti, “Mfumu ikulira maliro a Abisalomu.”
And it was told Joab, Behold, the king weeps and mourns for Absalom.
2 Ndipo kwa asilikali onse chipambano cha tsiku limenelo chinasandulika maliro, chifukwa tsiku limenelo anthu anamva kuti mfumu ili pa chisoni chachikulu chifukwa cha mwana wake.
And the victory that day was turned into mourning to all the people, for the people heard say that day, The king grieves for his son.
3 Ankhondo analowa mu mzinda mwakachetechete tsiku limenelo ngati momwe amalowera anthu mwamanyazi chifukwa athawa ku nkhondo.
And the people slipped away that day into the city, as people who are ashamed sneak away when they flee in battle.
4 Mfumu inaphimba nkhope yake ndipo inalira mofuwula, “Iwe mwana wanga Abisalomu! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”
And the king covered his face, and the king cried with a loud voice, O my son Absalom, O Absalom, my son, my son!
5 Kenaka Yowabu analowa mʼnyumba ya mfumu nafika kwa mfumuyo ndipo anati, “Lero mwachititsa manyazi asilikali anu onse, amene apulumutsa moyo wanu ndiponso moyo wa ana anu aamuna ndi aakazi, kudzanso moyo wa akazi anu ndi wa azikazi anu.
And Joab came into the house to the king, and said, Thou have shamed this day the faces of all thy servants, who this day have saved thy life, and the lives of thy sons and of thy daughters, and the lives of thy wives, and the lives of thy concubines,
6 Inu mumakonda amene amadana nanu ndipo mumadana ndi amene amakukondani. Inuyo mwaonetsa lero poyera kuti simusamala za atsogoleri anu a nkhondo ndi asilikali awo. Ine ndikuona kuti inu mukanakondwera ngati Abisalomu akanakhala ndi moyo lero, tonsefe titafa.
in that thou love those who hate thee, and hate those who love thee. For thou have declared this day that rulers and servants are nothing to thee. For this day I perceive, that if Absalom had lived, and all we had died this day, then it would have pleased thee well.
7 Tsopano pitani mukawalimbikitse asilikali anu. Ine ndikulumbira mwa Yehova kuti ngati inu simupita palibe munthu amene adzatsale ali ndi inu polowa dzuwa. Ichi chidzakhala choyipa kwambiri kuposa zovuta zonse zimene zinakugwerani kuyambira muli mnyamata mpaka lero.”
Now therefore arise, go forth, and speak graciously to thy servants. For I swear by Jehovah, if thou do not go forth, there will not remain a man with thee this night. And that will be worse to thee than all the evil that has befallen thee from thy youth until now.
8 Kotero mfumu inanyamuka ndipo inakhala pa mpando wake pa chipata. Pamene asilikali anawuzidwa kuti, “Mfumu yakhala pa chipata,” onse anabwera kwa iye. Nthawi imeneyi nʼkuti Aisraeli atathawira ku nyumba zawo.
Then the king arose, and sat in the gate. And they told to all the people, saying, Behold, the king is sitting in the gate. And all the people came before the king. Now Israel had fled every man to his tent.
9 Pakati pa mafuko onse a Israeli, anthu amakangana ndipo amati, “Mfumu inatipulumutsa mʼmanja mwa adani anthu. Iye ndi amene anatilanditsa mʼdzanja la Afilisti. Koma tsopano wathawa mʼdziko muno chifukwa cha Abisalomu.
And all the people were contending throughout all the tribes of Israel, saying, The king delivered us out of the hand of our enemies, and he saved us out of the hand of the Philistines. And now he fled out of the land from Absalom.
10 Ndipo Abisalomu amene ife tinamudzoza kuti atilamulire wafa pa nkhondo. Tsono nʼchifukwa chiyani simukunena kanthu za kubweretsanso mfumu?”
And Absalom, whom we anointed over us, is dead in battle. Now therefore why speak ye not a word of bringing the king back?
11 Mfumu Davide inatumiza uthenga uwu kwa ansembe Zadoki ndi Abiatara, “Funsani akuluakulu a Yuda, ‘Nʼchifukwa chiyani inu mukukhala otsiriza kuyitana mfumu ku nyumba yake yaufumu, pakuti zimene zikunenedwa mu Israeli yense zamveka kwa mfumu ndi onse amene akukhala nayo.
And king David sent to Zadok and to Abiathar the priests, saying, Speak to the elders of Judah, saying, Why are ye the last to bring the king back to his house? Since the speech of all Israel has come to the king, to bring him to his house.
12 Inu ndinu abale anga enieni, mafupa anga ndi mnofu wanga. Nʼchifukwa chiyani inuyo mukukhala otsiriza kubweretsa mfumu?’
Ye are my brothers, ye are my bone and my flesh. Why then are ye the last to bring back the king?
13 Ndipo munene kwa Amasa, ‘Kodi iwe si mʼbale wanga weniweni? Mulungu andilange, andilange kwambiri ngati kuyambira tsopano sukhala mtsogoleri wa ankhondo anga kulowa mʼmalo mwa Yowabu.’”
And say ye to Amasa, Are thou not my bone and my flesh? God do so to me, and more also, if thou not be captain of the army before me continually in the place of Joab.
14 Davide anakopa mitima ya anthu onse a Yuda ndipo anthuwo anakhala ngati munthu mmodzi. Iwo anatumiza mawu kwa mfumu, “Bwererani inu ndi anthu anu onse.”
And he inclined the heart of all the men of Judah, even as the heart of one man, so that they sent to the king, saying, Return thou, and all thy servants.
15 Kotero mfumu inabwerera ndipo inakafika mpaka ku Yorodani. Tsono anthu a ku Yuda anabwera ku Giligala kuti akakumane ndi mfumu ndi kumuwolotsa Yorodani.
So the king returned, and came to the Jordan. And Judah came to Gilgal, to go to meet the king, to bring the king over the Jordan.
16 Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wa ku Bahurimu, anabwera mofulumira pamodzi ndi Ayuda kudzakumana ndi mfumu Davide.
And Shimei the son of Gera, the Benjamite, who was of Bahurim, hastened and came down with the men of Judah to meet king David.
17 Iyeyo anali ndi anthu 1,000 a fuko la Benjamini pamodzi ndi Ziba, wantchito wa banja la Sauli ndi ana ake aamuna khumi ndi asanu ndi antchito ake makumi awiri. Iwo anathamangira ku Yorodani kumene kunali mfumu.
And there were a thousand men of Benjamin with him, and Ziba the servant of the house of Saul, and his fifteen sons and his twenty servants with him. And they went through the Jordan in the presence of the king.
18 Iwo anawoloka mtsinje kukatenga banja lonse la mfumu ndi kuchita zonse zimene mfumuyo imafuna. Pamene Simei mwana wa Gera anawoloka Yorodani, anagwa pansi chafufumimba pamaso pa mfumu,
And there went over a ferry-boat to bring over the king's household, and to do what he thought good. And Shimei the son of Gera fell down before the king when he came over the Jordan.
19 ndipo anati, “Mbuye wanga musaganizire za kulakwa kwanga. Musakumbukire zolakwa zimene mtumiki wanu anakuchitirani tsiku limene mbuye wanga mfumu mumachoka mu Yerusalemu. Mfumu musazikumbukirenso zimenezi.
And he said to the king, Let not my lord impute iniquity to me, neither remember thou that which thy servant did perversely the day that my lord the king went out of Jerusalem, that the king should take it to his heart.
20 Pakuti ine mtumiki wanu ndazindikira kuti ndachimwa. Koma lero ndabwera ngati woyamba wa nyumba ya Yosefe yonse kudzakumana nanu mbuye wanga mfumu.”
For thy servant knows that I have sinned. Therefore, behold, I have come this day the first of all the house of Joseph to go down to meet my lord the king.
21 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati, “Kodi Simei saphedwa chifukwa cha ichi? Iye anatukwana wodzozedwa wa Yehova.”
But Abishai the son of Zeruiah answered and said, Shall not Shimei be put to death for this, because he cursed Jehovah's anointed?
22 Davide anayankha kuti, “Kodi inu ana a Zeruya, ndikuchitireni chiyani? Lero lino iwe wakhala mdani wanga! Kodi wina aphedwe lero mu Israeli? Kodi ine sindikudziwa kuti lero ndine mfumu mu Israeli?”
And David said, What have I to do with you, ye sons of Zeruiah, that ye should this day be adversaries to me? Shall there any man be put to death this day in Israel? For do I not know that I am this day king over Israel?
23 Ndipo mfumu inati kwa Simei, “Iwe Simei suphedwa.” Ndipo mfumuyo inalonjeza ndi lumbiro.
And the king said to Shimei, Thou shall not die. And the king swore to him.
24 Mefiboseti, mdzukulu wa Sauli, nayenso anabwera kudzakumana ndi mfumu. Kuyambira tsiku limene mfumu inachoka mpaka tsiku limene inabwerera mu mtendere, iye sanasambe mapazi kaya kumeta ndevu kapena kuchapa zovala zake.
And Mephibosheth the son of Saul came down to meet the king. And he had neither dressed his feet, nor trimmed his beard, nor washed his clothes, from the day the king departed until the day he came home in peace.
25 Pamene anafika kuchokera ku Yerusalemu kudzakumana ndi mfumu, mfumu inamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunapite nane Mefiboseti?”
And it came to pass, when he came to Jerusalem to meet the king, that the king said to him, Why did thou not go with me, Mephibosheth?
26 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga mfumu, pakuti ine wantchito wanu ndine wolumala. Ndinati, ‘Andikonzere chishalo cha bulu wanga ndipo ndidzakwera kuti ndipite ndi mfumu.’ Koma Ziba wantchito wanga anandilakwitsa.
And he answered, My lord, O king, my servant deceived me. For thy servant said, I will saddle for me a donkey, that I may ride on it, and go with the king, because thy servant is lame.
27 Ndipo wayankhula zosinjirira za ine mtumiki wanu kwa inu mbuye wanga mfumu. Mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu ndipo chitani chimene chikukomerani.
And he has slandered thy servant to my lord the king. But my lord the king is as an agent of God; do therefore what is good in thine eyes.
28 Zidzukulu zonse za agogo anga sizinayenera chilichonse koma imfa kuchokera kwa inu mbuye wanga mfumu, koma inu munapereka malo kwa mtumiki wanu pakati pa amene amadya pa tebulo lanu. Tsono ine ndili ndi chiyaninso kuti ndipitirize kudandaula kwa mfumu?”
For all my father's house were but dead men before my lord the king. Yet thou set thy servant among those who ate at thine own table. What right therefore have I yet that I should cry any more to the king?
29 Mfumu inayankha kuti, “Uneneranji zambiri? Ine ndikulamula kuti iwe ndi Ziba mugawane minda.”
And the king said to him, Why do thou speak any more of thy matters? I say, thou and Ziba divide the land.
30 Mefiboseti anati kwa mfumu, “Muloleni atenge zonse, pakuti tsopano mbuye wanga mwafika kwanu mu mtendere.”
And Mephibosheth said to the king, Yea, let him take all, inasmuch as my lord the king has come in peace to his own house.
31 Barizilai Mgiliyadi anabweranso kuchokera ku Rogelimu kudzawoloka Yorodani ndi mfumu ndi kumuperekeza kuchokera kumeneko.
And Barzillai the Gileadite came down from Rogelim. And he went over the Jordan with the king to conduct him over the Jordan.
32 Tsono Barizilai anali wokalamba kwambiri, wa zaka makumi asanu ndi atatu. Iye ndi amene anapereka zinthu kwa mfumu pamene anali ku Mahanaimu pakuti anali wolemera kwambiri.
Now Barzillai was a very aged man, even eighty years old. And he had provided the king with sustenance while he lay at Mahanaim, for he was a very great man of wealth.
33 Mfumu inati kwa Barizilai, “Woloka nane ndipo ukakhale ndi ine mu Yerusalemu ndipo ineyo ndidzakusamalira.”
And the king said to Barzillai, Come thou over with me, and I will sustain thee with me in Jerusalem.
34 Barizilai anayankha mfumu kuti, “Kodi zakhala zaka zingati zoti ndikhale ndi moyo, kuti ndipite ku Yerusalemu ndi mfumu?
And Barzillai said to the king, How many are the days of the years of my life that I should go up with the king to Jerusalem?
35 Ine tsopano ndili ndi zaka 80. Kodi ndingathe kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa? Kodi mtumiki wanu angathe kuzindikira kukoma kwa zimene akudya ndi kumwa? Kodi ndingathe kumva kuyimba kwa amuna ndi akazi? Nʼchifukwa chiyani wantchito wanu akakhale ngati katundu kwa mbuye wanga mfumu?
I am this day eighty years old. Can I discern between good and bad? Can thy servant taste what I eat or what I drink? Can I hear any more the voice of singing men and singing women? Why then should thy servant be yet a burden to my lord the king?
36 Koma ine mtumiki wanu ndingoyenda pangʼono kuti ndiwoloke Yorodani pamodzi ndi mfumu. Amfumu mungandipatsirenji mphotho yotere?
Thy servant would but just go over the Jordan with the king, and why should the king recompense it to me with such a reward?
37 Muloleni, mtumiki wanu abwerere, kuti ndikafere kwathu pafupi ndi manda a abambo ndi amayi anga. Koma nayu mtumiki wanu Kimuhamu. Muloleni iye awoloke nanu mbuye wanga mfumu. Mumuchitire chilichonse chimene chikukomereni!”
Let thy servant, I pray thee, turn back again, that I may die in my own city by the grave of my father and my mother. But behold, thy servant Chimham, let him go over with my lord the king, and do to him what shall seem good to thee.
38 Mfumu inati, “Kimuhamu adzawoloka ndi ine, ndipo ndidzamuchitira iye chilichonse chimene chidzakondweretsa iwe. Ndipo chilichonse chimene udzandipempha ine ndidzakuchitira.”
And the king answered, Chimham shall go over with me, and I will do to him that which shall seem good to thee. And whatever thou shall require of me, that I will do for thee.
39 Kotero anthu onse anawoloka Yorodani ndipo kenaka mfumu inawoloka. Mfumu inapsompsona Barizilai ndi kumupatsa madalitso ndipo Barizilaiyo anabwerera kwawo.
And all the people went over the Jordan, and the king went over. And the king kissed Barzillai, and blessed him, and he returned to his own place.
40 Pamene mfumu inawolokera ku Giligala, Kimuhamu anawoloka naye. Ankhondo onse a Yuda ndi theka la ankhondo a Israeli onse anaperekeza mfumu.
So the king went over to Gilgal, and Chimham went over with him. And all the people of Judah brought the king over, and also half the people of Israel.
41 Kenaka Aisraeli onse amabwera kwa mfumu nʼkumati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani abale athu, anthu a ku Ayuda, anakubani mfumu, nawoloka nanu Yorodani inu ndi banja lanu, pamodzi ndi anthu ake onse?”
And, behold, all the men of Israel came to the king, and said to the king, Why have our brothers the men of Judah stolen thee away, and brought the king, and his household, over the Jordan, and all David's men with him?
42 Ayuda onse anayankha Aisraeli kuti, “Ife timachita zimenezi chifukwa mfumu ndi mʼbale wathu. Nʼchifukwa chiyani inu mwapsa mtima ndi zimenezi? Kodi ife tinadya chakudya chilichonse cha mfumu? Kodi chilipo chimene ife tatenga kukhala chathu?”
And all the men of Judah answered the men of Israel, Because the king is near of kin to us. Why then are ye angry for this matter? Have we eaten at all at the king's cost, or has he given us any gift?
43 Aisraeli anayankha Ayuda kuti, “Ife ndi magawo khumi mwa mfumu imeneyi, ndipo kuwonjezera apo, ife tili ndi zinthu zambiri mwa Davide kuposa inu. Tsono nʼchifukwa chiyani mukutichita chipongwe? Kodi ife si amene tinayamba kunena za kubweretsa mfumu yathu?” Koma anthu a Yuda anayankha mwaukali kwambiri kupambana anthu a ku Israeli.
And the men of Israel answered the men of Judah, and said, We have ten parts in the king, and we have also more right in David than ye. Why then did ye despise us, that our advice should not be had first in bringing back our king? And the words of the men of Judah were fiercer than the words of the men of Israel.

< 2 Samueli 19 >