< 2 Samueli 17 >

1 Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
Moreover Ahithophel said to Absalom, Let me now choose out twelve thousand men, and I will arise and pursue after David this night.
2 Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
And I will come upon him while he is weary and weak-handed, and will make him afraid. And all the people who are with him shall flee. And I will only smite the king,
3 ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
and I will bring back all the people to thee. The man whom thou seek is as if all returned, so all the people shall be in peace.
4 Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
And the saying pleased Absalom well, and all the elders of Israel.
5 Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
Then Absalom said, Call now Hushai the Archite also, and let us hear likewise what he says.
6 Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
And when Hushai came to Absalom, Absalom spoke to him, saying, Ahithophel has spoken after this manner. Shall we do after his saying? If not, speak thou.
7 Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
And Hushai said to Absalom, The counsel that Ahithophel has given this time is not good.
8 Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
Hushai said moreover, Thou know thy father and his men, that they are mighty men, and they are chafed in their minds, as a bear robbed of her whelps in the field. And thy father is a man of war, and will not lodge with the people.
9 Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
Behold, he is hid now in some pit, or in some other place. And it will come to pass, when some of them are fallen at the first, that whoever hears it will say, There is a slaughter among the people who follow Absalom.
10 Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
And even he who is valiant, whose heart is as the heart of a lion, will utterly melt, for all Israel knows that thy father is a mighty man, and those who are with him are valiant men.
11 “Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
But I counsel that all Israel be gathered together to thee, from Dan even to Beersheba, as the sand that is by the sea for multitude, and that thou go to battle in thine own person.
12 Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
So we shall come upon him in some place where he shall be found, and we will light upon him as the dew falls on the ground, and of him and of all the men who are with him we will not leave so much as one.
13 Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
Moreover, if he be gotten into a city, then all Israel shall bring ropes to that city, and we will draw it into the river until there be not one small stone found there.
14 Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
And Absalom and all the men of Israel said, The counsel of Hushai the Archite is better than the counsel of Ahithophel. For Jehovah had ordained to defeat the good counsel of Ahithophel, to the intent that Jehovah might bring evil upon Absalom.
15 Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
Then Hushai said to Zadok and to Abiathar the priests, Thus and thus did Ahithophel counsel Absalom and the elders of Israel, and thus and thus have I counseled.
16 Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
Now therefore send quickly, and tell David, saying, Do not lodge this night at the fords of the wilderness, but by all means pass over, lest the king be swallowed up, and all the people who are with him.
17 Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
Now Jonathan and Ahimaaz were staying by En-rogel. And a maid-servant used to go and tell them, and they went and told king David, for they might not be seen to come into the city.
18 Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
But a lad saw them, and told Absalom. And they went away quickly, both of them, and came to the house of a man in Bahurim who had a well in his court, and they went down there.
19 Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
And the woman took and spread the covering over the well's mouth, and spread ground grain on it. And nothing was known.
20 Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
And Absalom's servants came to the woman to the house, and they said, Where are Ahimaaz and Jonathan? And the woman said to them, They have gone over the brook of water. And when they had sought and could not find them, they returned to Jerusalem.
21 Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
And it came to pass, after they were departed, that they came up out of the well, and went and told king David. And they said to David, Arise ye, and pass quickly over the water, for thus Ahithophel has counseled against you.
22 Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
Then David arose, and all the people who were with him, and they passed over the Jordan. By the morning light there lacked not one of them who was not gone over the Jordan.
23 Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
And when Ahithophel saw that his counsel was not followed, he saddled his donkey, and arose, and got home to his city, and set his house in order, and hanged himself. And he died, and was buried in the sepulcher of his father.
24 Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
Then David came to Mahanaim. And Absalom passed over the Jordan, he and all the men of Israel with him.
25 Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
And Absalom set Amasa over the army instead of Joab. Now Amasa was the son of a man, whose name was Ithra the Israelite, who went in to Abigal the daughter of Nahash, sister to Zeruiah, Joab's mother.
26 Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
And Israel and Absalom encamped in the land of Gilead.
27 Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
And it came to pass, when David came to Mahanaim, that Shobi the son of Nahash of Rabbah of the sons of Ammon, and Machir the son of Ammiel of Lodebar, and Barzillai the Gileadite of Rogelim,
28 anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
brought beds, and basins, and earthen vessels, and wheat, and barley, and meal, and roasted grain, and beans, and lentils, and roasted pulse,
29 uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”
and honey, and butter, and sheep, and cheese of the herd, for David, and for the people who were with him, to eat. For they said, The people are hungry, and weary, and thirsty, in the wilderness.

< 2 Samueli 17 >