< 2 Samueli 16 >

1 Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
And when David was a little past the top of the ascent, behold, Ziba the servant of Mephibosheth met him with a couple of saddled donkeys, and upon them two hundred loaves of bread, and a hundred clusters of raisins, and a hundred of summer fruits, and a bottle of wine.
2 Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
And the king said to Ziba, What do thou mean by these? And Ziba said, The donkeys are for the king's household to ride on, and the bread and summer fruit for the young men to eat, and the wine, that such as are faint in the wilderness may drink.
3 Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
And the king said, And where is thy master's son? And Ziba said to the king, Behold, he abides at Jerusalem, for he said, Today the house of Israel will restore for me the kingdom of my father.
4 Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
Then the king said to Ziba, Behold, all that pertains to Mephibosheth is thine. And Ziba said, I do obeisance. Let me find favor in thy sight, my lord, O king.
5 Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
And when king David came to Bahurim, behold, there came out from there a man of the family of the house of Saul whose name was Shimei, the son of Gera. He came out, cursing as he came.
6 Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
And he cast stones at David, and at all the servants of king David, and all the people and all the mighty men were on his right hand and on his left.
7 Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
And thus said Shimei when he cursed, Begone, begone, thou man of blood, and base fellow.
8 Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
Jehovah has returned upon thee all the blood of the house of Saul in whose stead thou have reigned. And Jehovah has delivered the kingdom into the hand of Absalom thy son, and, behold, thou are taken in thine own mischief because thou are a man of blood.
9 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
Then Abishai the son of Zeruiah said to the king, Why should this dead dog curse my lord the king? Let me go over, I pray thee, and take off his head.
10 Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
And the king said, What have I to do with you, ye sons of Zeruiah? Because he curses, and because Jehovah has said to him, Curse David, who then shall say, Why have thou done so?
11 Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
And David said to Abishai, and to all his servants, Behold, my son, who came forth from my bowels, seeks my life. How much more this Benjamite? Let him alone, and let him curse, for Jehovah has bidden him.
12 Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
It may be that Jehovah will look on the wrong done to me, and that Jehovah will reward me good for his cursing of me this day.
13 Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
So David and his men went by the way, and Shimei went along on the hill-side opposite him, and cursed as he went, and threw stones at him, and cast dust.
14 Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
And the king, and all the people who were with him, came weary, and he refreshed himself there.
15 Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
And Absalom, and all the people, the men of Israel, came to Jerusalem, and Ahithophel with him.
16 Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
And it came to pass, when Hushai the Archite, David's friend, came to Absalom, that Hushai said to Absalom, Live, O king. Live, O king.
17 Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
And Absalom said to Hushai, Is this thy kindness to thy friend? Why did thou not go with thy friend?
18 Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
And Hushai said to Absalom, No, but whom Jehovah, and this people, and all the men of Israel have chosen, his will I be, and with him I will abide.
19 Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
And again, whom should I serve? Is it not in the presence of his son? As I have served in thy father's presence, so I will be in thy presence.
20 Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
Then Absalom said to Ahithophel, Give your counsel what we shall do.
21 Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
And Ahithophel said to Absalom, Go in to thy father's concubines that he has left to keep the house, and all Israel will hear that thou are abhorred by thy father. Then the hands of all who are with thee will be strong.
22 Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
So they spread Absalom a tent upon the top of the house, and Absalom went in to his father's concubines in the sight of all Israel.
23 Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.
And the counsel of Ahithophel, which he gave in those days, was as if a man inquired at the oracle of God; so was all the counsel of Ahithophel both with David and with Absalom.

< 2 Samueli 16 >