< 2 Samueli 13 >

1 Patapita nthawi, Amnoni mwana wa Davide anakonda Tamara, mlongo wa Abisalomu, mwana wa Davide, amene anali wokongola.
And it came to pass after this, that Absalom the son of David had a fair sister whose name was Tamar. And Amnon the son of David loved her.
2 Amnoni sankagona tulo mpaka anadwala chifukwa cha Tamara mlongo wakeyo, pakuti iye anali asanagonepo ndi mwamuna ndipo zimaoneka kuti zinali zosatheka kuti achite chilichonse kwa iye.
And Amnon was so frustrated that he fell sick because of his sister Tamar. For she was a virgin, and it seemed hard to Amnon to do anything to her.
3 Koma Amnoni anali ndi mnzake dzina lake Yehonadabu mwana wamwamuna wa Simea, mʼbale wake wa Davide. Yonadabu anali munthu wochenjera kwambiri.
But Amnon had a friend whose name was Jonadab, the son of Shimeah, David's brother. And Jonadab was a very sly man.
4 Iye anafunsa Amnoni, “Nʼchifukwa chiyani iwe mwana wa mfumu, umaoneka wowonda mmawa uliwonse? Bwanji wosandiwuza?” Amnoni anamuyankha kuti, “Ine ndamukonda Tamara, mlongo wa mʼbale wanga Abisalomu.”
And he said to him, Why, O son of the king, are thou emaciated this way from day to day? Will thou not tell me? And Amnon said to him, I love Tamar, my brother Absalom's sister.
5 Yehonadabu anati, “Pita ukagone ndipo unamizire kudwala. Abambo ako akabwera kudzakuona, udzati kwa iwo, Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara abwere kuti adzandikonzere chakudya kuti ndidye. Adzandikonzere chakudyacho ine ndikumuona ndi kudya chili mʼmanja mwake.”
And Jonadab said to him, Lie down on thy bed, and feign thyself sick. And when thy father comes to see thee, say to him, Let my sister Tamar come, I pray thee, and give me bread to eat, and dress the food in my sight, that I may see it, and eat it from her hand.
6 Kotero Amnoni anagona nakhala ngati akudwala. Mfumu itabwera kudzamuona, Amnoni anati kwa iyo, “Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara kuti abwere adzandipangire buledi wapamwamba ineyo ndikuona, kuti ndidye ali mʼmanja mwake.”
So Amnon lay down, and feigned himself sick. And when the king came to see him, Amnon said to the king, Let my sister Tamar come, I pray thee, and make me a couple of cakes in my sight, that I may eat from her hand.
7 Davide anatumiza mawu kwa Tamara ku nyumba yaufumu kuti, “Pita ku nyumba ya mlongo wako Amnoni ndipo ukamukonzere chakudya.”
Then David sent home to Tamar, saying, Go now to thy brother Amnon's house, and make food for him.
8 Choncho Tamara anapitadi ku nyumba ya mlongo wake Amnoni kumalo kumene ankagona. Anakanda ufa, nawumba buledi Amunoniyo akuona ndipo anaphika bulediyo.
So Tamar went to her brother Amnon's house, and he was laid down. And she took dough, and kneaded it, and made cakes in his sight, and baked the cakes.
9 Kenaka iye anatenga chiwaya ndipo anamupatsa bulediyo, koma iyeyo anakana. Amnoni anati “Uza aliyense atuluke muno.” Ndipo aliyense anatuluka.
And she took the pan, and poured them out before him, but he refused to eat. And Amnon said, Have all men out from me. And they went out every man from him.
10 Kenaka Amnoni anati kwa Tamara, “Bweretsa chakudya kuno, ku chipinda changa chogona kuti ndidye chili mʼmanja mwako.” Ndipo Tamara anatenga buledi amene anapanga ndi kubwera naye kwa mlongo wake ku chipinda chake.
And Amnon said to Tamar, Bring the food into the chamber that I may eat from thy hand. And Tamar took the cakes that she had made, and brought them into the chamber to Amnon her brother.
11 Koma atabweretsa kwa iye kuti adye, anamugwira ndipo anati, “Bwera ugone nane, iwe mlongo wanga.”
And when she had brought them near to him to eat, he took hold of her, and said to her, Come, lie with me, my sister.
12 Tamara anati kwa iye, “Ayi mlongo wanga! Usandikakamize. Zotere siziyenera kuchitika mu Israeli! Usachite chinthu choyipa chotere.
And she answered him, No, my brother, do not force me, for no such thing ought to be done in Israel. Do not do thou this folly.
13 Kodi ukuganiza bwanji za ine? Kodi manyazi anga ndidzawachotsa bwanji? Ndipo nanga iweyo? Udzakhalatu monga mmodzi mwa zitsiru zoyipitsitsa muno mu Israeli. Chonde kapemphe kwa mfumu. Sadzakuletsa kuti undikwatire.”
And I, where shall I carry my shame? And as for thee, thou will be as one of the fools in Israel. Now therefore, I pray thee, speak to the king, for he will not withhold me from thee.
14 Koma sanamvere zimene amanena Tamara ndipo popeza anali wamphamvu kuposa Tamarayo, iye anamugwirira.
However he would not hearken to her voice, but being stronger than she, he forced her, and lay with her.
15 Atatero Amnoni anadana naye kwambiri. Iyeyo anamuda kuposa momwe anamukondera. Amnoni anati, “Dzuka ndipo tuluka!”
Then Amnon hated her with exceedingly great hatred, for the hatred with which he hated her was greater than the love with which he had loved her. And Amnon said to her, Arise, be gone.
16 Iye anayankha, “Ayi! Kundithamangitsa kukhala kulakwa kwakukulu kuposa zimene wachita kale kwa ine.” Koma anakana kumumvera.
And she said to him, Not so, because this great wrong in putting me forth is worse than the other that thou did to me. But he would not hearken to her.
17 Amnoni anayitana wantchito wake ndipo anati, “Mutulutse mkazi uyu muno ndipo utseke chitseko akatuluka.”
Then he called his servant who ministered to him, and said, Put this woman out from me now, and bolt the door after her.
18 Choncho wantchito wakeyo anamutulutsa ndipo anatseka chitseko atatuluka. Tamara anali atavala mkanjo wokongoletsedwa kwambiri, pakuti ichi chinali chovala chimene ana aakazi a mfumu amene sanagonepo ndi mwamuna amavala.
And she had a garment of various colors upon her, for with such robes were the king's daughters who were virgins appareled. Then his servant brought her out, and bolted the door after her.
19 Tamara anatsira phulusa pamutu pake ndipo anangʼamba mkanjo wokongoletsedwa umene anavalawo. Iye anagwira manja ake kumutu ndipo anachoka, akulira mokweza pamene amapita.
And Tamar put ashes on her head, and tore her garment of various colors that was on her. And she laid her hand on her head, and went her way, crying aloud as she went.
20 Mlongo wake Abisalomu anati, “Kodi Amnoni uja mlongo wako wagona nawe? Khala chete mlongo wanga. Iye uja ndi mlongo wako ndipo usazilabadire.” Choncho Tamara anakhala mʼnyumba ya Abisalomu mlongo wake ngati woferedwa.
And Absalom her brother said to her, Has Amnon thy brother been with thee? But now hold thy peace, my sister. He is thy brother. Do not take this thing to heart. So Tamar remained desolate in her brother Absalom's house.
21 Mfumu Davide itamva zimenezi, inakwiya kwambiri.
But when king David heard of all these things, he was very angry.
22 Abisalomu sananene mawu aliwonse kwa Amnoni; abwino kapena oyipa. Iye anamuda Amunoniyo chifukwa anachititsa manyazi mlongo wake Tamara.
And Absalom spoke to Amnon neither good nor bad, for Absalom hated Amnon, because he had forced his sister Tamar.
23 Patapita zaka ziwiri, pamene wometa nkhosa za Abisalomu anali ku Baala-Hazori pafupi ndi malire a fuko la Efereimu, iye anayitana ana onse aamuna a mfumu kuti apite kumeneko.
And it came to pass after two full years, that Absalom had sheep-shearers in Baal-hazor, which is beside Ephraim, and Absalom invited all the king's sons.
24 Abisalomu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Ometa nkhosa za mtumiki wanu anabwera. Chonde mfumu ndi akuluakulu anu mubwere kudzakhala nane?”
And Absalom came to the king, and said, Behold now, thy servant has sheep-shearers. Let the king, I pray thee, and his servants go with thy servant.
25 Mfumu inayankha kuti, “Ayi mwana wanga, tisapite tonsefe. Tidzakhala cholemetsa kwa iwe.” Ngakhale Abisalomu anayesetsa kuwumiriza mfumuyo, inakana kupita. Mʼmalo mwake inangomudalitsa Abisalomuyo.
And the king said to Absalom, No, my son, let us not all go, lest we be burdensome to thee. And he pressed him. However he would not go, but blessed him.
26 Kenaka Abisalomu anati, “Ngati sizitero, chonde mulole mʼbale wanga Amnoni apite nane.” Mfumu inamufunsa kuti, “Apite nawe chifukwa chiyani?”
Then Absalom said, If not, I pray thee, let my brother Amnon go with us. And the king said to him, Why should he go with thee?
27 Koma Abisalomu anamuwumiriza, kotero analola kuti Amnoni pamodzi ndi ana onse a mfumu apite naye.
But Absalom pressed him, and he let Amnon and all the king's sons go with him.
28 Abisalomu analamula antchito ake kuti, “Tamverani! Amnoni akakaledzera ndi vinyo ndipo ine ndikakanena kuti, ‘Mukantheni Amnoni,’ pamenepo mukamuphe. Musakachite mantha. Kodi ine sindinakulamuleni? Mukhale amphamvu ndipo mulimbe mtima.”
And Absalom commanded his servants, saying, Notice ye now, when Amnon's heart is merry with wine, and when I say to you, Smite Amnon, then kill him. Fear not; have I not commanded you? Be courageous, and be valiant.
29 Kotero antchito a Abisalomu anachita kwa Amnoni zimene Abisalomu anawalamula. Kenaka ana onse a mfumu anayimirira ndipo anakwera pa abulu awo nathawa.
And the servants of Absalom did to Amnon as Absalom had commanded. Then all the king's sons arose, and every man got up upon his mule, and fled.
30 Ali mʼnjira, Davide anamva mphekesera yakuti, “Abisalomu wakantha ana onse a mfumu ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene watsala.”
And it came to pass, while they were in the way, that the news came to David, saying, Absalom has slain all the king's sons, and there is not one of them left.
31 Mfumu inayimirira, ningʼamba zovala zake ndi kugona pa dothi. Antchito ake onse anayimirira pomwepo atangʼamba zovala zawo.
Then the king arose, and tore his garments, and lay on the earth, and all his servants stood by with their clothes torn.
32 Koma Yehonadabu mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anati, “Mbuye wanga mfumu musaganize kuti wapha ana onse a mfumu; wafa ndi Amnoni yekha. Awa ndiwo akhala maganizo a Abisalomu kuyambira tsiku limene Amnoni anagwirira mlongo wake Tamara.
And Jonadab, the son of Shimeah, David's brother, answered and said, Let not my lord suppose that they have killed all the young men the king's sons, for Amnon only is dead. For by the command of Absalom this has been determined from the day that he forced his sister Tamar.
33 Mbuye wanga mfumu musavutike ndi maganizo ndi nkhani yoti ana onse a mfumu afa. Wafa ndi Amnoni yekha.”
Now therefore let not my lord the king take the thing to his heart, to think that all the king's sons are dead, for only Amnon is dead.
34 Nthawi imeneyi nʼkuti Abisalomu atathawa. Tsono munthu amene amalondera anayangʼana ndipo anaona anthu ambiri pa msewu wa kumadzulo kwake, akubwera kutsetsereka phiri. Mlondayo anapita kukawuza mfumu kuti, “Ndikuona anthu pa njira ya Horonaimu, mʼmbali mwa phiri.”
But Absalom fled. And the young man who kept the watch lifted up his eyes, and looked, and, behold, there came much people by the way of the hill-side behind him.
35 Yehonadabu anati kwa mfumu, “Taonani ana a mfumu afika. Zachitika monga momwe mtumiki wanu ananenera.”
And Jonadab said to the king, Behold, the king's sons have come; as thy servant said, so it is.
36 Pamene amatsiriza kuyankhula, ana a mfumu analowa, akulira mofuwula. Mfumunso ndi antchito ake onse analira mokhudzidwa.
And it came to pass, as soon as he had made an end of speaking, that, behold, the king's sons came, and lifted up their voice, and wept. And the king also and all his servants wept very much.
37 Abisalomu anathawa, napita kwa Talimai mwana wa Amihudi, mfumu ya ku Gesuri. Koma mfumu Davide inalira mwana wake tsiku ndi tsiku.
But Absalom fled, and went to Talmai the son of Ammihur, king of Geshur. And David mourned for his son every day.
38 Abisalomu atathawa ndi kupita ku Gesuri, anakhala kumeneko zaka zitatu.
So Absalom fled, and went to Geshur, and was there three years.
39 Ndipo Davide anagwidwa ndi chifundo chofuna kumulondola Abisalomu pakuti anali atatonthozedwa pa imfa ya Amnoni.
And the soul of king David longed to go forth to Absalom, for he was comforted concerning Amnon, seeing he was dead.

< 2 Samueli 13 >