< 2 Samueli 12 >

1 Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
And Jehovah sent Nathan to David. And he came to him, and said to him, There were two men in one city: the one rich, and the other poor.
2 Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
The rich man had exceedingly many flocks and herds,
3 koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
but the poor man had nothing except one little ewe lamb, which he had bought and nourished up. And it grew up together with him, and with his sons. It ate of his own morsel, and drank of his own cup, and lay in his bosom, and was to him as a daughter.
4 “Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
And there came a traveler to the rich man, and he spared to take of his own flock and of his own herd to dress for the wayfaring man who came to him, but took the poor man's lamb, and dressed it for the man who came to him.
5 Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
And David's anger was greatly kindled against the man, and he said to Nathan, As Jehovah lives, the man who has done this is worthy to die.
6 Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
And he shall restore the lamb fourfold, because he did this thing, and because he had no pity.
7 Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
And Nathan said to David, Thou are the man. Thus says Jehovah, the God of Israel, I anointed thee king over Israel, and I delivered thee out of the hand of Saul.
8 Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
And I gave thee thy master's house, and thy master's wives into thy bosom, and gave thee the house of Israel and of Judah. And if that had been too little, I would have added to thee such and such things.
9 Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
Why have thou despised the word of Jehovah, to do that which is evil in his sight? Thou have smitten Uriah the Hittite with the sword, and have taken his wife to be thy wife, and have slain him with the sword of the sons of Ammon.
10 Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
Now therefore the sword shall never depart from thy house, because thou have despised me, and have taken the wife of Uriah the Hittite to be thy wife.
11 “Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
Thus says Jehovah, Behold, I will raise up evil against thee out of thine own house. And I will take thy wives before thine eyes, and give them to thy neighbor, and he shall lie with thy wives in the sight of this sun.
12 Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
For thou did it secretly, but I will do this thing before all Israel, and before the sun.
13 Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
And David said to Nathan, I have sinned against Jehovah. And Nathan said to David, Jehovah also has put away thy sin; thou shall not die.
14 Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
However, because by this deed thou have given great occasion to the enemies of Jehovah to blaspheme, the child also that is born to thee shall surely die.
15 Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
And Nathan departed to his house. And Jehovah struck the child that Uriah's wife bore to David, and it was very sick.
16 Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
David therefore besought God for the child. And David fasted, and went in, and lay all night upon the ground.
17 Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
And the elders of his house arose, and stood beside him, to raise him up from the ground, but he would not, neither did he eat bread with them.
18 Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
And it came to pass on the seventh day, that the child died. And the servants of David feared to tell him that the child was dead, for they said, Behold, while the child was yet alive we spoke to him, and he did not hearken to our voice, how will he then vex himself, if we tell him that the child is dead!
19 Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
But when David saw that his servants were whispering together, David perceived that the child was dead. And David said to his servants, Is the child dead? And they said, He is dead.
20 Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
Then David arose from the earth, and washed, and anointed himself, and changed his apparel. And he came into the house of Jehovah, and worshiped. Then he came to his own house, and when he required, they set bread before him, and he ate.
21 Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
Then his servants said to him, What thing is this that thou have done? Thou fasted and wept for the child while it was alive, but when the child was dead, thou arose and ate bread.
22 Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
And he said, While the child was yet alive, I fasted and wept. For I said, Who knows whether Jehovah will not be gracious to me, that the child may live?
23 Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
But now he is dead; why should I fast? Can I bring him back again? I shall go to him, but he will not return to me.
24 Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
And David comforted Bathsheba his wife, and went in to her, and lay with her. And she bore a son, and he called his name Solomon. And Jehovah loved him,
25 Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
and he sent by the hand of Nathan the prophet. And he called his name Jedidiah, for Jehovah's sake.
26 Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
Now Joab fought against Rabbah of the sons of Ammon, and took the royal city.
27 Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
And Joab sent messengers to David, and said, I have fought against Rabbah; yea, I have taken the city of waters.
28 Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
Now therefore gather the rest of the people together, and encamp against the city, and take it, lest I take the city, and it be called after my name.
29 Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
And David gathered all the people together, and went to Rabbah, and fought against it, and took it.
30 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
And he took the crown of their king from off his head. And the weight of it was a talent of gold, and in it were precious stones. And it was set on David's head. And he brought forth the spoil of the city, exceedingly much.
31 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
And he brought forth the people that were in it, and put them under saws, and under harrows of iron, and under axes of iron, and made them pass through the brick-kiln. And thus he did to all the cities of the sons of Ammon. And David and all the people returned to Jerusalem.

< 2 Samueli 12 >