< 1 Samueli 19 >

1 Sauli anawuza mwana wake Yonatani ndi nduna zake zonse kuti aphe Davide. Koma Yonatani amamukonda kwambiri Davide.
And Saul spoke to Jonathan his son, and to all his servants, that they should kill David. But Jonathan, Saul's son, delighted much in David.
2 Choncho anawuza Davide kuti, “Abambo anga Sauli akufuna kukupha. Tsono uchenjere. Mmawa upite ukabisale ndipo ukakhale komweko.
And Jonathan told David, saying, Saul my father seeks to kill thee. Now therefore, I pray thee, take heed to thyself in the morning, and abide in a secret place, and hide thyself.
3 Ine ndidzapita ndi kukayima pafupi ndi abambo anga ku munda kumene iwe ukabisale. Ndipo ndidzayankhula ndi abambo anga za iwe ndipo chilichonse chimene ndikamve ndidzakuwuza.”
And I will go out and stand beside my father in the field where thou are, and I will converse with my father of thee, and if I see anything, I will tell thee.
4 Tsono Yonatani anakanena zabwino za Davide kwa abambo ake Sauli ndipo anati, “Mfumu musachimwire mtumiki wanu Davide, sanakuchimwireni, koma amakuchitirani zabwino kwambiri.
And Jonathan spoke good of David to Saul his father, and said to him, Let not the king sin against his servant, against David, because he has not sinned against thee, and because his works have been very good toward thee.
5 Iye anayika moyo wake pa chiswe pamene anapha Mfilisiti uja. Choncho Yehova anachita zazikulu popambanitsa Aisraeli pa nkhondo. Inu munaona zonsezo ndipo munakondwera. Nanga nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwira munthu wosalakwa pofuna kupha Davide?”
For he put his life in his hand, and smote the Philistine, and Jehovah wrought a great victory for all Israel. Thou saw it, and rejoiced. Why then will thou sin against innocent blood, to kill David without a cause?
6 Sauli anamvera mawu a Yonatani ndipo analumbira kuti, “Pali Yehova, Davide sadzaphedwa.”
And Saul hearkened to the voice of Jonathan. And Saul swore, As Jehovah lives, he shall not be put to death.
7 Pambuyo pake Yonatani anayitana Davide namuwuza zonsezi. Choncho Yonatani anabwera naye Davide kwa Sauli ndipo ankamutumikira Sauliyo monga kale.
And Jonathan called David, and Jonathan showed him all those things. And Jonathan brought David to Saul, and he was in his presence as beforetime.
8 Panabukanso nkhondo ina ndipo Davide anapita ndi kukamenyana ndi Afilisti. Iye anawakantha mwamphamvu kotero kuti Afilisti anathawa.
And there was war again. And David went out, and fought with the Philistines, and killed them with a great slaughter, and they fled before him.
9 Tsiku lina mzimu woyipa uja unafikanso pa Sauli. Nthawi imeneyi nʼkuti Sauli uja ali mʼnyumba mwake, mkondo uli mʼdzanja lake ndi Davide akuyimba zeze,
And an evil spirit from Jehovah was upon Saul as he sat in his house with his spear in his hand, and David was playing with his hand.
10 Sauli anafuna kumubaya Davide ndi kumukhomera kukhoma, koma Davide anapewa mkondowo kotero Sauli anakabaya pa khoma. Usiku womwewo Davide anathawa.
And Saul sought to smite David even to the wall with the spear, but he slipped away out of Saul's presence, and he smote the spear into the wall. And David fled, and escaped that night.
11 Usiku womwewo Sauli anatumiza anthu ku nyumba ya Davide kuti akamubisalire ndi kumupha mmamawa. Koma Mikala mkazi wake anamuchenjeza nati, “Ngati usiku uno supulumutsa moyo wako, mawa udzaphedwa.”
And Saul sent messengers to David's house, to watch him, and to kill him in the morning. And Michal, David's wife, told him, saying, If thou save not thy life tonight, tomorrow thou will be slain.
12 Choncho Mikala anamutulutsira Davide pa zenera, ndipo anathawa ndi kupulumuka.
So Michal let David down through the window, and he went, and fled, and escaped.
13 Kenaka Mikala anatenga fano naligoneka pa bedi nayika pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwa fanolo ndipo analifunditsa nsalu.
And Michal took the teraphim, and laid it in the bed, and put a pillow of goats' hair at the head of it, and covered it with the clothes.
14 Pamene amithenga a Sauli aja anafika kuti akamugwire Davide, Mikala anati, “Davide akudwala.”
And when Saul sent messengers to take David, she said, He is sick.
15 Koma Sauli anatumanso anthuwo kuti akamuone Davide, nati, “Mubwere naye kuno ali pa bedi pomwepo kuti ndidzamuphe.”
And Saul sent the messengers to see David, saying, Bring him up to me in the bed, that I may kill him.
16 Koma pamene anthuwo analowa, anangoona fano pa bedipo ndi pilo wa ubweya wa mbuzi ku mutu kwake.
And when the messengers came in, behold, the teraphim was in the bed, with the pillow of goats' hair at the head of it.
17 Tsono Sauli anafunsa Mikala kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandinamiza chotere polola kuti mdani wanga athawe?” Mikala anayankha kuti, “Davide anandiwuza kuti, ‘Ukapanda kutero ndikupha.’”
And Saul said to Michal, Why have thou deceived me thus, and let my enemy go, so that he is escaped? And Michal answered Saul, He said to me, Let me go. Why should I kill thee?
18 Choncho Davide anathawa napulumuka. Pambuyo pake anapita kwa Samueli ku Rama nakamuwuza zonse zimene Sauli anamuchita. Kenaka iye ndi Samueli anapita kukakhala ku Nayoti.
Now David fled, and escaped, and came to Samuel to Ramah, and told him all that Saul had done to him. And he and Samuel went and dwelt in Naioth.
19 Sauli anamva kuti, “Davide ali ku Nayoti ku Rama.”
And it was told Saul, saying, Behold, David is at Naioth in Ramah.
20 Choncho iye anatumiza anthu kuti akamugwire Davide. Koma anaona gulu la aneneri likulosera ndi Samueli akuwatsogolera. Pomwepo Mzimu wa Mulungu unawafikira ndipo nawonso anayamba kulosera.
And Saul sent messengers to take David. And when they saw the company of the prophets prophesying, and Samuel standing as head over them, the Spirit of God came upon the messengers of Saul, and they also prophesied.
21 Sauli atamva zimenezi anatumizanso anthu ena, koma nawonso anayamba kulosa. Anatumanso anthu ena kachitatu, koma nawonso anayamba kulosa.
And when it was told Saul, he sent other messengers, and they also prophesied. And Saul sent messengers again the third time, and they also prophesied.
22 Pomaliza Sauli mwini wake ananyamuka kupita ku Rama ndipo anafika ku chitsime chachikulu cha ku Seku. Ndipo anafunsa, “Samueli ndi Davide ali kuti?” Munthu wina anamuyankha kuti, “Ali ku Nayoti ku Rama.”
Then he also went to Ramah, and came to the great well that is in Secu. And he asked and said, Where are Samuel and David? And one said, Behold, they are at Naioth in Ramah.
23 Choncho Sauli anapita ku Nayoti ku Rama. Koma Mzimu wa Mulungu unafikanso pa iye ndipo ankalosa akuyenda mpaka anafika ku Nayoti.
And he went there to Naioth in Ramah, and the Spirit of God came upon him also, and he went on, and prophesied until he came to Naioth in Ramah.
24 Nayenso anavula zovala zake nayamba kulosa pamaso pa Samueli. Kenaka anagona wamaliseche tsiku lonse ndi usiku wonse. Nʼchifukwa chake anthu amati, “Kodi Sauli alinso mmodzi wa aneneri?”
And he also stripped off his clothes, and he also prophesied before Samuel, and lay down naked all that day and all that night. Therefore they say, Is Saul also among the prophets?

< 1 Samueli 19 >