< 1 Samueli 18 >

1 Davide atatha kuyankhula ndi Sauli, mtima wa Yonatani unagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo iye ankamukonda Davide monga momwe ankadzikondera yekha.
And it came to pass, when he had made an end of speaking to Saul, that the soul of Jonathan was knit with the soul of David, and Jonathan loved him as his own soul.
2 Choncho Sauli anamusunga Davideyo kuyambira tsiku limenelo ndipo sanamulole kuti abwerere ku nyumba ya abambo ake.
And Saul took him that day, and would no more let him go home to his father's house.
3 Ndipo Yonatani anapanga pangano ndi Davide chifukwa ankamukonda monga momwe ankadzikondera.
Then Jonathan and David made a covenant, because he loved him as his own soul.
4 Yonatani anavula mkanjo umene anavala ndipo anamupatsa Davide pamodzi ndi zovala za nkhondo, lupanga, uta ndi lamba.
And Jonathan stripped himself of the robe that was upon him, and gave it to David, and his apparel, even to his sword, and to his bow, and to his belt.
5 Davide ankapita kulikonse kumene Sauli ankamutuma kuti apite kukamenya nkhondo, ndipo ankapambana. Choncho Sauli anamupatsa udindo woyangʼanira gulu lankhondo. Ichi chinakondweretsa anthu onse ngakhalenso atsogoleri a nkhondo a Sauli.
And David went out wherever Saul sent him, and behaved himself wisely. And Saul set him over the men of war, and it was good in the sight of all the people, and also in the sight of Saul's servants.
6 Anthu akubwerera kwawo Davide atapha Mfilisiti uja, amayi anatuluka mʼmizinda yonse ya Israeli, akuyimba ndi kuvina kukachingamira mfumu Sauli. Ankayimba ndi kuvina mokondwa, kwinaku ngʼoma ndi zitoliro zikulira.
And it came to pass as they came, when David returned from the slaughter of the Philistine, that the women came out of all the cities of Israel, singing and dancing, to meet king Saul, with timbrels, with joy, and with instruments of music.
7 Amayiwo ankalandizana nyimbo mokondwera namati: “Sauli wapha 1,000, Koma Davide wapha miyandamiyanda.”
And the women sang one to another as they played, and said, Saul has slain his thousands, and David his ten thousands.
8 Koma Sauli anapsa mtima kwambiri ndipo mawu amenewa anamuyipira. Iye anati, “Iwo amuwerengera Davide miyandamiyanda, koma ine 1,000 okha. Nanga chatsalanso nʼchiyani kuti atenge? Si ufumu basi?”
And Saul was very angry, and this saying displeased him, and he said, They have ascribed to David ten thousands, and to me they have ascribed but thousands, and what can he have more but the kingdom?
9 Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.
And Saul eyed David from that day and forward.
10 Mmawa mwake mzimu woyipa uja unabwera mwamphamvu pa Sauli. Sauli anayamba kubwebweta mʼnyumba mwake. Davide ankamuyimbira zeze monga nthawi zonse. Sauli anali ndi mkondo mʼdzanja lake.
And it came to pass on the morrow, that an evil spirit from God came mightily upon Saul, and he prophesied in the midst of the house. And David played with his hand, as he did day by day, and Saul had his spear in his hand.
11 Tsono anawuponya mkondowo, namati mu mtima mwake, “Ndimubaya Davide ndi kumukhomera ku khoma.” Koma Davide anawulewa kawiri konse.
And Saul cast the spear, for he said, I will smite David even to the wall. And David turned away from his presence twice.
12 Pambuyo pake Sauli amamuopa Davide chifukwa Yehova anali ndi Davideyo, nʼkumusiya Sauli.
And Saul was afraid of David because Jehovah was with him, and was departed from Saul.
13 Kotero Sauli anamuchotsa Davide pamaso pake ndi kumuyika kukhala mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Choncho Davide ankapita ndi kubwera akutsogolera ankhondowa.
Therefore Saul removed him from him, and made him his captain over a thousand, and he went out and came in before the people.
14 Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye.
And David behaved himself wisely in all his ways, and Jehovah was with him.
15 Sauli ataona momwe Davide ankapambanira, iye anamuopa kwambiri.
And when Saul saw that he behaved himself very wisely, he was afraid of him.
16 Koma Aisraeli onse ndi anthu a Yuda ankamukonda Davide chifukwa ankawatsogolera pa nkhondo zawo.
But all Israel and Judah loved David, for he went out and came in before them.
17 Tsiku lina Sauli anawuza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkazi wamkulu. Ine ndakupatsa kuti umukwatire. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Yehova.” Poteropo Sauli ankanena kuti, “Ndisamuphe ndi manja angawa koma aphedwe ndi Afilisti!”
And Saul said to David, Behold, my elder daughter Merab, I will give her to thee for a wife. Only be thou valiant for me, and fight Jehovah's battles. For Saul said, Let not my hand be upon him, but let the hand of the Philistines be upon him.
18 Ndipo Davide anati kwa Sauli, “Ine ndine yani, ndipo abale anga kapena banja la abambo anga ndife yani mʼdziko la Israeli kuti ndikhale mpongozi wa mfumu?”
And David said to Saul, Who am I, and what is my life, or my father's family in Israel, that I should be son-in-law to the king?
19 Koma pa nthawi yoti Merabi mwana wa Sauli akwatiwe ndi Davide, Sauli anamupereka kwa Adrieli wa ku Mehola kuti amukwatire.
But it came to pass at the time when Merab, Saul's daughter, should have been given to David, that she was given to Adriel the Meholathite to wife.
20 Koma Mikala mwana wamkazi wa Sauli anamukonda Davide ndipo Sauli atamva za zimenezi, anakondwera.
And Michal, Saul's daughter, loved David, and they told Saul, and the thing pleased him.
21 Sauli ankaganiza kuti, “Ndimupatse amukwatire kuti akhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo adzaphedwe ndi Afilisti.” Choncho Sauli anawuza Davide kachiwiri, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”
And Saul said, I will give him her, that she may be a snare to him, and that the hand of the Philistines may be against him. Therefore Saul said to David, Thou shall this day be my son-in-law a second time.
22 Sauli analamulanso nduna zake kuti, “Muyankhuleni Davide mwamseri ndi kumuwuza kuti, ‘Taona, mfumu imakondwera nawe, ndipo nduna zake zonse zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’”
And Saul commanded his servants, saying, Converse with David secretly, and say, Behold, the king has delight in thee, and all his servants love thee. Now therefore be the king's son-in-law.
23 Iwo anakamuwuza Davide mawu amenewa, koma Davide anati, “Kodi inu mukuganiza kuti ndi chinthu chapafupi kukhala mpongozi wa mfumu? Ine ndine wosauka ndiponso wosatchuka.”
And Saul's servants spoke those words in the ears of David. And David said, Does it seem to you a light thing to be the king's son-in-law, seeing that I am a poor man, and lightly esteemed?
24 Nduna za Sauli zinamuwuza zonse zimene anayankha Davide.
And the servants of Saul told him, saying, On this manner David spoke.
25 Sauli anayankha kuti, “Kamuwuzeni Davide kuti, ‘Mfumu sikufuna malowolo a mtundu wina uliwonse koma timakungu ta msonga za mavalo a Afilisti 100 kuti ilipsire adani ake.’” Maganizo a Sauli anali akuti Davide aphedwe ndi Afilisti.
And Saul said, Thus shall ye say to David, The king does not desire any dowry, but a hundred foreskins of the Philistines, to be avenged of the king's enemies. Now Saul thought to make David fall by the hand of the Philistines.
26 Nduna za Saulizo zitamuwuza Davide zimenezi, anakondwera kuti akhale mpongozi wa mfumu. Koma nthawi imene anapatsidwa isanathe,
And when his servants told David these words, it pleased David well to be the king's son-in-law. And the days were not expired.
27 Davide ndi anyamata ake anapita ndi kukapha Afilisti 200. Iye anabwera ndi timakungu tija natipereka tonse kwa mfumu kuti akhale mpongozi wa mfumu. Kotero Sauli anapereka mwana wake wamkazi, Mikala, kwa Davide kuti amukwatire.
And David arose and went, he and his men, and killed of the Philistines two hundred men. And David brought their foreskins, and they gave them in full number to the king, that he might be the king's son-in-law. And Saul gave him Michal his daughter to wife.
28 Sauli atazindikira kuti Yehova anali ndi Davide ndiponso kuti mwana wake Mikala amamukonda Davide,
And Saul saw and knew that Jehovah was with David, and Michal, Saul's daughter, loved him.
29 iye anapitirirabe kumuopa Davide ndi kumadana naye moyo wake wonse.
And Saul was yet the more afraid of David, and Saul was David's enemy continually.
30 Nthawi zonse pamene atsogoleri a Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, Davide ankapambana kuposa nduna zonse za Sauli. Choncho dzina lake linatchuka kwambiri.
Then the rulers of the Philistines went forth, and it came to pass, as often as they went forth, that David behaved himself more wisely than all the servants of Saul, so that his name was very precious.

< 1 Samueli 18 >