< 1 Samueli 20 >

1 Tsono Davide anathawa ku Nayoti ku Rama ndi kupita kwa Yonatani ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ine ndinachita chiyani? Kodi ndinalakwa chiyani? Kodi abambo ako ndinawalakwira chiyani kuti azifuna kundipha?”
And David fled from Naioth in Ramah, and came and said before Jonathan, What have I done? What is my iniquity, and what is my sin before thy father, that he seeks my life?
2 Yonatani anayankha kuti, “Sizitheka! Iwe sufa ayi! Taona abambo anga sachita chinthu chilichonse chachikulu kapena chachingʼono wosandiwuza ine. Tsopano abambo anga angandibisire bwanji zimenezi? Sichoncho ayi.”
And he said to him, Far from it. Thou shall not die. Behold, my father does nothing either great or small, but that he discloses it to me, and why should my father hide this thing from me? It is not so.
3 Koma Davide analumbira kuti, “Abambo ako akudziwa bwino lomwe kuti iwe umandikonda ndipo iwo amaganiza kuti, Yonatani sayenera kudziwa zimenezi mwina adzamva chisoni kwambiri. Komabe, pali Yehova ndi pali iwe, imfa sinanditalikire.”
And David swore moreover, and said, Thy father knows well that I have found favor in thine eyes, and he says, Let not Jonathan know this, lest he be grieved. But truly as Jehovah lives, and as thy soul lives, there is but a step between me and death.
4 Yonatani anawuza Davide kuti, “Chilichonse chimene iwe ukufuna kuti ndichite, ndidzakuchitira.”
Then Jonathan said to David, Whatever thy soul desires, I will even do it for thee.
5 Ndipo Davide anati, “Taona mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano, ndipo ine ndiyenera kukadya ndi mfumu. Koma undilole ndipite ndikabisale mʼmunda mpaka mkuja madzulo.
And David said to Jonathan, Behold, tomorrow is the new moon, and I should not fail to sit with the king to eat. But let me go that I may hide myself in the field to the third day at evening.
6 Ngati abambo ako akafunsa za ine, ukawawuze kuti, ‘Davide anandiwumiriza kuti ndimulole apite msanga kwawo ku Betelehemu, chifukwa akupereka nsembe yapachaka ya banja lonse.’
If thy father misses me at all, then say, David earnestly asked leave of me that he might run to Bethlehem his city, for it is the yearly sacrifice there for all the family.
7 Akanena kuti, ‘Wachita bwino,’ ndiye kuti zinthu zindiyendera bwino ine mtumiki wako. Koma ngati akapsa mtima, ndiye udziwe kuti iwo atsimikiza zondichita zoyipa.
If he says thus, It is well. Thy servant shall have peace. But if he is angry, then know that evil is determined by him.
8 Koma undikomere mtima ine mtumiki wako, pakuti unapangana nane pangano pamaso pa Yehova. Ngati ndine wolakwa undiphe ndiwe, koma usandipereke kwa abambo ako.”
Therefore deal kindly with thy servant, for thou have brought thy servant into a covenant of Jehovah with thee. But if there be in me iniquity, kill me thyself, for why should thou bring me to thy father?
9 Yonatani anati, “Sizitheka! Ndikanadziwa kuti abambo anga atsimikiza kuti akuchite choyipa, kodi sindikanakuwuza?”
And Jonathan said, Far be it from thee, for if I should at all know that evil were determined by my father to come upon thee, then would I not tell it to thee?
10 Davide anafunsa kuti, “Adzandiwuza ndani ngati abambo ako akuyankhe mwaukali?”
Then David said to Jonathan, Who shall tell me if perchance thy father answers thee roughly?
11 Yonatani anawuza Davide kuti, “Tiyeni tikayende ku mundako.” Ndipo anapita onse awiri.
And Jonathan said to David, Come, and let us go out into the field. And they went out both of them into the field.
12 Kenaka Yonatani anawuza Davide kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akhale mboni! Ine ndikadzafunsa abambo anga nthawi yonga ino mmawa kapena mkuja, ndipo ndikadzapeza kuti akukufunira zabwino, ine ndidzatuma mawu kuti udziwe.
And Jonathan said to David, Jehovah, the God of Israel-when I have sounded my father about this time tomorrow, or the third day, behold, if there be good toward David, shall I not then send to thee, and disclose it to thee?
13 Koma ngati abambo anga atsimikiza kukuchita choyipa, Yehova andilange ine Yonatani, ndipotu kwambiri ngati sindidzakudziwitsa ndi kukulola kuti upite mu mtendere. Yehova akhale nawe monga anakhalira ndi abambo anga.
Jehovah do so to Jonathan, and more also, should it please my father to do thee evil, if I not disclose it to thee, and send thee away that thou may go in peace. And Jehovah be with thee as he has been with my father.
14 Ndikakhalabe ndi moyo udzandionetse kukoma mtima monga kwa Yehova nthawi yonse ya moyo wanga, kuti ine ndisaphedwe.
And thou shall not only show me the loving kindness of Jehovah, while I yet live, that I not die,
15 Ndipo usadzaleke kuchitira chifundo banja langa. Pamene Yehova adzawatha adani onse a Davide pa dziko lapansi.”
but also thou shall not cut off thy kindness from my house forever. No, not when Jehovah has cut off the enemies of David every one from the face of the earth.
16 “Dzina la ine Yonatani lisadzafafanizidwe nawo pamodzi. Yehova alange adani onse a Davide.”
So Jonathan made a covenant with the house of David, saying, And Jehovah will require it at the hand of David's enemies.
17 Kenaka Yonatani anamulumbiritsanso Davide kuti asaleke kumukonda, pakuti ankamukonda monga ankadzikondera yekha.
And Jonathan caused David to swear again, for the love that he had to him. For he loved him as he loved his own soul.
18 Kenaka Yonatani anawuzanso Davide kuti, “Mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. Zidzadziwika kuti iwe palibe chifukwa mpando wako udzakhala wopanda munthu.
Then Jonathan said to him, Tomorrow is the new moon, and thou will be missed because thy seat will be empty.
19 Mkuja adzakufunafuna. Tsono udzapite pamalo pamene unabisala poyamba paja ndipo ukadikire pa mulu wa miyala uli apowo.
And when thou have stayed three days, thou shall go down quickly, and come to the place where thou hid thyself when the business was in hand, and shall remain by the stone Ezel.
20 Ine ndidzaponya mivi itatu pambali pake, ngati ndikulasa chinthu.
And I will shoot three arrows on the side of it, as though I shot at a mark.
21 Ndipo ndidzatuma mnyamata ndi kuti, ‘Pita ukatole miviyo!’ Ngati ndidzanena kwa iye kuti, ‘Taona, mivi ili mbali yakuno, kayitole,’ iwe ukatuluke, pakuti ndikulumbira, pali Yehova Wamoyo, ndiye kuti zako zili bwino, palibe choopsa chilichonse.
And, behold, I will send the lad, saying, Go, find the arrows. If I say to the lad, Behold, the arrows are on this side of thee, take them, and come, for there is peace to thee and no hurt, as Jehovah lives.
22 Koma ndikadzati, ‘Taona mivi ili patsogolo pako,’ iwe udzachoke chifukwa Yehova ndiye walola kuti uchokepo.
But if I say thus to the boy, Behold, the arrows are beyond thee, go thy way, for Jehovah has sent thee away.
23 Tsono zimene tapanganazi Yehova ndiye mboni pakati pa iwe ndi ine mpaka muyaya.”
And concerning the matter which thou and I have spoken of, behold, Jehovah is between thee and me forever.
24 Choncho Davide anakabisala mʼmunda ndipo nthawi ya chikondwerero cha mwezi watsopano itakwana mfumu Sauli anadzakhala pansi kuti adye.
So David hid himself in the field. And when the new moon came, the king sat down to eat food.
25 Iye anakhala pa malo ake a nthawi zonse pafupi ndi khoma moyangʼanana ndi Yonatani, ndipo Abineri anakhala moyandikana ndi Sauli, koma pa malo a Davide panalibe munthu.
And the king sat upon his seat, as at other times, even upon the seat by the wall, and Jonathan stood up, and Abner sat by Saul's side, but David's place was empty.
26 Sauli sananene chilichonse tsiku limenelo pakuti ankaganiza kuti “Chilipo chimene chachitika ndi Davide. Mwina mwake ngosayenera za chipembedzo.”
Nevertheless Saul spoke nothing that day, for he thought, Something has befallen him. He is not clean. Surely he is not clean.
27 Koma pa tsiku lachiwiri la chikondwerero cha mwezi watsopano pamalo pa Davide panalibenso munthu. Kenaka Sauli anafunsa Yonatani kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwana wa Yese sanabwere kudzadya, dzulo ngakhale lero?”
And it came to pass on the morrow after the new moon, which was the second day, that David's place was empty. And Saul said to Jonathan his son, Why has the son of Jesse not come in to the food, neither yesterday, nor today?
28 Yonatani anayankha kuti, “Davide anandiwumiriza kuti ndimulole kuti apite ku Betelehemu.
And Jonathan answered Saul, David earnestly asked leave of me to go to Bethlehem.
29 Anati, ‘Undilole ndipite, chifukwa banja lathu likupereka nsembe mu mzindamo ndipo mʼbale wanga wandiwumiriza kuti ndikakhale nawo. Ngati wandikomera mtima, chonde ndilole ndipite ndikaone abale anga.’ Nʼchifukwa chake sanabwere kudzadya ndi mfumu.”
And he said, Let me go, I pray thee, for our family has a sacrifice in the city, and my brother, he has commanded me. And now, if I have found favor in thine eyes, let me get away, I pray thee, and see my brothers. Therefore he has not come to the king's table.
30 Sauli anamupsera mtima Yonatani ndipo namuwuza kuti, “Iwe mwana wobadwa mwa mkazi wamakhalidwe oyipa ndi wowukira! Kodi ukuyesa kuti ine sindikudziwa kuti umagwirizana ndi mwana wa Yese, amene akufuna kukuchititsa manyazi iwe ndi amayi ako?
Then Saul's anger was kindled against Jonathan, and he said to him, Thou son of a perverse rebellious woman, do I not know that thou have chosen the son of Jesse to thine own shame, and to the shame of thy mother's nakedness?
31 Mwana wa Yese akakhala ndi moyo pa dziko lapansi lino, iwe sudzakhala mfumu. Tsopano tumiza munthu akamutenge kubwera naye kwa ine, pakuti Davide ayenera kufa basi!”
For as long as the son of Jesse lives upon the ground, thou shall not be established, nor thy kingdom. Therefore now send and fetch him to me, for he shall surely die.
32 Yonatani anafunsa abambo ake kuti, “Nʼchifukwa chiyani mufuna kuti Davide aphedwe? Iye walakwa chiyani?”
And Jonathan answered Saul his father, and said to him, Why should he be put to death? What has he done?
33 Apo Sauli anamuponyera mkondo wake kuti amuphe. Tsono Yonatani anadziwa kuti abambo ake atsimikiza mtima kuti aphe Davide.
And Saul cast his spear at him to smite him. By this Jonathan knew that it was determined by his father to put David to death.
34 Yonatani anachoka pa tebulopo ali wopsa mtima kwambiri. Tsiku lachiwiri la chikondwererocho Yonatani sanadye chakudya. Iye anawawidwa mtima chifukwa abambo ake anatsimikiza zakupha Davide.
So Jonathan arose from the table in fierce anger, and ate no food the second day of the month, for he was grieved for David because his father had done him shame.
35 Tsono mmawa Yonatani anapita ku munda kumene anapangana ndi Davide. Anali ndi mnyamata wake.
And it came to pass in the morning, that Jonathan went out into the field at the time appointed with David, and a little lad with him.
36 Tsono anawuza mnyamatayo kuti, “Thamanga ukatole muvi umene nditi ndiponye.” Mnyamatayo akuthamanga Yonatani anaponya muvi patsogolo pa mnyamatayo.
And he said to his lad, Run, now find the arrows which I shoot. And as the lad ran, he shot an arrow beyond him.
37 Mnyamatayo atafika pamene muvi wa Yonatani unagwera,
And when the lad was come to the place of the arrow which Jonathan had shot, Jonathan cried after the lad, and said, Is not the arrow beyond thee?
38 Yonatani anayitananso mnyamatayo kuti, “Fulumira, pita msanga usayime.” Choncho mnyamatayo anatola muvi uja ndi kubwera nayo kwa mbuye wake.
And Jonathan cried after the lad, Make speed, haste, stay not. And Jonathan's lad gathered up the arrows, and came to his master.
39 (Mnyamatayo sanadziwe chimene chimachitika koma Yonatani ndi Davide ndiwo ankadziwa).
But the lad knew nothing. Only Jonathan and David knew the matter.
40 Pambuyo pake Yonatani anapereka zida zake za nkhondo kwa mnyamatayo ndipo anati, “Pita, nyamula ubwerere nazo ku mzinda.”
And Jonathan gave his weapons to his lad, and said to him, Go, carry them to the city.
41 Mnyamatayo anapita. Kenaka Davide anatuluka ku mbali ina ya mulu wa miyala uja, nadzigwetsa pansi ndi kugunditsa nkhope yake pansi katatu. Anapsompsona nayamba kulira onse awiri, koma Davide analira kwambiri.
And as soon as the lad was gone, David arose out of a place toward the South, and fell on his face to the ground, and bowed himself three times. And they kissed each other, and wept one with another until David surpassed him.
42 Yonatani anawuza Davide kuti, “Pita mu mtendere pakuti ife awiri tinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Yehova ndiye akhale mboni pakati pa iwe ndi ine ndiponso pakati pa zidzukulu zako ndi zidzukulu zanga kwa nthawi yonse.’” Kenaka Davide anachoka, ndipo Yonatani anabwerera ku mzinda kuja.
And Jonathan said to David, Go in peace, inasmuch as we have sworn both of us in the name of Jehovah, saying, Jehovah shall be between me and thee, and between my seed and thy seed, forever. And he arose and departed, and Jonathan went into the city.

< 1 Samueli 20 >