< До Тита 3 >

1 Нагадуй їм, щоб слухали вла́ди верховної та кори́лися їй, і до всякого доброго ді́ла готові були́,
Uwakumbutse anthu kuti azigonjera oweruza ndi olamulira, aziwamvera ndi kukhala okonzeka kuchita chilichonse chabwino.
2 щоб не зневажали ніко́го, щоб були́ не сварли́ві, а тихі, виявляючи повну ла́гідність усім лю́дям.
Asamachitire chipongwe aliyense, asamakangane, akhale ofatsa ndipo oganizira ena, ndipo nthawi zonse akhale aulemu kwa anthu onse.
3 Бо колись були й ми нерозсудні, неслухня́ні, зве́дені, служили різним пожадли́востям та розкошам, жили в злобі та в за́здрощах, бридки́ми були, нена́виділи один о́дного.
Nthawi ina tinali opusa, osamvera, onamizidwa ndi omangidwa ndi zilakolako ndi zokondweretsa zamitundumitundu. Tinkakhala moyo wadumbo ndi wakaduka, odedwa ndiponso odana wina ndi mnzake.
4 А коли з'явилась благодать та люди́нолюбство Спасителя, нашого Бога,
Koma kukoma mtima ndi chikondi cha Mulungu Mpulumutsi wathu chitaonekera,
5 Він нас спас не з діл праведности, що ми їх учинили були́, а з Своєї милости через обмиття відро́дження й обно́влення Духом Святим,
Iye anatipulumutsa, osati chifukwa cha ntchito zathu zolungama zimene tinachita koma chifukwa cha chifundo chake. Anatipulumutsa potisambitsa, kutibadwitsa kwatsopano ndi kutikonzanso mwa Mzimu Woyera
6 Якого Він щедро вилив на нас через Христа Ісуса, Спасителя нашого,
amene anatipatsa mowolowamanja kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu,
7 щоб ми виправдались Його благодаттю, і стали спадкоє́мцями за надією на вічне життя. (aiōnios g166)
kuti titalungamitsidwa mwachisomo chake, tikhale olowamʼmalo okhala ndi chiyembekezo cha moyo wosatha. (aiōnios g166)
8 Вірне слово, і я хочу, щоб ти і про це впевня́в, щоб ті, хто ввірував у Бога, дба́ли про добрі діла пильнувати. Для людей оце добре й кори́сне!
Mawuwa ndi okhulupirika ndipo ine ndikufuna kuti iwe utsindike zinthu izi, kuti amene akhulupirira Mulungu adzipereke kuchita ntchito zabwino. Zinthu izi ndi zabwino kwambiri ndi zopindulitsa kwa aliyense.
9 Вистерігайсь нерозумних змага́нь, і родоводів, і спорів, і супере́чок про Зако́н, — бо вони некори́сні й марні́.
Koma upewe kufufuzafufuza zopusa, kuwerengawerenga mndandanda wa mibado ya makolo, mikangano ndi mitsutso pa za Malamulo, chifukwa zimenezi ndi zosapindulitsa ndi zopanda pake.
10 Люди́ни єретика, по першім та другім наставленні, відрікайся,
Munthu woyambitsa mipatuko umuchenjeze koyamba, ndiponso umuchenjeze kachiwiri. Kenaka umupewe.
11 знавши, що зіпсувся такий та грішить, і він сам себе засудив.
Iwe udziwe kuti munthu wotero ngosokoneza ndi wochimwa, ndipo akudzitsutsa yekha.
12 Як пришлю я до тебе Арте́ма або Тихи́ка, поква́пся прибути до мене в Нікопо́ль, бо думаю там перези́мувати.
Ndikadzamutuma Artema kapena Tukiko kwanuko, udzayesetse kundipeza ku Nikapoli, chifukwa ndatsimikiza kukhala kumeneko pa nthawi yozizira.
13 Зако́нника Зи́ну та Аполло́са вишли ква́пливо вперед, щоб для них не забракло нічо́го.
Uyesetse chilichonse ungathe kuthandiza Zena katswiri wa malamulo ndi Apolo, kuti apitirize ulendo wawo, ndipo uwonetsetse asasowe kanthu.
14 Нехай же навчаються й наші дбати про добрі діла при конечних потребах, щоб безплодні вони не були́.
Anthu athu aphunzire kudzipereka pogwira ntchito zabwino, nʼcholinga chakuti athandize zinthu zimene zikufunika msangamsanga. Ndipo asakhale moyo osapindulitsa.
15 Вітають тебе всі, хто зо мною. Вітай тих, хто любить нас у вірі. Благода́ть з вами всіма́! Амі́нь.
Onse amene ali ndi ine akupereka moni. Upereke moni kwa amene amatikonda ife mʼchikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.

< До Тита 3 >