< До Филимона 1 >

1 Павло, в'я́зень Христа Ісуса, та брат Тимофій, улю́бленому Филимо́нові й співробі́тникові нашому,
Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu. Kulembera Filemoni, bwenzi lathu lokondedwa ndi mtumiki mnzathu.
2 і сестрі любій Апфі́ї, і співвойо́вникові нашому Архи́пові, і Церкві домашній твоїй:
Kwa Apiya mlongo wathu, Arkipo msilikali mnzathu, ndiponso mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwanu.
3 благодать вам і мир від Бога Отця нашого й Господа Ісуса Христа!
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
4 Я за́всіди дякую Богові моє́му, коли тебе згадую в молитвах своїх.
Ine ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakukumbukira iwe mʼmapemphero anga.
5 Бо я чув про любов твою й віру, яку маєш до Господа Ісуса, і до всіх святих,
Pakuti ndamva za chikondi chako, za chikhulupiriro chako mwa Ambuye Yesu ndiponso za chikondi chako pa oyera mtima onse.
6 щоб спільність віри твоєї дія́льна була в пізна́нні всякого добра, що в нас для Христа.
Ine ndikupemphera kuti mgwirizano wako ndi ife mʼchikhulupiriro ukhale opindulitsa pozamitsa nzeru zako zozindikira zinthu zilizonse zabwino zimene timagawana chifukwa cha Khristu.
7 Бо ми маємо радість велику й потіху в любові твоїй, серця́ бо святих заспоко́їв ти, брате.
Mʼbale, chikondi chako chandipatsa chimwemwe chachikulu ndi chilimbikitso, chifukwa umatsitsimutsa mitima ya anthu a Ambuye.
8 Через це, хоч я маю велику відвагу в Христі подавати нака́зи тобі про потрібне,
Tsopano ngakhale kuti mwa Khristu nditha kulimba mtima ndi kulamulira kuti uchite zimene uyenera kuchita,
9 але більше з любови благаю я, як Павло, стари́й, тепер же ще й в'язень Христа Ісуса.
komabe ndikupempha mwachikondi. Ine Paulo, munthu wokalamba, ndipo tsopano ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu,
10 Благаю тебе про сина свого, про Они́сима, що його породив я в кайда́нах своїх.
ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.
11 Колись то для тебе він був непотрібний, тепер же для тебе й для мене він дуже потрібний.
Anali wopanda phindu kwa iwe, koma tsopano wasanduka wa phindu kwa iwe ndi kwa inenso.
12 Тобі я вертаю його, того, хто є неначе серце моє.
Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.
13 Я хотів був тримати його при собі, щоб він замість тебе мені послужив у кайда́нах за Єва́нгелію,
Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.
14 та без волі твоєї нічо́го робити не хотів я, щоб твій добрий учинок не був ніби ви́мушений, але добровільний.
Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, nʼcholinga chakuti chilichonse chabwino ungandichitire chikhale mwakufuna kwako osati mokakamiza.
15 Бо може для того він був розлучився на час, щоб навіки прийняв ти його, (aiōnios g166)
Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios g166)
16 і вже не як раба, але вище від раба, — як брата улю́бленого, особливо для мене, а тим більше для тебе, — і за ті́лом, і в Го́споді.
Osati ngati kapolo, koma woposa kapolo, ngati mʼbale wokondedwa. Iyeyu ndi wokondedwa kwambiri kwa ine koma kwa iweyo ndi wokondedwa koposa, ngati munthu komanso ngati mʼbale mwa Ambuye.
17 Отож, коли маєш за друга мене, то прийми його, як мене.
Tsono ngati umati ndine mnzako, umulandire iyeyu monga momwe ukanandilandirira ineyo.
18 Коли ж він чим скри́вдив тебе або винен тобі, — полічи це мені.
Ngati anakulakwira kapena kukongola kanthu kalikonse, ndidzalipira ineyo.
19 Я, Павло, написав це рукою своєю: „Я віддам“, щоб тобі не казати, що ти навіть само́го себе мені винен.
Ine, Paulo ndikulemba zimenezi ndi dzanja langa. Ine ndidzalipira. Nʼkosafunika kukukumbutsa kuti iweyo ngongole yako kwa ine ndi moyo wakowo.
20 Так, брате, — нехай я оде́ржу те, що від тебе прохаю в Го́споді. Заспокой моє серце в Христі!
Mʼbale, ndikufuna kuti ndipindule nawe mwa Ambuye; tsono tsitsimutsa mtima wanga mwa Khristu.
21 Пересвідчений я про слухня́ність твою, і тобі написав оце, відаючи, що ти зробиш і більше, ніж я говорю́.
Ine ndili ndi chitsimikizo cha kumvera kwako pamene ndikukulembera kalatayi. Ndikulemba ndikudziwa kuti udzachita ngakhale kuposa zimene ndakupemphazi.
22 А ра́зом мені приготуй і поме́шкання, бо наді́юся я, що за ваші моли́тви я буду дарований вам.
Chinthu chinanso ndi ichi: undikonzere malo, chifukwa ndikukhulupirira kuti Mulungu adzamvera mapemphero anu ndi kundibwezera kwa inu.
23 Вітає тебе Епафра́с, мій співв'я́зень у Христі Ісусі,
Epafra, wamʼndende mnzanga chifukwa cha Khristu Yesu akupereka moni.
24 Ма́рко, Ариста́рх, Дима́с, Лука́, — мої співробі́тники.
Atumiki anzanga awa, Marko, Aristariko, Dema ndi Luka, akuperekanso moni.
25 Благода́ть Господа Ісуса Христа з вашим духом! Амі́нь.
Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wako.

< До Филимона 1 >