< До євреїв 13 >

1 Братолю́бство нехай пробува́є між вами!
Pitirizani kukondana monga abale.
2 Не забувайте любови до при́ходнів, бо деякі нею, на́віть не ві́даючи, гостинно прийняли а́нголів.
Musayiwale kusamalira alendo, pakuti pochita zimenezi anthu ena anasamalira angelo amene samawadziwa.
3 Пам'ятайте про в'я́знів, немов із ними були б ви пов'язані, про тих, хто страждає, як такі, що й самі ви знахо́дитесь в тілі.
Muzikumbukira amene ali mʼndende ngati kuti inunso ndi omangidwa, ndiponso amene akusautsidwa ngati inunso mukuvutika.
4 Нехай буде в усіх че́сний шлюб та ложе непоро́чне, а блу́дників та пере́любів судитиме Бог.
Ukwati muziwulemekeza nonse, ndipo mwamuna ndi mkazi azikhala wokhulupirika, pakuti anthu adama ndi achigololo Mulungu adzawalanga.
5 Будьте життям не грошолюбні, задовольняйтеся тим, що́ маєте. Сам бо сказав: „Я тебе не покину, ані не відступлю́ся від тебе!“
Mtima wanu usakonde ndalama koma mukhutitsidwe ndi zimene muli nazo, chifukwa Mulungu anati, “Sadzakusiyani, kapena kukutayani konse.”
6 Тому́ то ми сміливо говоримо: „Господь — мені Помічни́к, і я не злякаюсь ніко́го: що зробить люди́на мені?“
Kotero ife tikunena molimba mtima kuti, “Ambuye ndiye mthandizi wanga; sindidzachita mantha. Munthu angandichitenji ine?”
7 Спогадуйте наставників ваших, що вам говорили Слово Боже; і, дивлячися на кінець їхнього життя, переймайте їхню віру.
Muzikumbukira atsogoleri anu, amene amakulalikirani Mawu a Mulungu. Ganizirani zamoyo wawo ndipo tsatirani chikhulupiriro chawo.
8 Ісус Христос учора, і сьогодні, і навіки Той Са́мий! (aiōn g165)
Yesu Khristu ndi yemweyo dzulo, lero ndi kunthawi zonse. (aiōn g165)
9 Не захоплюйтеся всілякими та чужими науками. Бо річ добра зміцняти серця благода́ттю, а не стра́вами, що ко́ристи від них не оде́ржали ті, хто за ними ходив.
Musasocheretsedwe ndi ziphunzitso zosiyanasiyana zachilendo. Nʼkwabwino kuti mitima yathu ilimbikitsidwe ndi chisomo osati ndi chakudya, chimene sichipindulitsa iwo amene amachidya.
10 Маємо же́ртівника, що від нього годуватися права не мають ті, хто скинії служить, —
Ife tili ndi guwa lansembe, ndipo ansembe otumikira mʼtenti cha Ayuda, saloledwa kudya zochokera pamenepo.
11 бо котри́х звірят кров первосвященик уносить до святині за гріхи, тих м'ясо па́литься поза табо́ром, —
Mkulu wa ansembe amatenga magazi kukapereka nsembe chifukwa cha machimo, koma nyamayo imawotchedwa kunja kwa msasa.
12 тому́ то Ісус, щоб кров'ю Своєю людей освятити, постраждав поза брамою.
Nʼchifukwa chakenso Yesu anafera kunja kwa mzinda kuti ayeretse anthu ake kudzera mʼmagazi ake.
13 Тож виходьмо до Нього поза та́бір, і наругу Його понесімо,
Tiyeni tsono, tipite kwa iye kunja kwa msasa, titasenza chitonzo chake.
14 бо постійного міста не маємо тут, а шукаємо майбутнього!
Pakuti ife tilibe mzinda wokhazikika koma tikudikira mzinda umene ukubwera.
15 Отож, за́вжди приносьмо Богові жертву хвали́, цебто плід уст, що Ім'я́ Його славлять.
Tsono, tiyeni kudzera mwa Yesu tipereke nsembe zachiyamiko kwa Mulungu osalekeza, chipatso cha milomo imene imavomereza dzina lake.
16 Не забувайте ж і про доброчинність та спільність, бо жертви такі вгодні Богові.
Ndipo musayiwale kumachita zabwino ndi kuthandiza ena, pakuti Mulungu amakondwera ndi nsembe zotere.
17 Слухайтесь ваших наставників та коріться їм, — вони бо пильнують душ ваших, як ті, хто має здати справу. Нехай вони роблять це з радістю, а не зідхаючи, — бо це для вас не кори́сне.
Muzimvera atsogoleri anu ndi kugonjera ulamuliro wawo, iwo amakuyangʼanirani monga anthu amene adzayenera kufotokoza za ntchito yawo pamaso pa Mulungu. Muziwamvera kuti agwire ntchito yawo ndi chimwemwe osati molemedwa pakuti izi sizingakupindulireni.
18 Моліться за нас, бо наді́ємося, що ми маємо добре сумління, бо хочемо добре в усьому пово́дитись.
Mutipempherere ifenso. Pakuti tikutsimikiza kuti tili ndi chikumbumtima changwiro ndipo timafuna kuchita zinthu zonse mwaulemu.
19 А надто прошу́ це робити, щоб шви́дше до вас мене ве́рнено.
Ine ndikukupemphani kuti mundipempherere kuti Mulungu andibwezere kwa inu msanga.
20 Бог же миру, що з мертвих підняв великого Па́стиря вівцям кров'ю вічного заповіту, Господа нашого Ісуса, (aiōnios g166)
Mulungu wamtendere, amene kudzera mʼmagazi a pangano lamuyaya anaukitsa Ambuye athu Yesu kwa akufa, amene ndi Mʼbusa wamkulu, (aiōnios g166)
21 нехай вас удоскона́лить у кожному доброму ділі, щоб волю чинити Його, чинячи в вас любе перед лицем Його через Ісуса Христа, Якому слава на віки вічні. Амі́нь. (aiōn g165)
akupatseni chilichonse chabwino kuti muchite chifuniro chake ndipo Mulungu achite mwa ife, chimene chingamukomere kudzera mwa Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero ku nthawi zanthawi, Ameni. (aiōn g165)
22 Благаю ж вас, браття, прийміть слово поті́хи, бо коротко я написав вам.
Ndikukupemphani abale kuti mulandire mawu anga achilimbikitso, pakuti ndakulemberani mwachidule.
23 Знайте, що наш брат Тимофі́й вже ви́пущений, і я з ним; коли незаба́ром він при́йде, я вас побачу.
Ine ndikufuna kuti inu mudziwe kuti mʼbale wathu Timoteyo wamasulidwa. Ngati iye angafike msanga ndibwera naye kudzakuonani.
24 Вітайте всіх ваших наставників та всіх святих. Вітають вас ті, хто в Італії.
Mupereke moni kwa atsogoleri anu onse ndiponso kwa anthu onse a Mulungu. Abale ochokera ku Italiya akupereka moni.
25 Благодать зо всіма́ вами! Амі́нь.
Chisomo chikhale ndi inu nonse.

< До євреїв 13 >