< Proverbios 24 >

1 NO tengas envidia de los hombres malos, ni desees estar con ellos:
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 Porque su corazón piensa en robar, é iniquidad hablan sus labios.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 Con sabiduría se edificará la casa, y con prudencia se afirmará:
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 Y con ciencia se henchirán las cámaras de todo bien preciado y agradable.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 El hombre sabio es fuerte; y de pujante vigor el hombre docto.
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 Porque con ingenio harás la guerra: y la salud está en la multitud de consejeros.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 Alta está para el insensato la sabiduría: en la puerta no abrirá él su boca.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 Al que piensa mal hacer le llamarán hombre de malos pensamientos.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 El pensamiento del necio es pecado: y abominación á los hombres el escarnecedor.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 Si fueres flojo en el día de trabajo, tu fuerza será reducida.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 Si dejares de librar los que son tomados para la muerte, y los que son llevados al degolladero;
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 Si dijeres: Ciertamente no lo supimos; ¿no lo entenderá el que pesa los corazones? El que mira por tu alma, él lo conocerá, y dará al hombre según sus obras.
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 Come, hijo mío, de la miel, porque es buena, y del panal dulce á tu paladar:
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 Tal será el conocimiento de la sabiduría á tu alma: si la hallares tendrá recompensa, y al fin tu esperanza no será cortada.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Oh impío, no aceches la tienda del justo, no saquees su cámara;
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 Porque siete veces cae el justo, y se torna á levantar; mas los impíos caerán en el mal.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Cuando cayere tu enemigo, no te huelgues; y cuando tropezare, no se alegre tu corazón:
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 Porque Jehová no lo mire, y le desagrade, y aparte de sobre él su enojo.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 No te entrometas con los malignos, ni tengas envidia de los impíos;
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 Porque para el malo no habrá [buen] fin, y la candela de los impíos será apagada.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 Teme á Jehová, hijo mío, y al rey; no te entrometas con los veleidosos:
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 Porque su quebrantamiento se levantará de repente; y el quebrantamiento de ambos, ¿quién lo comprende?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 También estas cosas [pertenecen] á los sabios. Tener respeto á personas en el juicio no es bueno.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 El que dijere al malo, Justo eres, los pueblos lo maldecirán, y le detestarán las naciones:
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 Mas los que [lo] reprenden, serán agradables, y sobre ellos vendrá bendición de bien.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 Besados serán los labios del que responde palabras rectas.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Apresta tu obra de afuera, y disponla en tu heredad; y después edificarás tu casa.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 No seas sin causa testigo contra tu prójimo; y no lisonjees con tus labios.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 No digas: Como me hizo, así le haré; daré el pago al hombre según su obra.
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 Pasé junto á la heredad del hombre perezoso, y junto á la viña del hombre falto de entendimiento;
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 Y he aquí que por toda ella habían ya crecido espinas, ortigas habían ya cubierto su haz, y su cerca de piedra estaba ya destruída.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Y yo miré, y púse[lo] en mi corazón: vi[lo], y tomé consejo.
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 Un poco de sueño, cabeceando otro poco, poniendo mano sobre mano otro poco para dormir;
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 Así vendrá como caminante tu necesidad, y tu pobreza como hombre de escudo.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

< Proverbios 24 >