< Proverbios 23 >

1 CUANDO te sentares á comer con algún señor, considera bien lo que estuviere delante de ti;
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 Y pon cuchillo á tu garganta, si tienes gran apetito.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 No codicies sus manjares delicados, porque es pan engañoso.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 No trabajes por ser rico; pon coto á tu prudencia.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 ¿Has de poner tus ojos en las riquezas, siendo ningunas? porque hacerse han alas, como alas de águila, y volarán al cielo.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 No comas pan de [hombre de] mal ojo, ni codicies sus manjares:
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 Porque cual es su pensamiento en su alma, tal es él. Come y bebe, te dirá; mas su corazón no está contigo.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Vomitarás la parte que tú comiste, y perderás tus suaves palabras.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 No hables á oídos del necio; porque menospreciará la prudencia de tus razones.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 No traspases el término antiguo, ni entres en la heredad de los huérfanos:
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 Porque el defensor de ellos es el Fuerte, el cual juzgará la causa de ellos contra ti.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Aplica tu corazón á la enseñanza, y tus oídos á las palabras de sabiduría.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 No rehuses la corrección del muchacho: [porque] si lo hirieres con vara, no morirá.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Tú lo herirás con vara, y librarás su alma del infierno. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 Hijo mío, si tu corazón fuere sabio, también á mí se me alegrará el corazón;
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 Mis entrañas también se alegrarán, cuando tus labios hablaren cosas rectas.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 No tenga tu corazón envidia de los pecadores, antes [persevera] en el temor de Jehová todo tiempo:
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Porque ciertamente hay fin, y tu esperanza no será cortada.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Oye tú, hijo mío, y sé sabio, y endereza tu corazón al camino.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 No estés con los bebedores de vino, ni con los comedores de carne:
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Porque el bebedor y el comilón empobrecerán: y el sueño hará vestir vestidos rotos.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Oye á tu padre, á aquel que te engendró; y cuando tu madre envejeciere, no la menosprecies.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Compra la verdad, y no la vendas; la sabiduría, la enseñanza, y la inteligencia.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Mucho se alegrará el padre del justo: y el que engendró sabio se gozará con él.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Alégrense tu padre y tu madre, y gócese la que te engendró.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Dame, hijo mío, tu corazón, y miren tus ojos por mis caminos.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Porque sima profunda es la ramera, y pozo angosto la extraña.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 También ella, como robador, acecha, y multiplica entre los hombres los prevaricadores.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 ¿Para quién será el ay? ¿para quién el ay? ¿para quién las rencillas? ¿para quién las quejas? ¿para quién las heridas en balde? ¿para quién lo amoratado de los ojos?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Para los que se detienen mucho en el vino, para los que van buscando la mistura.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 No mires al vino cuando rojea, cuando resplandece su color en el vaso: éntrase suavemente;
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 [Mas] al fin como serpiente morderá, y como basilisco dará dolor:
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Tus ojos mirarán las extrañas, y tu corazón hablará perversidades.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Y serás como el que yace en medio de la mar, ó como el que está en la punta de un mastelero.
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 [Y dirás]: Hiriéronme, mas no me dolió; azotáronme, mas no lo sentí; cuando despertare, aun lo tornaré á buscar.
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Proverbios 23 >