< Proverbios 18 >

1 SEGÚN [su] antojo busca el que se desvía, y se entremete en todo negocio.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 No toma placer el necio en la inteligencia, sino en lo que su corazón se descubre.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Cuando viene el impío, viene también el menosprecio, y con el deshonrador la afrenta.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 Aguas profundas son las palabras de la boca del hombre; y arroyo revertiente, la fuente de la sabiduría.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Tener respeto á la persona del impío, para hacer caer al justo de [su] derecho, no es bueno.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Los labios del necio vienen con pleito; y su boca á cuestiones llama.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 La boca del necio es quebrantamiento para sí, y sus labios son lazos para su alma.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 Las palabras del chismoso parecen blandas, y descienden hasta lo íntimo del vientre.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 También el que es negligente en su obra es hermano del hombre disipador.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Torre fuerte es el nombre de Jehová: á él correrá el justo, y será levantado.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 Las riquezas del rico son la ciudad de su fortaleza, y como un muro alto en su imaginación.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Antes del quebrantamiento se eleva el corazón del hombre, y antes de la honra es el abatimiento.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 El que responde palabra antes de oir, le es fatuidad y oprobio.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 El ánimo del hombre soportará su enfermedad: mas ¿quién soportará al ánimo angustiado?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 El corazón del entendido adquiere sabiduría; y el oído de los sabios busca la ciencia.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 El presente del hombre le ensancha [el camino], y le lleva delante de los grandes.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 El primero en su propia causa [parece] justo; y su adversario viene, y le sondea.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 La suerte pone fin á los pleitos, y desparte los fuertes.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 El hermano ofendido [es más tenaz] que una ciudad fuerte: y las contiendas [de los hermanos] son como cerrojos de alcázar.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 Del fruto de la boca del hombre se hartará su vientre; hartaráse del producto de sus labios.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 La muerte y la vida están en poder de la lengua; y el que la ama comerá de sus frutos.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 El que halló esposa halló el bien, y alcanzó la benevolencia de Jehová.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 El pobre habla con ruegos; mas el rico responde durezas.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 El hombre [que tiene] amigos, ha de mostrarse amigo: y amigo hay más conjunto que el hermano.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

< Proverbios 18 >