< Job 30 >

1 MAS ahora los más mozos de días que yo, se ríen de mí; cuyos padres yo desdeñara ponerlos con los perros de mi ganado.
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 Porque ¿para qué yo habría menester la fuerza de sus manos, en los cuales había perecido con el tiempo?
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 Por causa de la pobreza y del hambre [andaban] solos; huían á la soledad, á lugar tenebroso, asolado y desierto.
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 Que cogían malvas entre los arbustos, y raíces de enebro para calentarse.
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 Eran echados de entre [las gentes], y todos les daban grita como al ladrón.
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 Habitaban en las barrancas de los arroyos, en las cavernas de la tierra, y en las rocas.
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 Bramaban entre las matas, y se reunían debajo de las espinas.
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 Hijos de viles, y hombres sin nombre, más bajos que la misma tierra.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 Y ahora yo soy su canción, y he sido hecho su refrán.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 Abomínanme, aléjanse de mí, y aun de mi rostro no detuvieron su saliva.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Porque [Dios] desató mi cuerda, y me afligió, por eso se desenfrenaron delante de mi rostro.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 A la mano derecha se levantaron los jóvenes; empujaron mis pies, y sentaron contra mí las vías de su ruina.
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 Mi senda desbarataron, aprovecháronse de mi quebrantamiento, contra los cuales no hubo ayudador.
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 Vinieron como por portillo ancho, revolviéronse á [mi] calamidad.
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Hanse revuelto turbaciones sobre mí; combatieron como viento mi alma, y mi salud pasó como nube.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 Y ahora mi alma está derramada en mí; días de aflicción me han aprehendido.
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 De noche taladra sobre mí mis huesos, y mis pulsos no reposan.
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 Con la grande copia [de materia] mi vestidura está demudada; cíñeme como el cuello de mi túnica.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Derribóme en el lodo, y soy semejante al polvo y á la ceniza.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 Clamo á ti, y no me oyes; preséntome, y no me atiendes.
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Haste tornado cruel para mí: con la fortaleza de tu mano me amenazas.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Levantásteme, é hicísteme cabalgar sobre el viento, y disolviste mi sustancia.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Porque yo conozco que me reduces á la muerte; y á la casa determinada á todo viviente.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 Mas él no extenderá la mano contra el sepulcro; ¿clamarán [los sepultados] cuando él los quebrantare?
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 ¿No lloré yo al afligido? Y mi alma ¿no se entristeció sobre el menesteroso?
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Cuando esperaba yo el bien, entonces vino el mal; y cuando esperaba luz, la oscuridad vino.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 Mis entrañas hierven, y no reposan; días de aflicción me han sobrecogido.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 Denegrido ando, y no por el sol: levantádome he en la congregación, y clamado.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 He venido á ser hermano de los dragones, y compañero de los buhos.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 Mi piel está denegrida sobre mí, y mis huesos se secaron con ardentía.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 Y hase tornado mi arpa en luto, y mi órgano en voz de lamentadores.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

< Job 30 >