< Job 29 >

1 Y VOLVIÓ Job á tomar su propósito, y dijo:
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 ¡Quién me tornase como en los meses pasados, como en los días que Dios me guardaba,
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 Cuando hacía resplandecer su candela sobre mi cabeza, á la luz de la cual yo caminaba en la oscuridad;
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 Como fué en los días de mi mocedad, cuando el secreto de Dios estaba en mi tienda;
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 Cuando aun el Omnipotente estaba conmigo, y mis hijos alrededor de mí;
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 Cuando lavaba yo mis caminos con manteca, y la piedra me derramaba ríos de aceite!
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 Cuando salía á la puerta á juicio, y en la plaza hacía preparar mi asiento,
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 Los mozos me veían, y se escondían; y los viejos se levantaban, y estaban en pie;
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 Los príncipes detenían sus palabras, ponían la mano sobre su boca;
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 La voz de los principales se ocultaba, y su lengua se pegaba á su paladar:
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 Cuando los oídos que me oían, me llamaban bienaventurado, y los ojos que me veían, me daban testimonio:
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 Porque libraba al pobre que gritaba, y al huérfano que carecía de ayudador.
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 La bendición del que se iba á perder venía sobre mí; y al corazón de la viuda daba alegría.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 Vestíame de justicia, y ella me vestía como un manto; y mi toca era juicio.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 Yo era ojos al ciego, y pies al cojo.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 A los menesterosos era padre; y de la causa que no entendía, me informaba con diligencia:
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 Y quebraba los colmillos del inicuo, y de sus dientes hacía soltar la presa.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 Y decía yo: En mi nido moriré, y como arena multiplicaré días.
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 Mi raíz estaba abierta junto á las aguas, y en mis ramas permanecía el rocío.
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 Mi honra se renovaba en mí, y mi arco se corroboraba en mi mano.
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 Oíanme, y esperaban; y callaban á mi consejo.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 Tras mi palabra no replicaban, y mi razón destilaba sobre ellos.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 Y esperábanme como á la lluvia, y abrían su boca [como] á la lluvia tardía.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 Si me reía con ellos, no lo creían: y no abatían la luz de mi rostro.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 Calificaba yo el camino de ellos, y sentábame en cabecera; y moraba como rey en el ejército, como el que consuela llorosos.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

< Job 29 >