< Job 36 >

1 Y pasando a delante Eliú, dijo:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Espérame un poco, y enseñarte he: porque todavía hablo por Dios.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Tomaré mi sabiduría de lejos, y daré la justicia a mi Hacedor.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Porque de cierto no son mentira mis palabras, antes se trata contigo con perfecta sabiduría.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 He aquí, que Dios es grande, y no aborrece, fuerte en virtud de corazón.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 No dará vida al impío; y a los afligidos dará su derecho.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 No quitará sus ojos del justo: mas con los reyes los pondrá también en trono para siempre, y serán ensalzados.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 Y si estuvieren presos en grillos, y cautivos en las cuerdas de aflicción,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 El les anunciará la obra de ellos, y que sus rebeliones prevalecieron.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Y despierta el oído de ellos para castigo, y dice que se conviertan de la iniquidad.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Si oyeren, y sirvieren, acabarán sus días en bien, y sus años en deleites.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Mas si no oyeren, serán pasados a cuchillo: y perecerán sin sabiduría.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Mas los hipócritas de corazón le irritarán más; y no clamarán, cuando él los atare.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 El alma de ellos morirá en su mocedad, y su vida entre los sodomíticos.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Al pobre librará de su pobreza, y en la aflicción despertará su oreja.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Y aun te apartará de la boca de la angustia en anchura, debajo de la cual no haya estrechura, y te asentará mesa llena de grosura.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Mas tú has henchido el juicio del impío contra la justicia, y el juicio [que lo] sustenta todo.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Por lo cual es de temer, que no te quite con herida, la cual no evites con gran rescate.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 ¿Estimará él tus riquezas, ni el oro, ni todas las fuerzas de poder?
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 No desees la noche, en la cual él corta los pueblos de su lugar.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Guárdate, no mires a la iniquidad, teniéndola por mejor que la pobreza.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 He aquí, que Dios será ensalzado con su poder, ¿quién semejante a él, enseñador?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 ¿Quién visitó sobre él su camino? ¿Y quién dijo: Iniquidad has hecho?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Acuérdate de engrandecer su obra, la cual contemplan los hombres.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 La cual vieron todos los hombres, y el hombre la ve de lejos.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 He aquí que Dios es grande, y nosotros no le conoceremos: ni se puede rastrear el número de sus años.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 Porque él detiene las goteras de las aguas, cuando la lluvia se derrama de su vapor.
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Cuando gotean de las nubes, gotean sobre los hombres en abundancia.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 ¿Si entenderá también los extendimientos de las nubes, y los bramidos de su tabernáculo?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 He aquí, que él extendió sobre ella su luz; y cubrió las raíces de la mar.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Con ellas castiga a los pueblos, y da comida a la multitud.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Con las nubes encubre la luz, y les manda que vayan contra ella.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 La una da nuevas de la otra: la una adquiere ira contra la que viene.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Job 36 >