< Job 35 >

1 Y procediendo Eliú en su razonamiento, dijo:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 ¿Piensas haber sido conforme a derecho lo que dijiste: Más justo soy que Dios?
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 Porque dijiste: ¿Qué te aprovechará, que provecho tendré de mi pecado?
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 Yo te responderé algunas razones; y a tus compañeros contigo.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Mira a los cielos, y ve, y considera que los cielos son más altos que tú.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Si pecares, ¿qué habrás hecho contra él? y si tus rebeliones se multiplicaren, ¿qué le harás tú?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Si fueres justo, ¿qué le darás a él? ¿o qué recibirá de tu mano?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Al hombre como tú dañará tu impiedad; y al hijo del hombre aprovechará tu justicia.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 A causa de la multitud de las violencias clamarán, y darán voces por la fuerza de los violentos:
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Y ninguno dirá: ¿Dónde está Dios mi hacedor, que da canciones en la noche;
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 Que nos enseña más que las bestias de la tierra, y nos hace sabios más que las aves del cielo?
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Allí clamarán, y él no oirá por la soberbia de los malos.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Ciertamente Dios no oirá la vanidad, ni el Omnipotente la mirará.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Aunque más digas: No le mirará: haz juicio delante de él, y espera en él.
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 Mas ahora, porque su ira no visita, ni conoce en gran manera,
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Job abrió su boca vanamente, y multiplica palabras sin sabiduría.
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

< Job 35 >