< Luka 19 >

1 In Jezus je vstopil [v Jeriho] in šel skozi Jeriho.
Yesu analowa mu Yeriko napitirira.
2 In glej, tam je bil mož, imenovan Zahej, ki je bil šef med davkarji in je bil bogat.
Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera.
3 In prizadeval si je, da bi videl, kdo je bil Jezus, pa ni mogel zaradi množice, ker je bil majhne postave.
Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu.
4 In stekel je naprej ter splezal na egiptovsko smokvo, da bi ga videl, kajti moral bi iti mimo po tej poti.
Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.
5 Ko je Jezus prišel na ta kraj, je pogledal gor, ga zagledal in mu rekel: »Zahej, podvizaj se in pridi dol, kajti danes moram ostati v tvoji hiši.«
Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, “Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero.”
6 In ta je pohitel in prišel dol ter ga radostno sprejel.
Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.
7 In ko so to videli, so vsi godrnjali, rekoč: »Ta je odšel, da bi bil gost pri človeku, ki je grešnik.«
Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, “Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa.”
8 Zahej pa je vstal in rekel Gospodu: »Glej, Gospod, polovico svojih dobrin dam revnim in če sem po krivem obtožen, da sem karkoli vzel od kateregakoli človeka, mu štirikratno povrnem.«
Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, “Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi.”
9 Jezus pa mu je rekel: »Ta dan je prišla k tej hiši rešitev duše, glede na to, da je tudi on Abrahamov sin.
Yesu anati kwa iye, “Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu.
10 Kajti Sin človekov je prišel, da poišče in da reši to, kar je bilo izgubljeno.«
Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.”
11 In medtem ko so slišali te stvari, je dodal in povedal prispodobo, kajti bil je blizu Jeruzalema in ker so mislili, da naj bi se Božje kraljestvo prikazalo takoj.
Pamene iwo ankamvera izi, Iye anapitiriza kuwawuza fanizo, chifukwa Iye anali kufupi ndi Yerusalemu ndipo anthu ankaganiza kuti ufumu wa Mulungu ukanaoneka nthawi yomweyo.
12 Rekel je torej: »Neki visoki plemič je odšel v daljno deželo, da prejme zase kraljestvo in da se vrne.
Iye anati, “Munthu wa banja laufumu anapita ku dziko lakutali kukadzozedwa ufumu ndipo kenaka abwerenso kwawo.
13 In poklical je svojih deset služabnikov ter jim razdelil deset funtov in jim rekel: ›Zaposlite se s trgovanjem, dokler ne pridem.‹
Tsono iye anayitana antchito ake khumi ndi kuwapatsa ndalama khumi. Iye anati, ‘Gwiritsani ntchito ndalama izi mpaka nditabwerera.’
14 Toda njegovi državljani so ga sovražili in za njim poslali sporočilo, rekoč: ›Nočemo, da bi ta človek zavladal nad nami.‹
“Koma anthu ake anamuda ndipo anatuma nthumwi pambuyo pake kukanena kuti, ‘Sitikufuna munthuyu kuti akhale mfumu yathu.’
15 Pripetilo pa se je, ko se je vrnil, da je prejel kraljestvo. Potem je ukazal, naj te služabnike, ki jim je dal denar, pokličejo k njemu, da lahko izve, koliko je vsak človek pridobil s trgovanjem.
“Iye analandira ufumuwo ngakhale zinali zotero, ndipo anabwerera kwawo. Kenaka iye anatumiza uthenga kwa antchito ake amene anawapatsa ndalama aja, ndi cholinga chakuti adziwe chimene anapindula nazo.
16 Potem je prišel prvi, rekoč: ›Gospodar, tvoj funt je pridobil deset funtov.‹
“Woyamba anabwera ndipo anati, ‘Bwana ndalama zanu zapindula khumi zina.’
17 Rekel mu je: ›V redu, ti dobri služabnik, ker si bil zvest v zelo majhnem, imej oblast nad desetimi mesti.‹
“Bwana wakeyo anayankha kuti, Wachita bwino wantchito wabwino. ‘Chifukwa wakhulupirika pa zinthu zazingʼono, lamulira mizinda khumi.’
18 In prišel je drugi, rekoč: ›Gospod, tvoj funt je pridobil pet funtov.‹
“Wachiwiri anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama zanu zapindula zisanu zina.’
19 In tudi njemu je rekel podobno: ›Tudi ti bodi nad petimi mesti.‹
“Bwana anayankha kuti, ‘Iwe lamulira mizinda isanu.’
20 In prišel je še en, rekoč: ›Gospod, glej, tukaj je tvoj funt, ki sem ga hranil v prtiču,
“Kenaka wantchito wina anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama yanu nayi; ine ndinayibisa ndi kuyisunga mʼkansalu.
21 kajti bal sem se te, ker si strog človek; jemlješ to, česar nisi položil in žanješ to, česar nisi posejal.‹
Ine ndimakuopani, chifukwa ndinu munthu wowuma mtima. Inu mumatenga chimene simunachiyike ndi kukolola chimene simunadzale.’
22 On pa mu reče: ›Po tvojih lastnih ustih te bom sodil, ti zlobni služabnik. Vedel si, da sem bil strog človek, ki jemljem to, česar nisem položil in žanjem to, česar nisem posejal.
“Bwana wake anayankha kuti, ‘Ine ndikukuweruza iwe ndi mawu ako omwewo. Ndiwe wantchito woyipa. Kani umadziwa kuti ndine munthu wowuma mtima ndi wotenga chimene sindinasungitse, ndi kukolola chimene sindinadzale?
23 Zakaj torej mojega denarja nisi dal v banko, da bi lahko ob svojem prihodu svojo lastnino zahteval z obrestmi?‹
Nanga nʼchifukwa chiyani sunasungitse ndalama yanga, kuti ine pobwera, ndidzayitenge ndi chiwongoladzanja?’
24 In rekel je tem, ki so stali poleg: ›Vzemite od njega funt in ga dajte tistemu, ki ima deset funtov.‹
“Ndipo iye anawuza amene anayimirira pafupi kuti, ‘Tengani ndalama yake ndi kumupatsa amene ali ndi ndalama khumiyo!’”
25 (Oni pa so mu rekli: ›Gospod, ta ima deset funtov.‹)
Iwo anati, “Bwana iyeyu ali nazo kale khumi!”
26 Kajti povem vam: ›Da se bo vsakemu, ki ima, dalo; od tistega, ki nima, pa se bo odvzelo celó to, kar ima.‹
Iye anayankha kuti, “Ndikukuwuzani kuti, aliyense amene ali nazo, adzapatsidwa zambiri, koma amene alibe, adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho.
27 Toda tiste moje sovražnike, ki niso hoteli, da bi jim jaz vladal, privedite sèm in jih pokončajte pred menoj.‹«
Tsono adani anga aja amene sankafuna kuti ndikhale mfumu yawo, abweretseni pano ndi kuwapha ine ndikuona.”
28 In ko je tako govoril, je šel pred njimi ter se vzpenjal v Jeruzalem.
Yesu atatha kunena izi, anayendabe kupita ku Yerusalemu.
29 Pripetilo pa se je, ko je prišel blizu Bétfage in Betanije, pri gori, ki se imenuje Oljska gora, [da] je poslal dva izmed svojih učencev,
Iye atayandikira ku Betifage ndi Betaniya pa phiri lotchedwa Olivi, Iye anatuma awiri a ophunzira nati kwa iwo,
30 rekoč: »Pojdita v vas nasproti vama, v kateri bosta ob svojem vstopu našla privezano žrebe, na katerem človek še nikoli ni sedel. Odvežita ga in ga privedita sèm.
“Pitani mʼmudzi uli patsogolo panu, mukakalowa mʼmudzimo, mukapeza mwana wabulu womangiriridwa amene wina aliyense sanakwerepo. Mukamumasule ndi kubwera naye kuno.
31 Če pa vaju katerikoli človek vpraša: ›Zakaj ga odvezujeta?‹ mu recita takole: ›Ker ga potrebuje Gospod.‹«
Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumumasula mwana buluyo?’ Mukamuwuze kuti, ‘Ambuye akumufuna.’”
32 In onadva, ki sta bila poslana, sta šla svojo pot in našla tako, kakor jima je povedal.
Otumidwawo anapita nakamupeza mwana wabulu monga momwe Yesu anawawuzira.
33 In ko sta odvezovala žrebe, so jima lastniki le-tega rekli: »Zakaj odvezujeta žrebe?«
Pamene ankamasula mwana wabuluyo, eni ake anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukumasula mwana wabuluyo?”
34 Onadva pa sta rekla: »Gospod ga potrebuje.«
Iwo anayankha kuti, “Ambuye akumufuna.”
35 In privedla sta ga k Jezusu in svoje obleke vrgla na žrebe ter nanj posadila Jezusa.
Iwo anabweretsa buluyo kwa Yesu, naponya zovala zawo pa bulupo ndi kumukwezapo Yesu.
36 In ko je šel, so na pot razgrinjali svoja oblačila.
Pamene ankapita, anthu anayala zovala zawo mu msewu.
37 Ko je prišel blizu, torej celó k pobočju Oljske gore, se je celotna množica učencev začela veseliti in z močnim glasom hvaliti Boga za vsa mogočna dela, ki so jih videli,
Iye atafika pafupi ndi pamene msewu umatsikira ku phiri la Olivi, gulu lonse la ophunzira linayamba kuyamika Mulungu mwachimwemwe ndi mawu ofuwula chifukwa cha zodabwitsa zonse anaziona.
38 rekoč: »Blagoslovljen naj bo Kralj, ki prihaja v imenu Gospodovem. V nebesih mir in slava na višavah.«
“Yodala mfumu imene ikubwera mʼdzina la Ambuye!” “Mtendere kumwamba ndi ulemerero mmwambamwamba!”
39 Nekaj farizejev izmed množice pa mu je reklo: »Učitelj, oštej svoje učence.«
Ena mwa Afarisi mʼgulumo anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, adzudzuleni ophunzira anu!”
40 In odgovoril jim je in jim rekel: »Povem vam, da če bi ti molčali, bodo takoj kamni zavpili.«
Iye anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani kuti, ngati atakhala chete, miyala idzafuwula.”
41 Ko pa je prišel bliže, je zagledal mesto ter se razjokal nad njim,
Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira
42 rekoč: »Če bi ti spoznalo, celó ti, vsaj na ta tvoj dan, stvari, ki pripadajo tvojemu miru! Toda sedaj so skrite pred tvojimi očmi.
nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako.
43 Kajti nadte bodo prišli dnevi, ko bodo tvoji sovražniki okoli tebe nasuli okope in te obkolili in te stiskali na vsaki strani
Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse.
44 in zravnali te bodo z zemljo in tvoje otroke v tebi; in v tebi ne bodo pustili enega kamna na drugem, ker nisi spoznalo časa svojega obiskanja.«
Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”
45 In odšel je v tempelj ter začel izganjati te, ki so v njem prodajali in te, ki so kupovali,
Kenaka Iye analowa mʼdera la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kutulutsa kunja amene amachita malonda.
46 rekoč jim: »Pisano je: ›Moja hiša je hiša molitve, ‹ toda vi ste jo naredili za brlog razbojnikov.«
Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzakhala nyumba ya mapemphero, koma inu mwayisadutsa phanga la achifwamba.”
47 In vsak dan je učil v templju. Toda visoki duhovniki in pisarji in vodje ljudstva so si prizadevali, da ga pokončajo,
Tsiku lililonse amaphunzitsa mʼNyumba ya Mulungu. Koma akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi atsogoleri pakati pa anthu amayesetsa kuti amuphe.
48 pa niso mogli najti, kaj bi lahko storili, kajti vsi ljudje so ga zelo pozorno poslušali.
Komabe iwo sanathe kupeza njira ina iliyonse kuti achite izi, chifukwa anthu onse anakhulupirira mawu ake.

< Luka 19 >