< Luka 24 >

1 Torej na prvi dan tedna so zelo zgodaj zjutraj prišle k mavzoleju in nosile dišave, ki so jih pripravile in nekatere druge z njimi.
Pa tsiku loyamba la Sabata, mmamawa kwambiri, amayi anatenga zonunkhira napita ku manda.
2 Našle pa so kamen odvaljen od mavzoleja.
Anaona mwala wa pa manda utagubuduzika
3 In vstopile so vanj, pa niso našle telesa Gospoda Jezusa.
ndipo atalowamo sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu.
4 In pripetilo se je, medtem ko so bile glede tega zelo zmedene, glej, dva moža sta stala poleg njih v sijočih oblekah
Pamene iwo ankadabwa za zimenezi, mwadzidzidzi, amuna awiri ovala zovala zonyezimira kwambiri anayimirira pambali pawo.
5 in medtem ko so bile prestrašene in so svoje obraze sklonile k zemlji, sta jim rekla: »Zakaj iščete živega med mrtvimi?
Ndi mantha, amayiwo anaweramitsa nkhope zawo pansi, koma amunawo anawawuza kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufuna wamoyo pakati pa akufa?
6 Njega ni tukaj, temveč je bil obujen. Spomnite se, kako vam je govoril, ko je bil še v Galileji,
Iye sali muno ayi. Wauka! Kumbukirani zimene anakuwuzani pamene anali nanu ku Galileya:
7 rekoč: ›Sin človekov mora biti izročen v roke grešnih ljudi in biti križan ter tretji dan ponovno vstati.‹«
‘Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa, napachikidwa ndipo tsiku lachitatu adzaukitsidwanso.’”
8 In spomnile so se njegovih besed
Ndipo anakumbukira mawu ake.
9 ter se vrnile od mavzoleja in vse te stvari povedale enajsterim ter vsem ostalim.
Atabwerera kuchokera ku mandako, anafotokoza zinthu zonse kwa khumi ndi mmodziwo ndi kwa ena onse.
10 Bile so Marija Magdalena in Joana in Marija, Jakobova mati ter druge ženske, ki so bile z njimi, ki so te stvari povedale apostolom.
Amayi anali Mariya Magadalena, Yohana, Mariya amayi a Yakobo, ndi ena anali nawo amene anawuza atumwi.
11 Njihove besede pa so se jim zdele kakor prazno opravljanje in jim niso verjeli.
Koma iwo sanawakhulupirire amayiwa, chifukwa mawu awo amaoneka kwa iwo ngati opanda nzeru.
12 Potem je vstal Peter in stekel k mavzoleju. In sklonjen dol je zagledal lanene trakove, položene posebej, ter odšel in se v sebi spraševal o tem, kar se je pripetilo.
Komabe Petro anayimirira ndi kuthamangira ku manda. Atasuzumira, anaona nsalu zimene anamukulungira zija zili pa zokha, ndipo iye anachoka, akudabwa ndi zimene zinachitikazo.
13 In glej, dva izmed njih sta tega istega dne odšla proti vasi, z imenom Emavs, ki je bila okoli šestdeset dolžin brazd od Jeruzalema.
Ndipo tsiku lomwelo, awiri a iwo ankapita ku mudzi wotchedwa Emau, pafupifupi makilomita khumi ndi imodzi kuchokera ku Yerusalemu.
14 In skupaj sta se pogovarjala o vseh teh stvareh, ki so se zgodile.
Iwo ankayankhulana za zonse zimene zinachitikazo.
15 In pripetilo se je, medtem ko sta se skupaj posvetovala in razpravljala, da se je približal sam Jezus in šel z njima.
Pamenepo Yesu mwini wake anabwera ndi kuyenda nawo pamodzi;
16 Vendar so bile njune oči zadržane, da ga ne bi spoznala.
koma iwo sanamuzindikire.
17 On pa jima je rekel: »Kakšne vrste pogovori so to, ki jih imata drug z drugim, medtem ko hodita in sta žalostna?«
Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukukambirana zotani mʼnjira muno?” Iwo anayima ndi nkhope zakugwa.
18 Eden izmed njiju, ki mu je bilo ime Kleopa, pa mu odgovori in reče: »Ali si ti edini tujec v Jeruzalemu in nisi izvedel stvari, ki so se v teh dneh tam zgodile?«
Mmodzi wa iwo wotchedwa Kaliyopa anamufunsa kuti, “Kodi ndiwe wekha wokhala mu Yerusalemu amene sukudziwa zinthu zimene zachitika mʼmasiku awa?”
19 In rekel jima je: »Katere stvari?« In rekla sta mu: »Glede Jezusa Nazarečana, ki je bil prerok, mogočen v dejanju in besedi, pred Bogom in vsemi ljudmi
Iye anafunsa kuti, “Zinthu zotani?” Iwo anayankha nati, “Za Yesu wa ku Nazareti, Iye anali mneneri, wamphamvu mʼmawu ndi mu zochita pamaso pa Mulungu ndi anthu onse.
20 in kako so ga visoki duhovniki in naši vladarji izročili, da bi bil obsojen na smrt in ga križali.
Akulu a ansembe ndi oweruza anamupereka Iye kuti aphedwe, ndipo anamupachika Iye;
21 Toda mi smo zaupali, da je bil on tisti, ki naj bi odkupil Izraela; in poleg vsega tega je danes tretji dan, odkar so se te stvari zgodile.
koma ife tinkayembekezera kuti Iye ndiye amene akanawombola Israeli. Ndipo kuwonjeza apo, lero ndi tsiku lachitatu chichitikireni izi.
22 Da, in nekatere ženske, prav tako iz naše skupine, ki so bile zgodaj pri mavzoleju, so nas osupnile.
Kuwonjezanso apo, ena mwa amayi athu atidabwitsa ife. Iwo anapita ku manda mmamawa
23 In ko niso našle njegovega telesa, so prišle, rekoč, da so prav tako videle videnje angelov, ki sta rekla, da je bil živ.
koma sanakapeze mtembo wake. Iwo anabwera ndi kudzatiwuza ife kuti anaona masomphenya a angelo amene anati Yesu ali moyo.
24 In nekateri izmed teh, ki so bili z nami, so odšli k mavzoleju in našli točno takó, kakor so rekle ženske, toda njega niso videli.«
Kenaka ena mwa anzathu anapita ku manda ndipo anakapeza monga momwe amayiwo ananenera, koma Iye sanamuone.”
25 Potem jima je rekel: »Oh bedaka in počasnega srca za verovanje vsega, kar so govorili preroki.
Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu anthu opusa, osafuna kukhulupirira msanga zonse zimene aneneri ananena!
26 Ali ni moral Kristus pretrpeti te stvari in vstopiti v svojo slavo?«
Kodi Khristu sanayenera kumva zowawa izi ndipo kenaka ndi kulowa mu ulemerero wake?”
27 In začel je pri Mojzesu in vseh prerokih ter jima v vseh pismih pojasnil besede glede njega samega.
Ndipo kuyambira ndi Mose ndi aneneri onse Iye anawafotokozera zimene zinalembedwa mʼmalemba wonse zokhudzana ndi Iye mwini.
28 In približali so se blizu k vasi, kamor sta šla, on pa je storil, kakor da bo odšel dalje.
Atayandikira mudzi omwe amapitako, Yesu anachita ngati akupitirira.
29 Vendar sta ga primorala, rekoč: »Ostani z nama, kajti blizu večera je in dan je davno minil.« In odšel je noter, da ostane z njima.
Koma iwo anamupempha Iye kwambiri kuti, “Mukhale ndi ife, popeza kwatsala pangʼono kuda, ndipo dzuwa lili pafupi kulowa.” Ndipo Iye anapita kukakhala nawo.
30 In pripetilo se je, medtem ko je z njima sedel pri hrani, [da] je vzel kruh in ga blagoslovil in prelomil ter jima dal.
Iye ali pa tebulo pamodzi nawo, anatenga buledi ndipo anayamika, nanyema nayamba kuwagawira.
31 In njune oči so bile odprte in sta ga spoznala, on pa je izginil iz njunega pogleda.
Kenaka maso awo anatsekuka ndipo anamuzindikira Iye, ndipo anachoka pakati pawo.
32 In rekla sta drug drugemu: »Ali ni najino srce gorelo znotraj naju, medtem ko je z nama govoril po poti in medtem ko nama je odpiral pisma?«
Iwo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi mitima yathu sinali kutentha mʼkati mwathu pamene Iye ankayankhulana nafe pa njira ndi mmene anatitsekulira malemba?”
33 In vstala sta še isto uro in se vrnila v Jeruzalem in našla skupaj zbrane enajstere in tiste, ki so bili z njimi,
Nthawi yomweyo iwo anayimirira ndi kubwerera ku Yerusalemu. Iwo anapeza khumi ndi mmodziwo ndi ena anali nawo nasonkhana pamodzi
34 govoreče: »Gospod je bil resnično obujen in se prikazal Simonu.«
ndipo anati, “Ndi zoonadi! Ambuye auka ndipo anaonekera kwa Simoni.”
35 In povedala sta, kakšne stvari so se zgodile na poti in kako sta ga prepoznala po lomljenju kruha.
Kenaka awiriwo anawawuza zimene zinachitika pa njira, ndi mmene iwo anamudziwira Yesu, Iye atanyema buledi.
36 In ko sta tako govorila, je sam Jezus stal v njihovi sredi in jim reče: »Mir vam bodi.«
Akufotokoza zimenezi, Yesu mwini wake anayimirira pakati pawo ndipo anati, “Mukhale ndi mtendere.”
37 Toda bili so prestrašeni in zgroženi in domnevali so, da so videli duha.
Koma chifukwa choti anathedwa nzeru ndi kuchita mantha, ankaganiza kuti akuona mzukwa.
38 Rekel jim je: »Zakaj ste zaskrbljeni? In zakaj v vaših srcih vstajajo misli?
Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuvutika? Nʼchifukwa chiyani mukukayika mu mtima mwanu?
39 Poglejte moje roke in moja stopala, da sem to jaz sam. Potipajte me in poglejte, kajti duh nima mesa in kosti, kakor vidite, da jih imam jaz.«
Taonani manja anga ndi mapazi anga. Ine ndine amene! Khudzeni kuti muone. Mzukwa ulibe mnofu ndi mafupa monga mukuonera ndili nazo.”
40 In ko je tako govoril, jim je pokazal svoje roke in svoja stopala.
Iye atanena izi anawaonetsa manja ake ndi mapazi ake.
41 In medtem ko zaradi radosti niso verjeli ter se čudili, jim je rekel: »Imate tukaj kaj hrane?«
Ndipo pamene iwo samakhulupirirabe, chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, Iye anawafunsa kuti, “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?”
42 In dali so mu kos pečene ribe in od satovja.
Iwo anamupatsa Iye kachidutswa ka nsomba yophika.
43 In vzel je to ter pred njimi pojedel.
Iye anakatenga ndi kukadya iwo akuona.
44 In rekel jim je: »To so besede, ki sem vam jih govoril, medtem ko sem bil še z vami, da se morajo izpolniti vse stvari, ki so bile glede mene zapisane v Mojzesovi postavi in v prerokih in v psalmih.«
Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene ndinakuwuzani pamene ndinali nanu: chilichonse chiyenera kukwaniritsidwa chimene chinalembedwa cha Ine mʼbuku la Malamulo a Mose, Aneneri ndi Masalimo.”
45 Tedaj jim je odprl njihov razum, da so lahko razumeli pisma
Kenaka anawatsekula maganizo kuti azindikire Malemba.
46 in jim rekel: »Tako je pisano in tako se je Kristusu spodobilo trpeti in tretji dan vstati od mrtvih,
Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene zinalembedwa: Khristu adzazunzika ndipo adzauka kwa akufa tsiku lachitatu.
47 in da bi se kesanje ter odpuščanje grehov oznanjalo v njegovem imenu med vsemi narodi, začenši v Jeruzalemu.
Ndipo kutembenuka mtima ndi kukhululukidwa kwa machimo zidzalalikidwa mu dzina lake kwa anthu amitundu yonse kuyambira mu Yerusalemu.
48 In vi ste priče teh stvari.
Inu ndinu mboni za zimenezi.
49 In glejte, nad vas pošiljam obljubo svojega Očeta, toda ostanite v jeruzalemskem mestu, dokler ne boste opremljeni z močjo od zgoraj.«
Ine ndidzakutumizirani chimene Atate anga analonjeza. Koma khalani mu mzinda muno mpaka mutavekedwa mphamvu yochokera kumwamba.”
50 In odvedel jih je ven, prav do Betanije in povzdignil svoje roke in jih blagoslovil.
Iye atawatengera kunja kwa mzindawo mpaka ku Betaniya, anakweza manja ake ndi kuwadalitsa.
51 In medtem ko jih je blagoslavljal, se je pripetilo, [da] je bil ločen od njih in odnesen gor v nebo.
Iye akuwadalitsa, anawasiya ndipo anatengedwa kupita kumwamba.
52 In oni so ga oboževali in se z veliko radostjo vrnili v Jeruzalem
Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu.
53 in bili so nenehno v templju in hvalili in blagoslavljali Boga. Amen.
Ndipo iwo anakhalabe ku Nyumba ya Mulungu, akulemekeza Mulungu.

< Luka 24 >