< Книга пророка Иоиля 3 >

1 Яко се, Аз во дни тыя и во время оно, егда возвращу пленники Иудины и Иерусалимли,
“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
2 и соберу вся языки, и сведу я на юдоль Иосафатову, и разсуждуся с ними ту о людех Моих и о наследии Моем Израили, иже разсеяшася во языцех, и землю Мою разделиша.
ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
3 И на люди Моя вергоша жребия, и даша отрочища блудницам, и отроковицы продаяху на вине и пияху.
Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
4 И что вы Мне, Тире и Сидоне и вся Галилеа иноплеменников? Еда воздаяние вы воздаете Мне? Или памятозлобствуете вы на Мя? Остро и быстро воздам воздаяние ваше на главы ваша,
“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
5 понеже сребро Мое и злато Мое взясте, и избранная Моя и добрая внесосте в требища ваша,
Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
6 и сыны Иудины и сыны Иерусалимли продасте сыном Еллинским, яко да ижденете я от предел их.
Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
7 И се, Аз возставлю я от места, в неже продасте я тамо, и воздам воздаяние ваше на главы ваша:
“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
8 и отдам сыны ваша и дщери ваша в руце сынов Иудиных, и продадят я в плен во страну далече сущу, яко Господь глагола.
Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
9 Проповедите сия во языцех, освятите рать, возставите сечцы, приведите и восходите, вси мужие воинстии,
Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
10 разсецыте рала ваша на мечи и серпы ваша на копия: немощный да глаголет, яко могу аз:
Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
11 совокупляйтеся и входите, вси языцы окрест, и соберитеся ту: кроткий да будет храбр.
Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
12 Да востанут и взыдут вси языцы на юдоль Иосафатову, яко тамо сяду разсудити вся языки яже окрест.
“Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
13 Испустите серпы, яко предстоит обымание винограда: внидите, топчите, яко исполнь точило, изливаются подточилия, яко умножишася злобы их.
Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
14 Гласи прогласишася на поли судебнем, яко близ день Господень на юдоли судебней.
Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
15 Солнце и луна померкнут, и звезды скрыют свет свой.
Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
16 Господь же от Сиона воззовет и от Иерусалима даст глас Свой, и потрясется небо и земля: Господь же пощадит люди Своя и укрепит (Господь) сыны Израилевы.
Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
17 И увесте, яко Аз Господь Бог ваш, вселяяся в Сионе в горе Моей святей: и будет Иерусалим свят, и иноплеменницы не пройдут сквозе его ктому.
“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
18 И будет в той день, искаплют горы сладость, и холми источат млеко, и вси источницы Иудины источат воды, и источник от дому Господня изыдет и напоит водотечь Сития.
“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
19 Египет в погибель будет, и Идумеа в поле погибели будет за озлобление сынов Иудиных, понеже пролияша кровь праведную на земли своей:
Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
20 Иудеа же во веки населится, и Иерусалим в роды родов.
Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
21 И взыщу крови их и не обезвиню: и Господь вселится в Сионе.
Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”

< Книга пророка Иоиля 3 >