< Вторая книга Царств 22 >

1 И глагола Давид ко Господу словеса песни сея в день, в оньже избави и Господь из руки всех враг его и из руки Сауловы,
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 и рече песнь: Господи, каменю мой и утверждение мое, и избавляяй мя мне:
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 Бог мой, хранитель мой будет мне, уповая буду на Него: защитник мой и рог спасения моего, Заступник мой и прибежище мое спасения моего, от неправеднаго спасеши мя.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 Хвальнаго призову Господа, и от враг моих спасуся:
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 яко одержаша мя болезни смертныя и потоцы беззакония смятоша мя,
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 болезни смертныя обыдоша мя, предвариша мя жестокости смертныя. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
7 Внегда скорбети ми призову Господа, и к Богу моему воззову, и услышит от храма святаго Своего глас мой, и вопль мой внидет во ушы Его.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 И смятеся и трепетна бысть земля, и основания небесе смятошася и подвигошася, яко прогневася на ня Господь:
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 взыде дым гневом Его, и огнь из уст Его пояст: углие возгорешася от Него,
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 и преклони небеса и сниде, и мрак под ногама Его,
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 и вседе на Херувимы и лете, и явися на крилу ветреню,
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 и положи тму закров Свой: окрест Его селение Его, темноту вод огусти во облацех воздушных:
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 от сияния пред Ним разгорешася углие огненнии.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 И возгреме с небесе Господь, и Вышний даде глас Свой,
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 и посла стрелы, и расточи их: и блесну молнию, и устраши я:
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 и явишася источницы морстии, и открышася основания вселенныя от запрещения Господня, от дохновения духа гнева Его:
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 посла с высоты и прият мя, извлече мя от вод многих:
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 избави мя от враг моих сильных и от ненавидящих мя, яко укрепишася паче мене:
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 предвариша мя в день печали моея. И бысть Господь утверждение мое,
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 и изведе мя на широту, и избави мя, яко благоволи во мне.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 И воздаде ми Господь по правде моей, и по чистоте руку моею воздаде ми,
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 яко сохраних пути Господни и не нечествовах от Бога моего,
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 яко вся судбы Его предо мною, и оправдания Его не отступиша от мене,
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 и буду непорочен Ему, и сохранюся от беззакония моего.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 И воздаст ми Господь по правде моей и по чистоте руку моею пред очима Его.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 С преподобным преподобен будеши, и с мужем неповинным неповинен будеши:
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 и со избранным избран будеши, и со строптивым развратишися:
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 люди же смиренныя спасеши, и очи гордых смириши.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 Яко Ты просвещаеши светилник мой, Господи, и Господь просветит ми тму мою:
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 яко Тобою потеку препоясан, и о Бозе моем прелезу стену.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 Крепок, непорочен путь Его: глаголгол Господень державен, разжжен: защитник есть всем уповающым на Него.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 Яко кто крепок разве Господа? И кто творец разве Бога нашего?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 Крепок укрепляяй мя силою, и положи непорочен путь мой:
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 положивый нозе мои яко елени, и на высоких поставляяй мя:
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 научаяй руце мои на брань, и положивый лук медян мышца моя.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 И дал ми еси защищение спасения моего, и кротость Твоя умножи мя.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 Разширил еси стопы моя подо мною, и не позыбнустеся голени мои.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 Пожену враги моя и потреблю я, и не возвращуся дондеже скончаю их:
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 и сокрушу их, и не востанут, и падут под ногама моима.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 И укрепиши мя силою на брань, подклониши востающыя на мя под мя.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 И враги моя дал ми еси хребет, ненавидящыя мя, и умертвил еси их:
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 возопиют, и несть помощника, ко Господу, и не услыша их:
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 и истних я яко прах земный, яко брение путий истончих я.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 И избавиши мя от пререкания людий моих, сохраниши мя в главу языков. И людие, ихже не ведях, работаша ми.
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 Сынове чуждии солгаша ми, в слух уха услыша мя:
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 сынове чуждии отвержени будут, и вострепещут во градех своих.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 Жив Господь, и благословен хранитель мой, и вознесется Бог мой, хранитель спасения моего.
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 Крепкий Господь даяй отмщения мне и наказуяй люди под мя,
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 и изводяй мя от враг моих, и от востающих на мя вознесеши мя, от мужа неправедна избавиши мя.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Сего ради исповемся Тебе, Господи, во языцех, и имени Твоему воспою:
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 величаяй спасения царя Своего, и творяй милость христу Своему Давиду и семени его до века.
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< Вторая книга Царств 22 >