< Третья книга Царств 2 >

1 И приближишася Давиду дние умрети ему, и заповеда Соломону сыну своему, глаголя:
Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
2 аз отхожду в путь всея земли: ты же крепися, и буди муж совершен,
“Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
3 и сохрани завет Господа Бога твоего, еже ходити во всех путех Его, хранити заповеди Его и оправдания Его, и судбы Его и свидения Его, писанная в законе Моисеове: да разумееши яже сотвориши по всем, елика заповедах тебе:
ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
4 да утвердит Господь слово Свое, еже рече о мне, глаголя: аще сохранят сынове твои пути своя, еже ходити предо Мною во истине всем сердцем своим и всею душею своею, глаголя: не искоренится тебе муж с престола Израилева:
Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
5 и ты веси, елика сотвори мне Иоав сын Саруин, елика сотвори двема воеводама сил Израилевых, Авениру сыну Нирову и Амессаю сыну Иеферову, и уби их, и излия крови брани в мире, и даде кровь неповинных на поясе своем, иже на чреслех его, и на сапозе своем сущем на нозе его:
“Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
6 и сотвориши по мудрости твоей, и не сведеши старости его с миром во ад: (Sheol h7585)
Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
7 сыном же Верзеллии Галаадитина сотвориши милость, и да будут с ядущими трапезу твою: яко тако приближишася мне, внегда бежати мне от лица Авессалома брата твоего:
“Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
8 и се, с тобою Семей сын Гирань сын Иемениин от Ваурима, и той прокля мя проклятием горьким, в день в оньже исхождах в Полки: и той сниде на сретение ми на Иордан, и кляхся ему о Господе, глаголя: не убию тя оружием:
“Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
9 и да не обезвиниши его, яко муж мудр еси ты, и увеси что сотвориши ему, и сведеши старость его с кровию во ад. (Sheol h7585)
Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
10 И успе Давид со отцы своими, и погребен бысть во граде Давидове.
Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
11 И бысть дний, в няже царствова Давид во Израили, четыредесять лет: в Хевроне царствова седмь лет, во Иерусалиме же тридесять три лета.
Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
12 И Соломон седе на престоле Давида отца своего сын дванадесяти лет, и уготовася царствие его зело.
Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
13 И вниде Адониа сын Аггифин к Вирсавии матери Соломони, и поклонися ей. Она же рече: мир ли вход твой? И рече: мир.
Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
14 И рече: слово мне к тебе. И рече ему: глаголи.
Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
15 И рече ей: ты веси, яко мне бе царство, и на мя весь Израиль положи лице свое, еже царствовати, и обратися царство, и бысть брату моему, яко от Господа бысть ему:
Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
16 и ныне прошения единаго аз прошу от тебе, не отврати лица своего. И рече ему Вирсавиа: глаголи.
Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
17 И рече к ней: рцы к Соломону царю, яко не имать отвратити лица своего от тебе, и дабы ми дал Ависагу Сумантяныню в жену.
Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
18 И рече Вирсавиа: добре, аз имам глаголати о тебе к царю.
Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
19 И вниде Вирсавиа пред царя Соломона глаголати ему о Адонии. И воста царь на сретение ей, и поклонися ей, и седе на престоле своем: и поставиша престол другий матери цареве, и седе одесную его,
Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
20 и рече ему: прошения мала единаго аз прошу у тебе, не отврати лица моего. И рече к ней царь: проси, мати моя, яко не отвращуся от тебе.
Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
21 И рече: даждь Ависагу Сумантяныню Адонии брату твоему в жену.
Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
22 И отвеща царь Соломон и рече матери своей: вскую ты просиши Ависаги Сумантяныни Адонии? Еще проси ему и царства, яко той брат мой болший мене, и ему Авиафар иерей, и ему Иоав сын Саруин воевода друг.
Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
23 И клятся царь Соломон Господем, глаголя: сия да сотворит мне Бог и сия да приложит, яко на душу свою глагола Адониа слово сие:
Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
24 и ныне жив Господь, Иже уготова мя, и посади мя на престоле отца моего Давида, и Той сотвори ми дом, якоже глагола Господь, яко днесь умрет Адониа.
Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
25 И посла царь Соломон рукою Ванеа сына Иодаева, и уби его, и умре Адониа в той день.
Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
26 И Авиафару иерею рече царь: тецы ты во Анафоф на село твое, яко муж смерти еси ты в днешний день, но не умерщвлю тебе, яко носил еси кивот завета Господня пред отцем моим (Давидом), и яко озлоблен был еси во всех, имиже озлоблен бе отец мой.
Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
27 И изгна Соломон Авиафара, еже не быти ему иереем Господним, якоже сбытися словеси Господню, еже глагола на дом Илиев в Силоме.
Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
28 И слух дойде до Иоава сына Саруина, яко Иоав последова Адонии, и в след Соломонь не уклонися. И бежа Иоав в скинию Господню, и ятся рогов олтаревых.
Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
29 И возвестиша Соломону, глаголюще: яко бежа Иоав в скинию Господню, и се, держится рогов олтаревых. И посла царь Соломон ко Иоаву, глаголя: что ти бысть, яко убежал еси во олтарь? И рече Иоав: яко убояхся от лица твоего, и бежах ко Господу. И посла Соломон Ванеа сына Иодаева, глаголя: иди, и убий его, и погреби его.
Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
30 И прииде Ванеа сын Иодаев ко Иоаву в скинию Господню, и рече ему: сия глаголет царь: изыди. И рече Иоав: не изыду, но да зде умру. И возвратися Ванеа сын Иодаев и рече царю, глаголя: сия глагола Иоав и сия отвеща мне.
Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
31 И рече ему царь: иди и сотвори ему, якоже рече, и убий его, и погреби его, и отими днесь кровь, юже туне пролия Иоав, от мене и от дому отца моего:
Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
32 и возврати Господь кровь неправды его на главу его, якоже нападе на два мужа праведна и блага паче его, и уби их оружием: и отец мой Давид не разуме крове их, Авенира сына Нирова, воеводу Израилева, и Амессая сына Иеферова, воеводу Иудина:
Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
33 и возвратися кровь их на главу его и на главу семене его во веки: Давиду же и семени его, и дому его, и престолу его мир да будет до века от Господа.
Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
34 И взыде Ванеа сын Иодаев и нападе на него, и уби его, и погребе его в дому его в пустыни.
Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
35 И постави царь Соломон Ванеа сына Иодаева вместо его над воинством: царство же управляшеся во Иерусалиме. И Садока иереа даде Соломон царь во иереа перваго вместо Авиафара.
Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
36 И послав царь Соломон, призва Семеа и рече ему: созижди себе дом во Иерусалиме и седи тамо, и не исходи оттуду никаможе:
Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
37 и будет в день исхода твоего, и прейдеши поток Кедрский, разумея разумей, яко смертию умреши: кровь твоя будет на главе твоей. И заклят его царь в день той.
Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
38 И рече Семей к царю: благ глагол, егоже глаголал еси, господи мой царю: тако сотворит раб твой. И седе Семей во Иерусалиме три лета.
Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
39 И бысть по триех летех, и бежаста два раба Семеина ко Агхусу сыну Маахаину, царю Гефску. И возвестиша Семею, глаголюще: се, раби твои во Гефе.
Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
40 И воста Семей, и оседла осля свое, и иде во Геф ко Агхусу взыскати рабы своя: и пойде Семей, и приведе рабы своя от Гефа.
Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
41 И возвестиша Соломону, глаголюще: яко Семей ходи из Иерусалима в Геф и возврати рабы своя.
Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
42 И посла царь и призва Семеа и рече к нему: не заклях ли тя Господем, и засвидетелствовах тебе, глаголя: в оньже аще день изыдеши из Иерусалима и пойдеши на десно или на шуее, разумея разумей, яко смертию умреши? И рекл ми еси: благ глагол, егоже слышах:
mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
43 и что яко не сохранил еси клятвы Господни и заповеди, юже заповедах на тя?
Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
44 И рече царь к Семею: ты веси всю злобу твою, юже весть сердце твое, яже сотворил еси Давиду отцу моему: и возврати Господь злобу твою на главу твою:
Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
45 и царь Соломон благословен, и престол Давидов будет готов пред Господем во веки.
Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
46 И заповеда царь Соломон Ванею сыну Иодаеву: и изыде, и уби его, и умре (Семей).
Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.

< Третья книга Царств 2 >