< Вторая книга Паралипоменон 24 >

1 Седми лет бе Иоас, егда царствовати нача, и четыредесять лет царствова во Иерусалиме. Имя же матери его Савиа от Вирсавеи.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 Сотвори же Иоас угодное пред Господем во вся дни Иодаа священника.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
3 И поят ему Иодай жены две, и родиша сыны и дщери.
Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
4 И бысть по сих, и взыде на сердце Иоасу, да возновит дом Господень.
Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
5 И собра священники и левиты и рече им: идите во грады Иудины, и соберите от всего Израиля сребро ко обновлению храма Господня от лета до лета, и поспешно сотворите. Левити же не потщашася.
Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
6 И призва царь Иоас Иодаа началника и рече ему: почто не надсматрял еси левитов, еже принести от Иуды и от Иерусалима, еже уставлено есть от Моисеа человека Божия, егда собра Израиля в скинию свидения?
Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
7 Гофолиа бо бе нечестива, и сынове ея разориша дом Божий, яко святая дому Господня сотвориша Ваалиму.
Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
8 И повеле царь, да сотворят ковчежец и поставят при вратех Господних извне,
Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
9 и да проповедят во Иудеи и во Иерусалиме, приносити Господу, якоже устави Моисей раб Божий над Израилем в пустыни.
Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
10 И даша вси началницы и вси людие, и вношаху и влагаху в ковчежец, дондеже наполнися.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
11 И бысть егда приношаху ковчежец к настоятелем царевым руками левитскими, и егда увидеша, яко умножися сребро, и прихождаше писарь царев и настоятель великаго жерца, и выбираху из ковчежца, и (паки) поставляху на место его: тако творяху от дне до дне, и собраша сребра много.
Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
12 И вдаде е царь и Иодай жрец творящым дела на дело дому Господня: и наимаху каменосечцы и древодели, да устрояют дом Господень, и ковачы железу и меди, да укрепят дом Господень.
Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
13 И творяху творящии дела, и взыде долгота дел руками их, и возставиша дом Господень в состояние (прежнее) его, и укрепиша.
Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
14 Егда же совершиша, принесоша ко царю и ко Иодаю останок сребра, из негоже сотвориша сосуды в дом Господень, сосуды в служение всесожжений, и кадилницы златыя и сребряныя, и приношаху всесожжения в дому Господни непрестанно, во вся дни Иодаевы.
Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
15 И состареся Иодай исполнен дний, и умре сый ста тридесяти лет внегда скончатися ему:
Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
16 и погребоша его во граде Давидове со царми, понеже сотвори благое со Израилем и с Богом и с домом Его.
Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
17 И бысть по скончании Иодаеве, внидоша началницы Иудины и поклонишася царю: тогда послуша их царь.
Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
18 И оставиша церковь Господа Бога отец своих и служаху Астарте и истуканным: и бысть гнев (Господень) на Иуду и Иерусалим в день той.
Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
19 И посла к ним пророки, да обратятся ко Господу, и не послушаша: и засвидетелствова им, и не покоришася.
Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
20 И Дух Божий облече Азарию священника сына Иодаева, и ста пред людьми и рече им: сия глаголет Господь: почто преступаете повеления Господня? Не поспешится вам, яко остависте Господа, и оставит вас.
Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
21 И нападоша на него и побиша и камением по повелению Иоаса царя, во дворе дому Господня.
Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
22 И не воспомяну Иоас царь милосердия, еже сотвори Иодай отец его с ним, но уби сына его: иже, егда умираше, рече: да видит и судит Господь.
Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
23 И бысть по скончании лета, воста на него сила Сирская, и прииде на Иуду и на Иерусалим, и убиша вся началники в людех в церкви, и весь плен их послаша ко царю в Дамаск:
Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
24 зане в малых мужех прииде сила Сирская, и Бог предаде в руце их силу многу зело, зане оставиша Господа Бога отец своих: и на Иоаса сотвори суд.
Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
25 И по отшествии их от него, оставлену ему сущу в болезнех великих, и нападоша на него раби его за кровь священника сына Иодаева, и убиша его на постели его, и умре: и погребоша его во граде Давидове, но не погребоша его во гробех царских.
Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
26 Нападшии же на него, Завед сын Семаафов Амманитянин и Иозавед сын Самарифов Моавитянин,
Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
27 и сынове его вси, и приступиша к нему пять. И прочая словес его, се, написана в летописце царстем. И воцарися Амасиа сын его вместо его.
Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< Вторая книга Паралипоменон 24 >