< Псалтирь 25 >

1 Псалом Давида. К Тебе, Господи, возношу душу мою.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Боже мой! на Тебя уповаю, да не постыжусь, да не восторжествуют надо мною враги мои,
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 да не постыдятся и все надеющиеся на Тебя: да постыдятся беззаконнующие втуне.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Укажи мне, Господи, пути Твои и научи меня стезям Твоим.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Направь меня на истину Твою и научи меня, ибо Ты Бог спасения моего; на Тебя надеюсь всякий день.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Вспомни щедроты Твои, Господи, и милости Твои, ибо они от века.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Грехов юности моей и преступлений моих не вспоминай; по милости Твоей вспомни меня Ты, ради благости Твоей, Господи!
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Благ и праведен Господь, посему наставляет грешников на путь,
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 направляет кротких к правде, и научает кротких путям Своим.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Все пути Господни - милость и истина к хранящим завет Его и откровения Его.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Ради имени Твоего, Господи, прости согрешение мое, ибо велико оно.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Кто есть человек, боящийся Господа? Ему укажет Он путь, который избрать.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Душа его пребудет во благе, и семя его наследует землю.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Тайна Господня - боящимся Его, и завет Свой Он открывает им.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Очи мои всегда к Господу, ибо Он извлекает из сети ноги мои.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Призри на меня и помилуй меня, ибо я одинок и угнетен.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Скорби сердца моего умножились; выведи меня из бед моих,
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 призри на страдание мое и на изнеможение мое и прости все грехи мои.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Посмотри на врагов моих, как много их, и какою лютою ненавистью они ненавидят меня.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Сохрани душу мою и избавь меня, да не постыжусь, что я на Тебя уповаю.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Непорочность и правота да охраняют меня, ибо я на Тебя надеюсь.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Избавь, Боже, Израиля от всех скорбей его.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Псалтирь 25 >