< Псалтирь 24 >

1 Псалом Давида. Господня земля и что наполняет ее, вселенная и все живущее в ней,
Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
2 ибо Он основал ее на морях и на реках утвердил ее.
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
3 Кто взойдет на гору Господню, или кто станет на святом месте Его?
Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
4 Тот, у которого руки неповинны и сердце чисто, кто не клялся душою своею напрасно и не божился ложно, -
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
5 тот получит благословение от Господа и милость от Бога, Спасителя своего.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
6 Таков род ищущих Его, ищущих лица Твоего, Боже Иакова!
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
7 Поднимите, врата, верхи ваши, и поднимитесь, двери вечные, и войдет Царь славы!
Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
8 Кто сей Царь славы? - Господь крепкий и сильный, Господь, сильный в брани.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
9 Поднимите, врата, верхи ваши, и поднимитесь, двери вечные, и войдет Царь славы!
Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Кто сей Царь славы? - Господь сил, Он - царь славы.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)

< Псалтирь 24 >