< Притчи 29 >

1 Человек, который, будучи обличаем, ожесточает выю свою, внезапно сокрушится, и не будет ему исцеления.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 Когда умножаются праведники, веселится народ, а когда господствует нечестивый, народ стенает.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 Человек, любящий мудрость, радует отца своего; а кто знается с блудницами, тот расточает имение.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 Царь правосудием утверждает землю, а любящий подарки разоряет ее.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 Человек, льстящий другу своему, расстилает сеть ногам его.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 В грехе злого человека - сеть для него, а праведник веселится и радуется.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Праведник тщательно вникает в тяжбу бедных, а нечестивый не разбирает дела.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Люди развратные возмущают город, а мудрые утишают мятеж.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 Умный человек, судясь с человеком глупым, сердится ли, смеется ли, - не имеет покоя.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 Кровожадные люди ненавидят непорочного, а праведные заботятся о его жизни.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 Глупый весь гнев свой изливает, а мудрый сдерживает его.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 Если правитель слушает ложные речи, то и все служащие у него нечестивы.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 Бедный и лихоимец встречаются друг с другом; но свет глазам того и другого дает Господь.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 Если царь судит бедных по правде, то престол его навсегда утвердится.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 Розга и обличение дают мудрость; но отрок, оставленный в небрежении, делает стыд своей матери.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 При умножении нечестивых умножается беззаконие; но праведники увидят падение их.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Наказывай сына твоего, и он даст тебе покой, и доставит радость душе твоей.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 Без откровения свыше народ необуздан, а соблюдающий закон блажен.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 Словами не научится раб, потому что, хотя он понимает их, но не слушается.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 Видал ли ты человека опрометчивого в словах своих? на глупого больше надежды, нежели на него.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 Если с детства воспитывать раба в неге, то впоследствии он захочет быть сыном.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 Человек гневливый заводит ссору, и вспыльчивый много грешит.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 Гордость человека унижает его, а смиренный духом приобретает честь.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 Кто делится с вором, тот ненавидит душу свою; слышит он проклятие, но не объявляет о том.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 Боязнь пред людьми ставит сеть; а надеющийся на Господа будет безопасен.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Многие ищут благосклонного лица правителя, но судьба человека - от Господа.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 Мерзость для праведников - человек неправедный, и мерзость для нечестивого - идущий прямым путем.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.

< Притчи 29 >