< Притчи 28 >

1 Нечестивый бежит, когда никто не гонится за ним; а праведник смел, как лев.
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 Когда страна отступит от закона, тогда много в ней начальников; а при разумном и знающем муже она долговечна.
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 Человек бедный и притесняющий слабых то же, что проливной дождь, смывающий хлеб.
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 Отступники от закона хвалят нечестивых, а соблюдающие закон негодуют на них.
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Злые люди не разумеют справедливости, а ищущие Господа разумеют все.
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 Лучше бедный, ходящий в своей непорочности, нежели тот, кто извращает пути свои, хотя он и богат.
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 Хранящий закон - сын разумный, а знающийся с расточителями срамит отца своего.
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 Умножающий имение свое ростом и лихвою соберет его для благотворителя бедных.
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 Кто отклоняет ухо свое от слушания закона, того и молитва - мерзость.
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Совращающий праведных на путь зла сам упадет в свою яму, а непорочные наследуют добро.
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 Человек богатый - мудрец в глазах своих, но умный бедняк обличит его.
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 Когда торжествуют праведники, великая слава, но когда возвышаются нечестивые, люди укрываются.
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 Скрывающий свои преступления не будет иметь успеха; а кто сознается и оставляет их, тот будет помилован.
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 Блажен человек, который всегда пребывает в благоговении; а кто ожесточает сердце свое, тот попадет в беду.
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 Как рыкающий лев и голодный медведь, так нечестивый властелин над бедным народом.
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 Неразумный правитель много делает притеснений, а ненавидящий корысть продолжит дни.
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 Человек, виновный в пролитии человеческой крови, будет бегать до могилы, чтобы кто не схватил его.
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
18 Кто ходит непорочно, тот будет невредим; а ходящий кривыми путями упадет на одном из них.
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 Кто возделывает землю свою, тот будет насыщаться хлебом, а кто подражает праздным, тот насытится нищетою.
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 Верный человек богат благословениями, а кто спешит разбогатеть, тот не останется ненаказанным.
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 Быть лицеприятным - нехорошо: такой человек и за кусок хлеба сделает неправду.
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 Спешит к богатству завистливый человек, и не думает, что нищета постигнет его.
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 Обличающий человека найдет после большую приязнь, нежели тот, кто льстит языком.
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 Кто обкрадывает отца своего и мать свою и говорит: “это не грех”, тот - сообщник грабителям.
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 Надменный разжигает ссору, а надеющийся на Господа будет благоденствовать.
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 Кто надеется на себя, тот глуп; а кто ходит в мудрости, тот будет цел.
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 Дающий нищему не обеднеет; а кто закрывает глаза свои от него, на том много проклятий.
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 Когда возвышаются нечестивые, люди укрываются, а когда они падают, умножаются праведники.
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< Притчи 28 >