< К Филимону 1 >

1 Павел, узник Иисуса Христа, и Тимофей брат, Филимону возлюбленному и сотруднику нашему,
Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu. Kulembera Filemoni, bwenzi lathu lokondedwa ndi mtumiki mnzathu.
2 и Апфии, сестре возлюбленной, и Архиппу, сподвижнику нашему, и домашней твоей церкви:
Kwa Apiya mlongo wathu, Arkipo msilikali mnzathu, ndiponso mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwanu.
3 благодать вам и мир от Бога Отца нашего и Господа Иисуса Христа.
Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
4 Благодарю Бога моего, всегда вспоминая о тебе в молитвах моих,
Ine ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakukumbukira iwe mʼmapemphero anga.
5 слыша о твоей любви и вере, которую имеешь к Господу Иисусу и ко всем святым,
Pakuti ndamva za chikondi chako, za chikhulupiriro chako mwa Ambuye Yesu ndiponso za chikondi chako pa oyera mtima onse.
6 дабы общение веры твоей оказалось деятельным в познании всякого у вас добра во Христе Иисусе.
Ine ndikupemphera kuti mgwirizano wako ndi ife mʼchikhulupiriro ukhale opindulitsa pozamitsa nzeru zako zozindikira zinthu zilizonse zabwino zimene timagawana chifukwa cha Khristu.
7 Ибо мы имеем великую радость и утешение в любви твоей, потому что тобою, брат, успокоены сердца святых.
Mʼbale, chikondi chako chandipatsa chimwemwe chachikulu ndi chilimbikitso, chifukwa umatsitsimutsa mitima ya anthu a Ambuye.
8 Посему, имея великое во Христе дерзновение приказывать тебе, что должно,
Tsopano ngakhale kuti mwa Khristu nditha kulimba mtima ndi kulamulira kuti uchite zimene uyenera kuchita,
9 по любви лучше прошу, не иной кто, как я, Павел старец, а теперь и узник Иисуса Христа;
komabe ndikupempha mwachikondi. Ine Paulo, munthu wokalamba, ndipo tsopano ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu,
10 прошу тебя о сыне моем Онисиме, которого родил я в узах моих:
ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.
11 он был некогда негоден для тебя, а теперь годен тебе и мне; я возвращаю его;
Anali wopanda phindu kwa iwe, koma tsopano wasanduka wa phindu kwa iwe ndi kwa inenso.
12 ты же прими его, как мое сердце.
Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.
13 Я хотел при себе удержать его, дабы он вместо тебя послужил мне в узах за благовествование;
Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.
14 но без твоего согласия ничего не хотел сделать, чтобы доброе дело твое было не вынужденно, а добровольно.
Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, nʼcholinga chakuti chilichonse chabwino ungandichitire chikhale mwakufuna kwako osati mokakamiza.
15 Ибо, может быть, он для того на время отлучился, чтобы тебе принять его навсегда, (aiōnios g166)
Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse. (aiōnios g166)
16 не как уже раба, но выше раба, брата возлюбленного, особенно мне, а тем больше тебе, и по плоти и в Господе.
Osati ngati kapolo, koma woposa kapolo, ngati mʼbale wokondedwa. Iyeyu ndi wokondedwa kwambiri kwa ine koma kwa iweyo ndi wokondedwa koposa, ngati munthu komanso ngati mʼbale mwa Ambuye.
17 Итак, если ты имеешь общение со мною, то прими его, как меня.
Tsono ngati umati ndine mnzako, umulandire iyeyu monga momwe ukanandilandirira ineyo.
18 Если же он чем обидел тебя или должен, считай это на мне.
Ngati anakulakwira kapena kukongola kanthu kalikonse, ndidzalipira ineyo.
19 Я, Павел, написал моею рукою: я заплачу; не говорю тебе о том, что ты и самим собою мне должен.
Ine, Paulo ndikulemba zimenezi ndi dzanja langa. Ine ndidzalipira. Nʼkosafunika kukukumbutsa kuti iweyo ngongole yako kwa ine ndi moyo wakowo.
20 Так, брат, дай мне воспользоваться от тебя в Господе; успокой мое сердце в Господе.
Mʼbale, ndikufuna kuti ndipindule nawe mwa Ambuye; tsono tsitsimutsa mtima wanga mwa Khristu.
21 Надеясь на послушание твое, я написал к тебе, зная, что ты сделаешь и более, нежели говорю.
Ine ndili ndi chitsimikizo cha kumvera kwako pamene ndikukulembera kalatayi. Ndikulemba ndikudziwa kuti udzachita ngakhale kuposa zimene ndakupemphazi.
22 А вместе приготовь для меня и помещение; ибо надеюсь, что по молитвам вашим я буду дарован вам.
Chinthu chinanso ndi ichi: undikonzere malo, chifukwa ndikukhulupirira kuti Mulungu adzamvera mapemphero anu ndi kundibwezera kwa inu.
23 Приветствует тебя Епафрас, узник вместе со мною ради Христа Иисуса,
Epafra, wamʼndende mnzanga chifukwa cha Khristu Yesu akupereka moni.
24 Марк, Аристарх, Димас, Лука, сотрудники мои.
Atumiki anzanga awa, Marko, Aristariko, Dema ndi Luka, akuperekanso moni.
25 Благодать Господа нашего Иисуса Христа со духом вашим. Аминь.
Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wako.

< К Филимону 1 >