< Иеремия 41 >

1 И было в седьмой месяц, Исмаил, сын Нафании, сына Елисама из племени царского, и вельможи царя и десять человек с ним пришли к Годолии, сыну Ахикама, в Массифу, и там они ели вместе хлеб в Массифе.
Pa mwezi wachisanu ndi chiwiri Ismaeli mwana wa Netaniya, mdzukulu wa Elisama amene anali wa banja laufumu ndiponso mmodzi wa atsogoleri a ankhondo a mfumu, anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ndi anthu khumi. Pamene ankadya naye kumeneko,
2 И встал Исмаил, сын Нафании, и десять человек, которые были с ним, и поразили Годолию, сына Ахикама, сына Сафанова, мечом и умертвили того, которого царь Вавилонский поставил начальником над страною.
Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu khumi aja anayimirira ndi kupha ndi lupanga Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani. Choncho anapha munthu amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.
3 Также убил Исмаил и всех Иудеев, которые были с ним, с Годолиею, в Массифе, и находившихся там Халдеев, людей военных.
Ismaeli anaphanso Ayuda onse amene anali pamodzi ndi Gedaliya ku Mizipa, kuphatikizanso asilikali a Ababuloni amene anali ku Mizipako.
4 На другой день по убиении Годолии, когда никто не знал об этом,
Mmawa mwake, anthu asanadziwe kuti Gedaliya waphedwa,
5 пришли из Сихема, Силома и Самарии восемьдесят человек с обритыми бородами и в разодранных одеждах, и изранив себя, с дарами и ливаном в руках для принесения их в дом Господень.
kunafika anthu 80 ochekera ku Sekemu, Silo ndi Samariya, amene anali atameta ndevu zawo, atangʼamba zovala zawo ndi kudzichekacheka. Iwowa anatenga chopereka cha ufa ndi lubani kuti adzapereke ku Nyumba ya Yehova.
6 Исмаил, сын Нафании, вышел из Массифы навстречу им, идя и плача, и, встретившись с ними, сказал им: идите к Годолии, сыну Ахикама.
Ismaeli mwana wa Netaniya anachoka ku Mizipa akulira kupita kukakumana nawo. Atakumana nawo, iye anati, “Bwerani mudzaonane ndi Gedaliya mwana wa Ahikamu.”
7 И как только они вошли в средину города, Исмаил, сын Нафании, убил их и бросил в ров, он и бывшие с ним люди.
Atafika pakati pa mzinda, Ismaeli mwana wa Netaniya pamodzi ndi anthu amene anali naye anawapha anthuwo ndi kuwaponya mʼchitsime.
8 Но нашлись между ними десять человек, которые сказали Исмаилу: не умерщвляй нас, ибо у нас есть в поле скрытые кладовые с пшеницею и ячменем, и маслом и медом. И он удержался и не умертвил их с другими братьями их.
Koma anthu khumi a gululo anawuza Ismaeli kuti, “Musatiphe! Tili ndi tirigu ndi barele, mafuta ndi uchi, zimene tabisa mʼmunda.” Choncho anawasiya ndipo sanawaphere pamodzi ndi anzawo aja.
9 Ров же, куда бросил Исмаил все трупы людей, которых он убил из-за Годолии, был тот самый, который сделал царь Аса, боясь Ваасы, царя Израильского; его наполнил Исмаил, сын Нафании, убитыми.
Tsono chitsime chimene anaponyamo mitembo ya anthu amene anawaphawo pamodzi ndi mtembo wa Gedaliya chinali chimene mfumu Asa anachikumba poopsedwa ndi Baasa mfumu ya Israeli. Ismaeli mwana wa Netaliya anachidzaza ndi mitembo.
10 И захватил Исмаил весь остаток народа, бывшего в Массифе, дочерей царя и весь остававшийся в Массифе народ, который Навузардан, начальник телохранителей, поручил Годолии, сыну Ахикама, и захватил их Исмаил, сын Нафании, и отправился к сыновьям Аммоновым.
Pambuyo pake Ismaeli anatenga ukapolo anthu ena onse amene anali ku Mizipa: ana aakazi a mfumu pamodzi ndi ena onse amene anatsalira kumeneko, amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anapatsa Gedaliya mwana wa Ahikamu kuti akhale bwanamkubwa wawo. Ismaeli mwana wa Netaliya anatenga ukapolo anthuwa ndi kuwoloka nawo kumapita ku dziko la Aamoni.
11 Но когда Иоанан, сын Карея, и все бывшие с ним военные начальники услышали о всех злодеяниях, какие совершил Исмаил, сын Нафании,
Pamene Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye pamodzi anamva zoyipa zonse zimene Ismaeli mwana wa Netaniya anachita,
12 взяли всех людей и пошли сразиться с Исмаилом, сыном Нафании, и настигли его у больших вод, в Гаваоне.
anatenga ankhondo awo onse kupita kukamenyana ndi Ismaeli mwana wa Netaniya. Anakamupeza kufupi ndi chidziwe chachikulu cha ku Gibiyoni.
13 И когда весь народ, бывший у Исмаила, увидел Иоанана, сына Карея, и всех бывших с ним военных начальников, обрадовался;
Pamene anthu onse amene Ismaeli anawagwira anaona Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali naye, anasangalala.
14 и отворотился весь народ, который Исмаил увел в плен из Массифы, и обратился и пошел к Иоанану, сыну Карея;
Anthu onse amene Ismaeli anawagwira ukapolo ku Mizipa anabwerera ndi kupita kwa Yohanani mwana wa Kareya.
15 а Исмаил, сын Нафании, убежал от Иоанана с восемью человеками и ушел к сыновьям Аммоновым.
Koma Ismaeli pamodzi ndi anthu ake asanu ndi atatu, anathawa Yohanani ndi kuthawira kwa Aamoni.
16 Тогда Иоанан, сын Карея, и все бывшие с ним военные начальники взяли из Массифы весь оставшийся народ, который он освободил от Исмаила, сына Нафании, после того как тот убил Годолию, сына Ахикама, мужчин, военных людей, и жен, и детей, и евнухов, которых он вывел из Гаваона;
Kenaka Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye anatsogolera anthu onse otsala a ku Mizipa amene anawapulumutsa kwa Ismaeli mwana wa Netaniya atapha Gedaliya mwana wa Ahikamu. Anthu amenewa anali: asilikali, akazi, ana ndi amuna ofulidwa otumikira mfumu amene anawatenga ku Gibiyoni.
17 и пошли, и остановились в селении Химам, близ Вифлеема, чтобы уйти в Египет
Ndipo ananyamuka nayima ku Geruti Kimuhamu pafupi ndi Betelehemu pa ulendo wawo wopita ku Igupto
18 от Халдеев, ибо они боялись их, потому что Исмаил, сын Нафании, убил Годолию, сына Ахикама, которого царь Вавилонский поставил начальником над страною.
kuthawa Ababuloni. Iwo anaopa Ababuloniwo chifukwa Ismaeli mwana wa Netaniya anapha Gedaliya mwana wa Ahikamu, amene mfumu ya ku Babuloni inamuyika kukhala bwanamkubwa wa dzikolo.

< Иеремия 41 >