< Иеремия 40 >

1 Слово, которое было к Иеремии от Господа, после того как Навузардан, начальник телохранителей, отпустил его из Рамы, где он взял его скованного цепями среди прочих пленных Иерусалимлян и Иудеев, переселяемых в Вавилон.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya pamene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anamasula Yeremiyayo ku Rama. Anamupeza Yeremiya ali womangidwa ndi unyolo pamodzi ndi amʼndende ena onse a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene ankapita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
2 Начальник телохранителей взял Иеремию и сказал ему: Господь Бог твой изрек это бедствие на место сие,
Mtsogoleriyu anamupeza Yeremiya, anamuwuza kuti, “Yehova Mulungu wako analengeza kale zakuti malo ano adzawonongedwa.
3 и навел его Господь и сделал то, что сказал; потому что вы согрешили пред Господом и не слушались гласа Его, за то и постигло вас это.
Ndipo tsopano Yehova wachitadi zimenezi monga mmene ananenera. Izi zonse zachitika chifukwa anthu inu munachimwira Yehova ndipo simunamumvere.
4 Итак вот, я освобождаю тебя сегодня от цепей, которые на руках твоих: если тебе угодно идти со мною в Вавилон, иди, и я буду иметь попечение о тебе; а если не угодно тебе идти со мною в Вавилон, оставайся. Вот, вся земля перед тобою; куда тебе угодно, и куда нравится идти, туда и иди.
Koma tsopano taona, lero ndikukumasula unyolo umene unali mʼmanja mwako. Ngati ukufuna kupita nane ku Babuloni, tiye ndipo adzakusamala bwino. Koma ngati sukufuna kupita, ndiye usapite. Dziko ndi limeneli monga ukulioneramo. Uli ndi ufulu kupita kulikonse kumene ukufuna.”
5 Когда он еще не отошел, сказал Навузардан: пойди к Годолии, сыну Ахикама, сына Сафанова, которого царь Вавилонский поставил начальником над городами Иудейскими, и оставайся с ним среди народа; или иди, куда нравится тебе идти. И дал ему начальник телохранителей продовольствие и подарок и отпустил его.
Yeremiya asanayankhe, Nebuzaradani anamuwuzanso kuti, “Ngati supita ndiye pita, ubwerere kwa Gedaliya, mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kuti akhale bwanamkubwa wa Yuda. Ukakhale naye pakati pa anthu, kapena upite kulikonse ukufuna.” Ndipo mtsogoleri uja anamupatsa Yeremiya chakudya ndi mphatso zina ndi kumulola kuti apite.
6 И пришел Иеремия к Годолии, сыну Ахикама, в Массифу, и жил с ним среди народа, остававшегося в стране.
Motero Yeremiya anapita kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ku Mizipa ndipo anakakhala naye kumeneko pakati pa anthu amene anatsala mʼdzikomo.
7 Когда все военачальники, бывшие в поле, они и люди их, услышали, что царь Вавилонский поставил Годолию, сына Ахикама, начальником над страною и поручил ему мужчин и женщин, и детей, и тех из бедных страны, которые не были переселены в Вавилон;
Panali atsogoleri ena a nkhondo ndi anthu awo amene sanadzipereke nawo. Iwowa anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu kukhala bwanamkubwa wa dzikolo ndipo kuti yamuyika kukhala wolamulira amuna, akazi ndi ana amene anali osauka kwambiri mʼdzikomo, amene sanawagwire ukapolo kupita nawo ku Babuloni.
8 тогда пришли к Годолии в Массифу и Исмаил, сын Нафании, и Иоанан и Ионафан, сыновья Карея, и Сераия, сын Фанасмефа, и сыновья Офи из Нетофафы, и Иезония, сын Махафы, они и дружина их.
Iwowa anapita ku Mizipa kwa Gedaliya. Amene anapitawo ndi awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani ndi Yonatani ana a Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti, ana a Efai a ku Netofa, ndi Yezaniya mwana wa Maaka, iwowo pamodzi ndi anthu awo.
9 Годолия, сын Ахикама, сына Сафанова, клялся им и людям их, говоря: не бойтесь служить Халдеям, оставайтесь на земле и служите царю Вавилонскому, и будет вам хорошо;
Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, anawalonjeza iwo pamodzi ndi anthuwo mwalumbiro. Ndipo anati, “Musaope kuwatumikira Ababuloni. Khalani mʼdziko muno, tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
10 а я останусь в Массифе, чтобы предстательствовать пред лицем Халдеев, которые будут приходить к нам; вы же собирайте вино и летние плоды, и масло и убирайте в сосуды ваши, и живите в городах ваших, которые заняли.
Ine ndidzakhala ku Mizipa kuti ndizikuyimirirani kwa Ababuloni amene azidzabwera kwa ife, koma inu muzikolola vinyo wanu, zipatso zanu, mafuta anu ndi kuzisunga mʼmitsuko yanu, nʼkumakhala mʼmizinda imene mwalandayo.”
11 Также все Иудеи, которые находились в земле Моавитской и между сыновьями Аммона и в Идумее, и во всех странах, услышали, что царь Вавилонский оставил часть Иудеев и поставил над ними Годолию, сына Ахикама, сына Сафана:
Nawonso Ayuda onse a ku Mowabu, ku Amoni, ku Edomu ndi a ku mayiko ena onse anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasiyako anthu ena ku Yuda ndipo kuti inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala bwanamkubwa wawo.
12 и возвратились все сии Иудеи из всех мест, куда были изгнаны, и пришли в землю Иудейскую к Годолии в Массифу, и собрали вина и летних плодов очень много.
Tsono Ayuda onsewo anabwerera ku Yuda, ku Mizipa kwa Gedaliya, kuchokera ku mayiko onse kumene anabalalikira. Ndipo anakolola zipatso zochuluka ndi vinyo wambiri.
13 Между тем Иоанан, сын Карея, и все военные начальники, бывшие в поле, пришли к Годолии в Массифу
Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri a ankhondo onse amene sanadzipereke aja anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya
14 и сказали ему: знаешь ли ты, что Ваалис, царь сыновей Аммоновых, прислал Исмаила, сына Нафании, чтобы убить тебя? Но Годолия, сын Ахикама, не поверил им.
ndipo anamufunsa kuti, “Kodi sukudziwa kuti Baalisi mfumu ya Aamoni watuma Ismaeli mwana wa Netaniya kuti akuphe?” Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu sanawankhulupirire.
15 Тогда Иоанан, сын Карея, сказал Годолии тайно в Массифе: позволь мне, я пойду и убью Исмаила, сына Нафании, и никто не узнает; зачем допускать, чтобы он убил тебя, и чтобы все Иудеи, собравшиеся к тебе, рассеялись, и чтобы погиб остаток Иуды?
Tsono Yohanani mwana wa Kareya, mwamseri anawuza Gedaliya ku Mizipa kuti, “Loleni ndipite ndikaphe Ismaeli mwana wa Netaniya, ndipo palibe amene ati adziwe. Akuphereninji ndi kuchititsa Ayuda onse, amene akuzungulirani kuti abalalike ndi kuti otsala a ku Yuda awonongeke?”
16 Но Годолия, сын Ахикама, сказал Иоанану, сыну Карея: не делай этого, ибо ты неправду говоришь об Исмаиле.
Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu anawuza Yohanani mwana wa Kareya kuti, “Usachite zimenezo! Zimene ukunena za Ismaeli ndi zabodza.”

< Иеремия 40 >