< 2-е Тимофею 2 >

1 Итак укрепляйся, сын мой, в благодати Христом Иисусом,
Tsono iwe, mwana wanga, limbika mʼchisomo chimene chili mwa Khristu Yesu.
2 и что слышал от меня при многих свидетелях, то передай верным людям, которые были бы способны и других научить.
Ndipo zinthu zimene unamva ine ndikuziyankhula pamaso pa mboni zambiri, uziphunzitse kwa anthu odalirika amene akaphunzitsenso ena.
3 Итак переноси страдания, как добрый воин Иисуса Христа.
Umve nane zowawa, monga msilikali wa Khristu Yesu.
4 Никакой воин не связывает себя делами житейскими, чтобы угодить военачальнику.
Palibe msilikali amene ali pa ntchito amagwiranso ntchito za anthu wamba, iye amafuna kukondweretsa bwana wolamulira.
5 Если же кто и подвизается, не увенчивается, если незаконно будет подвизаться.
Chimodzimodzinso, munthu amene ali pa mpikisano waliwiro, salandira mphotho ya wopambana pokhapokha atatsiriza monga mwa malamulo a mpikisanowo.
6 Трудящемуся земледельцу первому должно вкусить от плодов.
Mlimi wolimbika ndi amene amayembekezereka kukhala woyambirira kulandira gawo la zokolola.
7 Разумей, что я говорю. Да даст тебе Господь разумение во всем.
Lingalira zimene ndikunenazi, pakuti Ambuye adzakuzindikiritsa zonsezi.
8 Помни Господа Иисуса Христа от семени Давидова, воскресшего из мертвых, по благовествованию моему,
Kumbukira Yesu Khristu wochokera ku mtundu wa Davide kuti anauka kwa akufa. Uwu ndiye uthenga wanga wabwino
9 за которое я страдаю даже до уз, как злодей; но для слова Божия нет уз.
umene ndikuwuvutikira choterewu mpaka kumangidwa ndi maunyolo ngati wakuba. Koma mawu a Mulungu sanamangidwe ndi maunyolo.
10 Посему я все терплю ради избранных, дабы и они получили спасение во Христе Иисусе с вечною славою. (aiōnios g166)
Choncho ndikupirira chilichonse chifukwa cha osankhidwa, kuti nawonso apulumutsidwe ndi Khristu Yesu ndi kulandira ulemerero wosatha. (aiōnios g166)
11 Верно слово: если мы с Ним умерли, то с Ним и оживем;
Mawu oyenera kuwadalira ndi awa: Ngati ife tinafa naye pamodzi, tidzakhalanso moyo pamodzi naye.
12 если терпим, то с Ним и царствовать будем; если отречемся, и Он отречется от нас;
Ngati tinapirira, tidzalamuliranso naye pamodzi. Ngati ife timukana, Iye adzatikananso.
13 если мы неверны, Он пребывает верен, ибо Себя отречься не может.
Ngati ndife osakhulupirika, Iye adzakhalabe wokhulupirika popeza sangathe kudzikana.
14 Сие напоминай, заклиная пред Господом не вступать в словопрения, что нимало не служит к пользе, а к расстройству слушающих.
Uziwakumbutsa anthu a Mulungu zinthu izi. Uwachenjeze pamaso pa Mulungu kuti asamakangane pa za mawu. Zimenezi nʼzopanda phindu ndipo zimangowononga amene akumvawo.
15 Старайся представить себя Богу достойным, делателем неукоризненным, верно преподающим слово истины.
Uyesetse kukhala wovomerezeka pamaso pa Mulungu monga wantchito wopanda chifukwa chochitira manyazi amene amalalikira mawu achoonadi molondola.
16 А непотребного пустословия удаляйся; ибо они еще более будут преуспевать в нечестии,
Upewe nkhani zopanda pake, zosalemekeza Mulungu, chifukwa anthu oyankhula zotere amanka napotokerapotokera.
17 и слово их, как рак, будет распространяться. Таковы Именей и Филит,
Chiphunzitso chawo chidzafalikira ngati chilonda. Mwa anthuwa muli Humenayo ndi Fileto.
18 которые отступили от истины, говоря, что воскресение уже было, и разрушают в некоторых веру.
Iwowa apatuka pa choonadi. Iwo amaphunzitsa kuti kuuka kwa akufa kunachitika kale, motero amawononga chikhulupiriro cha anthu ena.
19 Но твердое основание Божие стоит, имея печать сию: “познал Господь Своих”; и: “да отступит от неправды всякий, исповедующий имя Господа”.
Komabe maziko olimba, amene Mulungu anawayika ngokhazikika, ndipo mawu olembedwapo ndi awa: “Yehova amadziwa amene ndi ake,” ndiponso, “Aliyense amene amavomereza dzina la Ambuye ayenera kusiya zoyipa.”
20 А в большом доме есть сосуды не только золотые и серебряные, но и деревянные и глиняные; и одни в почетном, а другие в низком употреблении.
Mʼnyumba yayikulu simukhala ziwiya zagolide ndi zasiliva zokha, koma mumakhalanso zamtengo ndi zadothi. Zina zimakhala za ntchito yapamwamba, zina za ntchito wamba.
21 Итак кто будет чист от сего, тот будет сосудом в чести, освященным и благопотребным Владыке, годным на всякое доброе дело.
Munthu akadziyeretsa nʼkusiya ntchito za wambazi, adzakhala chiwiya cha ntchito yapamwamba, woyeretsedwa, ndi waphindu kwa Ambuye wake, wokonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.
22 Юношеских похотей убегай, а держись правды, веры, любви, мира со всеми призывающими Господа от чистого сердца.
Thawa zilakolako zoyipa zachinyamata. Funafuna chilungamo, chikhulupiriro, chikondi ndi mtendere pamodzi ndi amene akuyitanira pa dzina la Ambuye ndi mtima osadetsedwa.
23 От глупых и невежественных состязаний уклоняйся, зная, что они рождают ссоры;
Ukane matsutsano oyipa ndi opusa, chifukwa amayambitsa mikangano.
24 рабу же Господа не должно ссориться, но быть приветливым ко всем, учительным, незлобивым,
Ndiponso mtumiki wa Ambuye asamakangane ndi anthu, koma azikhala wachifundo kwa aliyense, wodziwa kuphunzitsa, osati wokalipakalipa.
25 с кротостью наставлять противников, не даст ли им Бог покаяния к познанию истины,
Otsutsana naye awalangize mofatsa, mwina Mulungu adzawapatsa mwayi woti asinthike ndi kuzindikira choonadi.
26 чтобы они освободились от сети диавола, который уловил их в свою волю.
Motero nzeru zawo zidzabweramo, ndipo adzathawa msampha wa mdierekezi, amene anawagwira ukapolo kuti azichita zofuna zake.

< 2-е Тимофею 2 >