< 1-е Тимофею 2 >

1 Итак, прежде всего прошу совершать молитвы, прошения, моления, благодарения за всех человеков,
Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
2 за царей и за всех начальствующих, дабы проводить нам жизнь тихую и безмятежную во всяком благочестии и чистоте,
Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
3 ибо это хорошо и угодно Спасителю нашему Богу,
Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
4 Который хочет, чтобы все люди спаслись и достигли познания истины.
amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
5 Ибо един Бог, един и посредник между Богом и человеками, человек Христос Иисус,
Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
6 предавший Себя для искупления всех. Таково было в свое время свидетельство,
Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
7 для которого я поставлен проповедником и Апостолом, - истину говорю во Христе, не лгу, - учителем язычников в вере и истине.
Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
8 Итак, желаю, чтобы на всяком месте произносили молитвы мужи, воздевая чистые руки без гнева и сомнения;
Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
9 чтобы также и жены, в приличном одеянии, со стыдливостью и целомудрием, украшали себя не плетением волос, не золотом, не жемчугом, не многоценною одеждою,
Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
10 но добрыми делами, как прилично женам, посвящающим себя благочестию.
Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
11 Жена да учится в безмолвии, со всякою покорностью;
Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
12 а учить жене не позволяю, ни властвовать над мужем, но быть в безмолвии.
Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
13 Ибо прежде создан Адам, а потом Ева;
Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
14 и не Адам прельщен; но жена, прельстившись, впала в преступление;
Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
15 впрочем, спасется через чадородие, если пребудет в вере и любви и в святости с целомудрием.
Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.

< 1-е Тимофею 2 >