< Hoseas 9 >

1 Gled dig ikke, Israel, og juble ikke, likesom folkene! For du har forlatt din Gud i hor; du har elsket horelønn på hvert sted hvor kornet treskes.
Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
2 Treskeplassen og vinpersen skal ikke kunne fø dem, og mosten skal slå feil for dem.
Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
3 De skal ikke bli boende i Herrens land; men Efra'im skal vende tilbake til Egypten, og i Assur skal de ete det som er urent.
Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
4 De skal ikke ofre vin til drikkoffer for Herren, og deres slaktoffer skal ikke behage ham; som sorgens brød skal de være for dem; alle som eter det, skal bli urene; for sitt brød har de for sig selv, det kommer ikke i Herrens hus.
Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
5 Hvad vil I gjøre på høitidsdagen, på Herrens festdag?
Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
6 For de drar bort for ødeleggelses skyld; Egypten skal samle dem, Memfis begrave dem; deres sølvsmykker skal nesler ta i eie, torner skal vokse i deres telt.
Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
7 Kommet er hjemsøkelsens dager, kommet er gjengjeldelsens dager; Israel skal få merke det: En dåre er profeten, avsindig er åndens mann, fordi din misgjerning er så stor og ditt fiendskap så sterkt.
Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
8 Efra'im ser sig om efter andre guder ved siden av min Gud; profeten er en fuglefangersnare på alle hans veier, bare fiendskap i hans Guds hus.
Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
9 De er sunket dypt i fordervelse, som i Gibeas dager; han skal komme deres misgjerning i hu, han skal hjemsøke dem for deres synder.
Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
10 Som druer i ørkenen fant jeg Israel, som den tidligste frukt på et fikentre i dets første tid så jeg eders fedre; men da de kom til Ba'al-Peor, vidde de sig til avgudsdyrkelsen og blev vederstyggelige likesom den de elsket.
“Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
11 Efra'ims herlighet skal flyve bort som en fugl. Ingen fødsel, intet fruktsommelig morsliv, ingen undfangelse!
Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
12 Ja, selv om de opfør sine barn, vil jeg gjøre dem barnløse, så intet menneske blir tilbake; for ve dem når jeg forlater dem!
Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
13 Efra'im er, som om jeg så bort til Tyrus, plantet på en eng; men Efra'im må føre sine barn ut til bøddelen.
Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
14 Gi dem, Herre! - Ja, hvad skal du gi dem? Gi dem morsliv som føder i utide, og bryster som er uttørket!
Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
15 All deres ondskap er samlet i Gilgal, ja, der har jeg fattet hat til dem; for deres onde gjerningers skyld vil jeg drive dem ut av mitt hus; jeg vil ikke elske dem mere, alle deres førere er oprørere.
“Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
16 Efra'im er ormstukket, deres rot er blitt tørr, frukt skal de ikke bære; om de enn føder, vil jeg drepe deres dyre livsfrukt.
Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
17 Min Gud skal forkaste dem, fordi de ikke har hørt på ham, og de skal vanke om blandt folkene som flyktninger.
Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.

< Hoseas 9 >