< Esaias 50 >

1 Så sier Herren: Hvor er eders mors skilsmissebrev, som jeg har jaget henne bort med? Eller hvem av dem som har noget å kreve av mig, har jeg solgt eder til? Nei, for eders misgjerningers skyld er I blitt solgt, og for eders overtredelsers skyld er eders mor blitt jaget bort.
Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
2 Hvorfor var det ingen til stede da jeg kom? Hvorfor var det ingen som svarte da jeg ropte? Er min hånd for kort til å forløse, eller er det ingen kraft hos mig til å frelse? Se, ved min trusel tørker jeg ut havet, gjør jeg elver til en ørk, så fiskene i dem stinker, fordi der intet vann er, og dør av tørst;
Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
3 jeg klær himmelen i sort og innhyller den i sørgedrakt.
Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
4 Herren, Israels Gud, har gitt mig en disippeltunge, så jeg skal kunne kvege den trette med mitt ord; han vekker mitt øre hver morgen, han vekker det forat jeg skal høre som disipler hører.
Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
5 Herren, Israels Gud, har åpnet mitt øre, og jeg var ikke gjenstridig, jeg vek ikke tilbake.
Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
6 Min rygg bød jeg frem til dem som slo, og mine kinner til dem som rykket mig i skjegget; mitt ansikt skjulte jeg ikke for hån og spytt.
Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
7 Men Herren, Israels Gud, vil hjelpe mig; derfor blir jeg ikke til skamme, derfor har jeg gjort mitt ansikt hårdt som sten, og jeg vet at jeg ikke skal bli skuffet.
Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
8 Han er nær, han som hjelper mig til min rett; hvem vil stride mot mig? La oss stå frem sammen! Hvem er min motpart? La ham komme hit til mig!
Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
9 Se, Herren, Israels Gud, vil hjelpe mig; hvem er den som vil domfelle mig? Se, de skal alle sammen eldes som et klædebon; møll skal fortære dem.
Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
10 Hvem blandt eder frykter Herren og hører på hans tjeners røst? Når han vandrer i mørke, og intet lys skinner for ham, skal han sette sin lit til Herrens navn og stole på sin Gud!
Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
11 Se, alle I som tender ild, som væbner eder med brandpiler, gå selv inn i luen av eders ild og blandt de brandpiler I har tendt! - Fra min hånd skal dette times eder; i pine skal I komme til å ligge.
Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.

< Esaias 50 >