< Hagaja 2 >

1 Septītā mēneša divdesmit pirmā dienā notika Tā Kunga vārds caur pravieti Hagaju sacīdams:
Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti:
2 Runā jel uz Zerubabeli, Šealtiēļa dēlu, Jūda valdnieku, un uz Jozua, Jocadaka dēlu, augsto priesteri, un uz tiem atlikušiem ļaudīm un saki:
“Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti,
3 Kurš ir jūsu starpā atlicis, kas šo namu redzējis viņa pirmā godībā un to tagad redz? Vai šis(nams) pret viņu nav tā kā nekas jūsu acīs?
‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu?
4 Tomēr nu, Zerubabel, esi drošs! saka Tas Kungs, un Jozua, Jocadaka dēls, augstais priesteri, esi drošs, un esiet droši, visi šīs zemes ļaudis! saka Tas Kungs, un strādājiet, jo Es esmu ar jums, saka Tas Kungs Cebaot.
Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
5 Tas vārds, caur ko Es ar jums derību cēlis, kad jūs izgājāt no Ēģiptes zemes, un Mans gars paliek jūsu vidū. Nebīstaties!
‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’
6 Jo tā saka Tas Kungs Cebaot: vēl mazs brīdis, tad Es kustināšu debesis un zemi, jūru un sausumu,
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda.
7 Un visus pagānus Es kustināšu, un tad nāks visu tautu prieks. Un Es piepildīšu šo namu ar godību, saka Tas Kungs Cebaot.
Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
8 Man pieder sudrabs un Man pieder zelts, saka Tas Kungs Cebaot.
‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Šā pēdīgā nama godība būs lielāka nekā tā pirmā, saka Tas Kungs Cebaot. Un šai vietai Es došu mieru, saka Tas Kungs Cebaot.
‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
10 Divdesmit ceturtā dienā, devītā mēnesī, Dārija otrā gadā, Tā Kunga vārds notika caur pravieti Hagaju sacīdams:
Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti:
11 Tā saka Tas Kungs Cebaot: vaicā jel priesteriem par bauslību un saki:
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena:
12 Redzi, kad kas svētu gaļu nestu savas drēbes stūrī, un ar savu stūri aizskartu maizi vai pavalgu vai vīnu vai eļļu vai kādu citu barību, vai tā būtu svētīta? Tad tie priesteri atbildēja un sacīja: Nebūtu.
Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’” Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”
13 Tad Hagaja sacīja: ja kāds, nešķīsts būdams no miroņa, visu šo aizskar, vai tas paliktu nešķīsts? Un priesteri atbildēja un sacīja: tas paliktu nešķīsts.
Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?” Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”
14 Tad Hagaja atbildēja un sacīja: tādi ir šie ļaudis, un tāda ir šī tauta Manā priekšā, saka Tas Kungs, un tāds viss viņu roku darbs, un ko tie tur upurē, tas ir nešķīsts.
Pamenepo Hagai anati, “‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.
15 Un nu ņemiet vērā savā sirdī, kas bijis no šās dienas atpakaļ un vēl senāki, pirms akmens tapa likts uz akmeni pie Tā Kunga nama,
“‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova.
16 Pirms tas notika, kad kāds gāja pie labības kopas no divdesmit pūriem, tad tur bija tikai desmit, kad viņš gāja pie vīna spaida un gribēja smelt piecdesmit mērus, tad bija tikai divdesmit.
Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha.
17 Es jūs situ ar bulu, rūsu un krusu, visu jūsu roku darbu, un jūs neatgriežaties pie manis, saka Tas Kungs.
Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova
18 Ņemiet jel vērā savā sirdi, kas būs no šās dienas un uz priekšu, no devītā mēneša divdesmit ceturtās dienas, no tās dienas, kad pamats ir likts pie Tā Kunga nama, ņemiet to vērā savā sirdī.
‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino.
19 Vai vēl ir sēkla klētī? Un vīna koks un vīģes koks un granātkoks un eļļas koks, tie nav nesuši(augļus). No šās dienas es svētīšu.
Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso. “‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’”
20 Un Tā Kunga vārds otrreiz notika uz Hagaju divdesmit ceturtā mēneša dienā sacīdams:
Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti:
21 Runā uz Zerubabeli, Jūda valdnieku, un saki: Es kustināšu debesis un zemi.
“Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi.
22 Un Es apgāzīšu ķēniņu goda krēslus un izdeldēšu stiprās pagānu valstis un apgāzīšu ratus un braucējus, un kritīs zirgi un jātnieki, cits caur cita zobenu.
Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.
23 Tai dienā, saka Tas Kungs Cebaot, Es tevi ņemšu, Zerubabel, Šealtiēļa dēls, Mans kalps, saka Tas Kungs, un tevi turēšu kā spiežamu gredzenu, jo tevi Es esmu izredzējis, saka Tas Kungs Cebaot.
“‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

< Hagaja 2 >