< Hagaja 1 >

1 Ķēniņa Dārija otrā gadā, sestā mēnesi, pirmā mēneša dienā, Tā Kunga vārds notika caur pravieti Hagaju uz Zerubabeli Šealtiēļa dēlu, Jūda valdnieku, un uz Jozua, Jocadaka dēlu, augsto priesteri, un sacīja:
Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
2 Tā runā Tas Kungs Cebaot un saka: šie ļaudis runā: laiks vēl nav nācis, uzcelt Tā Kunga namu.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
3 Un Tā Kunga vārds notika caur pravieti Hagaju sacīdams:
Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
4 Vai tad jums ir laiks, dzīvot glītos namos un šim namam būs stāvēt postā?
“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
5 Nu tad tā saka Tas Kungs Cebaot: ņemat vērā savus ceļus.
Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
6 Jūs sējat daudz un pļaujat maz, jūs ēdat, bet nepaēdat, jūs dzerat bet nepadzerat, jūs ģērbjaties, bet jums nepaliek silti, un algādzis pelna algu cauram makam.
Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
7 Tā saka Tas Kungs Cebaot: liekat vērā savus ceļus.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
8 Ejat augšā kalnos un vediet kokus un uztaisiet šo namu; pie tā Man būs labs prāts, un Es tapšu pagodināts, saka Tas Kungs.
Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
9 Jūs gan gaidāt uz daudz, bet redzi, jūs dabūjat maz, un jebšu jūs to esat mājās pārnesuši, taču Es to izputināju. Kāpēc tā? saka Tas Kungs Cebaot. Mana nama labad, kas stāv postā, kamēr ikviens skrien sava nama labad.
“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
10 Tādēļ debess jums aiztur rasu, un zeme aiztur savus augļus.
Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
11 Un sausumu Es saucu(sūtu) pār zemi un pār kalniem un pār labību un pār vīnu un pār eļļu un pār visu, kas izaug no zemes, un pār cilvēkiem un pār lopiem un pār ikvienu rokas darbu.
Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
12 Tad Zerubabels, Šealtiēļa dēls, un Jozuas, Jocadaka dēls, augstais priesteris, un visi atlikušie ļaudis klausīja Tā Kunga, sava Dieva, balsij un pravieša Hagaja vārdiem it(tieši) kā Tas Kungs, viņu Dievs, to bija sūtījis, un tie ļaudis bijās no Tā Kunga.
Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
13 Tad sacīja Hagaja, Tā Kunga vēstnesis, kam Tā Kunga vēsts bija uz tiem ļaudīm: Es esmu ar jums, saka Tas Kungs.
Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
14 Un Tas Kungs pamodināja Zerubabela, Šealtiēļa dēla, Jūdas ķēniņa garu un Jozuas, Jocadaka dēla, augstā priestera garu un visu atlikušo ļaužu garu, ka tie gāja un darīja darbu pie Tā Kunga Cebaot, sava Dieva, nama,
Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
15 Sestā mēneša divdesmit ceturtā dienā ķēniņa Dārija otrā gadā.
pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

< Hagaja 1 >