< Psalm 77 >

1 [Psalm lal Asaph] Nga wowoyak tung nu sin God, Nga tung ke pusra lulap ac El porongeyu.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
2 In pacl in ongoiya, nga pre nu sin Leum, Ke fong nufon nga sralak pouk in pre, Tusruktu nga tia ku in konauk misla.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
3 Ke nga esamak God, nga oela, Ac ke nga nunku yohk kacl, insiuk munasla.
Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
4 El oru tuh ngan ngetnget ke fong fon. Yokna mwe tukulkul in nunak luk, ac nga tia etu lah mea nga ac fahk.
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
5 Nga nunku ke len pus somla, Ac esamak yac puspis in pacl oemeet ah.
Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
6 Nga ngetnget ke fong nufon ke sripen nunak luk. Nga nunak, ac pa inge ma nga siyuk sik sifacna:
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
7 “Ya Leum El ac siskutlana? Ya El ac fah tiana sifil insewowo sesr?
“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
8 Ya El tila lungse kut? Ya El ac tiana akpwayeye wuleang lal nu sesr?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
9 Ya God El mulkunla in pakoten? Ya kasrkusrak eisla acn sin pakoten?”
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
10 Na nga fahk, “Ma se nga nunku yohk emeet uh pa inge: Lah ku lun God uh in wanginla.”
Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Nga ac fah esam na orekma yohk lom, O LEUM GOD, Nga ac fah esamak orekma sakirik lom in pacl meet ah.
Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Nga ac fah nunku ke ma nukewa kom tuh oru, Ac nga fah nunku yohk ke orekma ku lom.
Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
13 O God, ma nukewa kom oru, mutal. Wangin pac sie god oana kom.
Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Kom pa God se su orek mwenmen. Kom akkalemye ku lom inmasrlon mutunfacl uh.
Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Ke ku lom kom molela mwet lom, Fwil natul Jacob ac natul Joseph.
Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
16 Ke kof uh liye kom, O God, elos sangeng, Ac acn loal in meoa uh rarrar.
Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
17 Pukunyeng uh okoala af, Pulahl kas yen engyeng uh, Ac sarom sarmelik nu yen nukewa.
Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 Pusren pulahl lulap lom ngirla, Ac kalmen sarom sarmelik fin faclu, Ac faclu rarrar ac kusrusrsrusr.
Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Kom fahsr sasla in noa uh Ac tupalla kof loal meoa, A falkom tiana ku in liyeyuk.
Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
20 Ke kolyuk lun Moses ac Aaron, Kom kolla mwet lom oana sie shepherd.
Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

< Psalm 77 >