< Job 1 >

1 Oasr mwet se pangpang Job, su muta in acn Uz. El sie mwet su alu nu sin God, ac el arulana inse pwaye nu sel. El sie mwet na wo, ac el arulana karinganang tuh elan tia oru kutena ma koluk.
Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
2 Oasr wen itkosr ac acn tolu natul.
Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
3 Oasr pac itkosr tausin sheep, tolu tausin camel, cow tausin se, ac donkey lumfoko natul. Oayapa oasr mwet kulansap puspis lal, ac el kasrup liki mwet nukewa ke facl ma oan kutulap in acn Canaan.
ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
4 Kais sie wen itkosr natul Job inge ac muta orek kufwa, na tamulel uh kewa ac tuku nu kac, ac pacl nukewa elos ac suli pac tamtael tolu wialos in wi pac tuku nu kac.
Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
5 Ke lotu se tukun pacl in kufwa nukewa, Job el ac toangna tukakek ac orek kisa lun kais sie tulik inge in aknasnasyalosla. El oru ouinge mweyen el mu sahp sie selos tuh kaskas koluk lain God ke seasmak lal uh.
Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
6 Ke sun pacl se ma lipufan uh ac tuku nu ye mutun LEUM GOD, Satan el wi pac tuku.
Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
7 Na LEUM GOD El siyuk sel, “Kom muta ya tuku?” Na Satan el topuk ac fahk, “Nga forfor na, rarauni faclu.”
Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
8 Na LEUM GOD El fahk, “Ya kom liyal Job, mwet kulansap luk ah? Wangin sie mwet fin faclu wo ac inse pwaye nu sik oana el. El alu nu sik ac arulana taran elan tia orala kutena ma koluk.”
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
9 Na Satan el fahk, “Ya Job el alu nu sum ke wangin?
Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
10 Kom nuna karinganul wi sou lal ac ma nukewa lal. Kom akinsewowoye ma nukewa el oru, ac kom sang cow na pus natul, ekoslana acn uh.
“Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
11 Tusruktu kom fin eisla ma lal inge nukewa lukel, el ac ngetot nu sum ac selngawikomi!”
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
12 Na LEUM GOD El fahk nu sel Satan, “Kwal, ma nukewa lal Job oan inpoum, tusruktu taranna kom in tia oru kutena ma nu ke manol Job.” Ouinge Satan el som.
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
13 Sie len ah ke tulik natul Job elos tukeni ac orek kufwa in lohm sin wen se ma matu oemeet wialos ah,
Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
14 na mwet utuk kas se kasrusr tuku nu ke lohm sel Job ac fahk, “Kut tuh orekmakin ox uh in kihling acn ah, ac donkey ah muta inima se ma apkuran nu yen kut orekma we.
wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
15 Na mwet Sabea elos tuku orek lokoalok, ac pisrala nufon kosro inge. Elos uniya nufon mwet kulansap lom, ac nga mukena kaingla ngan tuh fahkot nu sum.”
tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
16 Meet liki safla ma el fahk uh, sie pac mwet kulansap ah tuku ac fahk, “Sarom ah uniya sheep ac mwet karingin ah nufon. Nga mukena kaingla ngan tuh fahkot nu sum.”
Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
17 Na meet liki safla sramsram lal ah, sie pac mwet kulansap ah tuku ac fahk, “U tolu sin mwet Chaldea elos tuku orek lokoalok nu sesr ac usla camel uh, ac uniya mwet kulansap lom nukewa sayuk. Nga mukena kaingla ngan tuh fahkot nu sum.”
Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
18 El srakna sramsram, na sie pac mwet kulansap ah tuku ac fahk, “Tulik nutum ah orek kufwa in lohm sin wen matu se nutum ah,
Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
19 na polo eng na upa se tuhme yen mwesis ah me. Eng sac ikruiya lohm sac twe onelosla nufon. Nga mukena kaingla tuku ngan tuh fahkot nu sum.”
mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
20 Na Job el tuyak ac seya nuknuk lal ah ke asor. El kalla nufon aunsifal ac putati oankiyuki nu infohk uh.
Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
21 Ac el fahk, “Nga isusla pisinpo, ac nga ac misa pisinpo. LEUM GOD El tuh ase, na pa inge El sifil eisla. Lela Inel in kaksakinyuk!”
nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
22 Ma upa inge nukewa ne sikyak nu sel Job, a el tiana tafongla ac sis nu fin God koluk uh.
Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”

< Job 1 >