< Salmi 85 >

1 Per il Capo de’ musici. Salmo de’ figliuoli di Kore. O Eterno, tu sei stato propizio alla tua terra, tu hai ricondotto Giacobbe dalla cattività.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Tu hai perdonato l’iniquità del tuo popolo, hai coperto tutti i loro peccati. (Sela)
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Tu hai acquetato tutto il tuo cruccio, ti sei distolto dall’ardore della tua ira.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Ristabiliscici, o Dio della nostra salvezza, e fa’ cessar la tua indignazione contro di noi.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Sarai tu adirato contro di noi in perpetuo? Farai tu durar l’ira tua d’età in età?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Non tornerai tu a ravvivarci, onde il tuo popolo si rallegri in te?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Mostraci la tua benignità, o Eterno, e dacci la tua salvezza.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Io ascolterò quel che dirà Iddio, l’Eterno, poiché egli parlerà di pace al suo popolo ed ai suoi fedeli; ma non ritornino più alla follia!
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Certo, la sua salvezza è vicina a quelli che lo temono, affinché la gloria abiti nel nostro paese.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 La benignità e la verità si sono incontrate, la giustizia e la pace si son baciate.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 La verità germoglia dalla terra, e la giustizia riguarda dal cielo.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Anche l’Eterno largirà ogni bene, e la nostra terra produrrà il suo frutto.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 La giustizia camminerà dinanzi a lui, e seguirà la via dei suoi passi.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Salmi 85 >