< Salmi 81 >

1 Per il Capo de’ musici. Sulla Ghittea. Salmo di Asaf. Cantate con gioia a Dio nostra forza; mandate grida di allegrezza all’Iddio di Giacobbe!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
2 Intonate un salmo e fate risonare il cembalo, l’arpa deliziosa, col saltèro.
Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
3 Sonate la tromba alla nuova luna, alla luna piena, al giorno della nostra festa.
Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
4 Poiché questo è uno statuto per Israele, una legge dell’Iddio di Giacobbe.
ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
5 Egli lo stabilì come una testimonianza in Giuseppe, quando uscì contro il paese d’Egitto. Io udii allora il linguaggio di uno che m’era ignoto:
Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
6 O Israele, io sottrassi le tue spalle ai pesi, le tue mani han lasciato le corbe.
Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
7 Nella distretta gridasti a me ed io ti liberai; ti risposi nascosto in mezzo ai tuoni, ti provai alle acque di Meriba. (Sela)
Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
8 Ascolta, o popolo mio, ed io ti darò degli ammonimenti; o Israele, volessi tu pure ascoltarmi!
“Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
9 Non vi sia nel mezzo di te alcun dio straniero, e non adorare alcun dio forestiero:
Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
10 Io sono l’Eterno, l’Iddio tuo, che ti fece risalire dal paese d’Egitto; allarga la tua bocca, ed io l’empirò.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
11 Ma il mio popolo non ha ascoltato la mia voce, e Israele non mi ha ubbidito.
“Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
12 Ond’io li abbandonai alla durezza del cuor loro, perché camminassero secondo i loro consigli.
Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
13 Oh se il mio popolo volesse ascoltarmi, se Israele volesse camminar nelle mie vie!
“Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
14 Tosto farei piegare i loro nemici, e rivolgerei la mia mano contro i loro avversari.
nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
15 Quelli che odiano l’Eterno dovrebbero sottomettersi a lui, ma la loro durata sarebbe in perpetuo.
Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
16 Io li nutrirei del fior di frumento, e li sazierei di miele stillante dalla roccia.
Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”

< Salmi 81 >