< Psalm 137 >

1 An den Strömen Babels, da saßen wir und weinten, indem wir Zions gedachten.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 An den Weiden, die dort waren, hingen wir unsere Zithern auf.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 Denn dort begehrten, die uns gefangen geführt, Lieder von uns, und unsere Peiniger Fröhlichkeit: “Singt uns eines von den Zionsliedern!”
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Wie könnten wir die Jahwe-Lieder singen auf dem Boden der Fremde!
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Wenn ich deiner vergesse, Jerusalem, so schrumpfe meine Rechte ein.
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Es klebe meine Zunge an meinem Gaumen, wenn ich deiner nicht gedenke, wenn ich nicht lasse Jerusalem meine höchste Freude sein!
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Gedenke, Jahwe, den Edomitern, den Unglückstag Jerusalems, die da riefen: “Nieder damit, nieder damit bis auf den Grund in ihr!”
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 Tochter Babel, du Verwüsterin, wohl dem, der dir vergilt, was du uns angethan!
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Wohl dem, der deine zarten Kinder packt und schmettert an den Felsen.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Psalm 137 >