< Psalm 105 >

1 Danket Jahwe, ruft seinen Namen an! Macht unter den Völkern seine Thaten kund!
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Singet ihm! Lobsingt ihm! Redet von allen seinen Wundern.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Rühmt euch seines heiligen Namens; es freue sich das Herz derer, die Jahwe suchen.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Fragt nach Jahwe und seiner Stärke, sucht beständig sein Angesicht.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Gedenkt seiner Wunder, die er gethan, seiner Zeichen und der Urteilssprüche seines Mundes,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 Nachkommen Abrahams, seine Knechte, Söhne Jakobs, seine Auserwählten!
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Er, Jahwe, ist unser Gott; über die ganze Erde ergehen seine Gerichte.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Er gedenkt ewig seines Bunds, des Wortes, das er verordnet hat, auf tausend Geschlechter,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 des Bundes, den er mit Abraham geschlossen, und seines Schwurs an Isaak.
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 Und er stellte ihn für Jakob als eine Satzung hin, als einen ewig giltigen Bund für Israel, -
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 indem er sprach: “Dir will ich das Land Kanaan verleihen als euer erbliches Besitztum!” -
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 als sie noch gering an Zahl waren, gar wenige, und als Fremdlinge darin weilten.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Und sie zogen von Volk zu Volk, von einem Königreiche zu einer anderen Nation.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Er gestattete niemandem, sie zu bedrücken, und strafte um ihretwillen Könige.
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 “Tastet meine Gesalbten nicht an und thut meinen Propheten kein Leid!”
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Als er nun eine Hungersnot ins Land rief, jegliche Stütze an Brot zerbrach,
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 da hatte er ihnen bereits einen vorausgesandt; Joseph war als Sklave verkauft.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Sie hatten seine Füße in den Block gezwängt, in Eisenfesseln war er gekommen,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 bis zu der Zeit, wo sein Wort eintraf, der Ausspruch Jahwes ihn bewährte.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Da sandte der König hin und machte ihn los, der Völkerbeherrscher, und befreite ihn.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Er machte ihn zum Herrn über sein Haus und zum Herrscher über allen seinen Besitz,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 daß er seine Fürsten nach seinem Belieben feßle und seine Vornehmen klug mache.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Und Israel kam nach Ägypten und Jakob weilte als Fremdling im Lande Hams.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Und er machte sein Volk überaus fruchtbar und machte es zahlreicher als seine Bedränger.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Er wandelte ihren Sinn, sein Volk zu hassen, an seinen Knechten Arglist zu üben.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Er sandte Mose, seinen Knecht, Aaron, den er erwählt hatte.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Er verrichtete an ihnen seine Wunder und seine Zeichen am Lande Hams.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Er sandte Finsternis und machte es finster, aber sie achteten nicht auf sein Wort.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Er verwandelte ihre Gewässer in Blut und ließ ihre Fische sterben.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Ihr Land wimmelte von Fröschen in den Gemächern ihrer Könige.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Er gebot, da kamen Hundsfliegen, Stechmücken in ihr ganzes Gebiet.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Er sandte ihnen Hagel als Regen, flammendes Feuer in ihr Land.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 Er schlug ihren Weinstock und ihren Feigenbaum und zerschmetterte die Bäume ihres Gebiets.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Er gebot, da kamen die Heuschrecken und die Fresser ohne Zahl.
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 Die fraßen alle Pflanzen in ihrem Land und fraßen die Frucht des Feldes.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Er schlug alle Erstgeborenen in ihrem Lande, die Erstlinge all' ihrer Manneskraft.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Er ließ sie ausziehen mit Silber und Gold, und es gab keinen Strauchelnden unter seinen Stämmen.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Ägypten freute sich über ihren Auszug, denn es hatte sie Schrecken vor ihnen befallen.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Er breitete Gewölk als Decke aus und Feuer, um die Nacht zu erhellen.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Sie forderten, da ließ er Wachteln kommen und sättigte sie mit Himmelsbrot.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Er öffnete den Felsen, da flossen Wasser, rannen in der Dürre als ein Strom.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Denn er gedachte an sein heiliges Wort, an Abraham, seinen Knecht,
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 und führte sein Volk in Freuden heraus, seine Auserwählten unter Jubel.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Er verlieh ihnen die Länder der Heiden, und was die Völker mit Mühe erworben, das nahmen sie in Besitz,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 damit sie seine Satzungen hielten und seine Weisungen beobachteten. Rühmet Jah!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalm 105 >