< Psalm 104 >

1 Preise, meine Seele, Jahwe! Jahwe, mein Gott, du bist überaus groß; mit Majestät und Hoheit bist du angethan,
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 der sich in Licht hüllt wie in einen Mantel, den Himmel ausspannt wie ein Zelttuch,
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 der seinen Söller im Wasser bälkt, dichte Wolken zu seinem Fahrzeuge macht, auf den Fittigen des Windes wandelt,
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 der Winde zu seinen Boten macht, zu seinen Dienern loderndes Feuer.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 Er hat die Erde auf ihre Pfeiler gegründet, daß sie in alle Ewigkeit nicht wanken kann.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 Mit der Flut wie mit einem Gewande bedecktest du sie; auf den Bergen standen Gewässer.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 Vor deinem Schelten flohen sie, vor deinem Donnerschall zogen sie sich angstvoll zurück -
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 Berge stiegen empor, es senkten sich Thäler - an die Stätte, die du ihnen gegründet.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Du hast eine Grenze gesetzt, die dürfen sie nicht überschreiten, dürfen die Erde nicht wieder bedecken.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 Der in den Thälern Quellen entsendet; zwischen den Bergen fließen sie dahin.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 Sie tränken alle Tiere des Gefildes; die Wildesel löschen ihren Durst.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 An ihnen wohnen die Vögel des Himmels, lassen aus den Zweigen heraus ihre Stimme erschallen.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 Der von seinem Söller her die Berge tränkt - von der Frucht deiner Werke sättigt sich die Erde.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 Der Gras sprossen läßt für das Vieh und Pflanzen zum Nutzen der Menschen, indem er Brotkorn aus der Erde hervorgehen läßt
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 und Wein, der des Menschen Herz erfreut, und indem er ihr Angesicht von Öl erglänzen läßt und Brot giebt, das das Herz des Menschen stärkt.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 Es sättigen sich die Bäume Jahwes, die Cedern des Libanon, die er gepflanzt hat,
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 woselbst die Vögel nisten; auf den Cypressen hat der Storch sein Haus.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 Die hohen Berge sind der Steinböcke, die Felsen der Klippdachse Zuflucht.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 Er hat den Mond zur Bestimmung von Zeiträumen geschaffen; die Sonne kennt ihren Untergang.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Wirkst du Finsternis, so wird es Nacht; in ihr regen sich alle Tiere des Waldes.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 Die jungen Löwen brüllen nach Fraß, indem sie von Gott ihre Nahrung verlangen.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 Wenn die Sonne aufgeht, ziehen sie sich zurück und lagern sich in ihrer Behausung.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Der Mensch geht aus an sein Werk und an seine Arbeit bis zum Abend.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 Wie sind deiner Werke so viel, Jahwe! Du hast sie alle in Weisheit geschaffen; die Erde ist voll von deinen Geschöpfen.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 Da ist das Meer, groß und weit nach beiden Seiten, darin ein Gewimmel ohne Zahl, kleine und große Tiere.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 Daselbst gehen Schiffe, der Leviathan, den du geschaffen hast, darin zu spielen.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 Sie alle warten auf dich, daß du ihnen zu seiner Zeit ihre Speise gebest.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 Du giebst ihnen, sie lesen auf; du thust deine Hand auf, sie sättigen sich mit Gutem.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 Du verbirgst dein Antlitz, sie werden bestürzt; du ziehst ihren Odem ein, sie verhauchen und werden wieder zu Erde.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Du entsendest deinen Odem, sie werden geschaffen, und du erneust das Angesicht der Erde.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 Die Herrlichkeit Jahwes währt ewig, Jahwe freut sich seiner Werke!
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 der die Erde anblickt, daß sie erzittert, die Berge anrührt, daß sie rauchen.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 Ich will Jahwe singen mein Leben lang, meinem Gotte lobsingen, so lange ich bin.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Möge ihm mein Dichten wohlgefallen; ich freue mich Jahwes!
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Möchten die Sünder von der Erde verschwinden, und die Gottlosen nicht mehr sein. Preise, meine Seele, Jahwe! Rühmet Jah!
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psalm 104 >