< Psalm 135 >

1 Rühmet Jah! Rühmt den Namen Jahwes, rühmt, ihr Diener Jahwes,
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 die ihr im Tempel Jahwes steht, in den Vorhöfen des Tempels unseres Gottes!
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Rühmet Jah, den Jahwe ist gütig; lobsingt seinem Namen, denn er ist lieblich!
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Denn Jah hat sich Jakob erwählt, Israel zu seinem Eigentum.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Denn ich weiß, daß Jahwe groß ist und unser Herr alle Götter überragt.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Alles, was ihm beliebte, hat Jahwe gethan, im Himmel und auf Erden, im Meer und in allen Tiefen.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Der Wolken heraufführt vom Ende der Erde her, Regen und Blitze schafft, den Wind aus seinen Schatzkammern hervorholt;
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 der die Erstgeborenen Ägyptens schlug, sowohl Menschen, als Vieh,
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Zeichen und Wunder in dich, Ägypten, entsandte, wider den Pharao und alle seine Unterthanen;
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 der viele Völker schlug und mächtige Könige tötete:
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihon, den König der Amoriter, und Og, den König von Basan, und alle Königreiche Kanaans.
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 Und er gab ihr Land zum Besitztum, zum Besitztum seinem Volk Israel.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Jahwe, dein Name währt ewig, dein Gedächtnis, Jahwe, durch alle Geschlechter.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Denn Jahwe schafft seinem Volke Recht und erbarmt sich über seine Knechte.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Die Götzen der Heiden sind Silber und Gold, ein Werk von Menschenhänden.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Sie haben einen Mund und reden nicht, sie haben Augen und sehen nicht.
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 Sie haben Ohren und hören nicht, und kein Odem ist in ihrem Munde.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Ihnen gleich werden die, die sie verfertigen, jeder, der auf sie vertraut.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Ihr vom Hause Israel, preiset Jahwe! Ihr vom Hause Aarons, preiset Jahwe!
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Ihr vom Hause Levis, preiset Jahwe! Die ihr Jahwe fürchtet, preiset Jahwe!
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Gepriesen sei Jahwe vom Zion aus, er, der zu Jerusalem wohnt! Rühmet Jah!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalm 135 >