< Psalm 126 >

1 Wallfahrtslieder. Als Jahwe das Geschick Zions wendete, waren wir wie Träumende.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni, tinali ngati amene akulota.
2 Da war unser Mund voll Lachens, und unsere Zunge voll Jubels; da sprach man unter den Heiden: “Jahwe hat Großes an diesen gethan!”
Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka; malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe. Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti, “Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”
3 Großes hatte Jahwe an uns gethan; wir waren fröhlich.
Yehova watichitira zinthu zazikulu, ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.
4 Wende, Jahwe, unser Geschick, gleich Rinnsalen im Südland.
Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova, monga mitsinje ya ku Negevi.
5 Die unter Thränen säeten, werden mit Jubel ernten.
Iwo amene amafesa akulira, adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.
6 Unter beständigem Weinen geht man dahin und trägt den Samen zur Aussaat; mit Jubel kehrt man heim und trägt seine Garben!
Iye amene amayendayenda nalira, atanyamula mbewu yokafesa, adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe, atanyamula mitolo yake.

< Psalm 126 >