< Psalm 108 >

1 Ein Lied. Ein Psalm Davids. Mein Herz ist fest, o Gott; ich will singen und spielen!
Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
2 Wache auf, meine Ehre, wache auf, Harfe und Zither; aufwecken will ich die Morgenröte!
Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
3 Ich will dich preisen unter den Völkern, Jahwe, und will dich besingen unter den Nationen!
Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
4 Denn groß über den Himmel hinaus ist deine Gnade, und bis zu den Wolken deine Treue.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
5 Erhebe dich über den Himmel, o Gott, und über die ganze Erde breite sich deine Herrlichkeit.
Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
6 Damit deine Geliebten errettet werden, so hilf nun mit deiner Rechten und erhöre mich!
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
7 Gott hat in seinem Heiligtume geredet: “Ich will frohlocken! “Ich will Sichem verteilen und das Thal Sukkoth ausmessen.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
8 “Mein ist Gilead, mein ist Manasse, und Ephraim ist die Schutzwehr meines Hauptes, Juda mein Herrscherstab.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
9 “Moab ist mein Waschbecken; auf Edom werfe ich meinen Schuh, über Philistäa jauchze ich.”
Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
10 Wer führt mich nach der festen Stadt? Wer geleitet mich nach Edom?
Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
11 Hast nicht du, o Gott, uns verworfen und ziehst nicht aus, o Gott, mit unseren Heeren?
Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
12 Schaffe uns Hilfe gegen den Feind, denn eitel ist Menschenhilfe!
Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
13 Mit Gott werden wir Heldenthaten verrichten, und er wird unsere Feinde niedertreten.
Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.

< Psalm 108 >