< Sprueche 7 >

1 Mein Sohn, behalte meine Reden und verwahre meine Gebote bei dir.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Behalte meine Gebote, so wirst du leben, und meine Weisung wie deinen Augapfel.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Binde sie an deine Finger, schreibe sie auf die Tafel deines Herzens.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Sprich zur Weisheit: Meine Schwester bist du! und nenne Einsicht “Vertraute”,
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 daß du vor dem fremden Weibe bewahrt werdest, vor der Auswärtigen, die einschmeichelnd redet.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Durch das Fenster nämlich meines Hauses, durch mein Gitter schaute ich aus.
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 Da sah ich unter den unerfahrenen, bemerkte unter den jungen Leuten einen unsinnigen Jüngling.
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 Der ging auf der Gasse, nahe einer Ecke, und schritt in der Richtung nach ihrem Hause einher.
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 In der Dämmerung am Abende des Tags, in schwarzer Nacht und Dunkelheit.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Da auf einmal tritt ihm ein Weib entgegen im Huren-Anzug und mit heimtückischem Sinne -
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 leidenschaftlich ist sie und unbändig; ihre Füße können nicht im Hause bleiben.
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Bald ist sie auf der Straße, bald auf den Plätzen und lauert neben jeder Ecke -
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 nun hat sie ihn gefaßt und geküßt; mit frecher Miene sprach sie zu ihm:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 Heilsopfer lagen mir ob; heute habe ich meine Gelübde bezahlt.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Darum bin ich herausgegangen, dir entgegen, um nach dir zu suchen, und habe dich nun gefunden.
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Mit Decken habe ich mein Bette bedeckt, mit buntgestreiften Teppichen von ägyptischem Garn.
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 Ich habe mein Lager besprengt mit Balsam, Aloë und Zimmet.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Komm, wir wollen uns in Liebe berauschen bis zum Morgen, wollen schwelgen in Liebeslust.
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Denn der Mann ist nicht daheim; er hat eine Reise in die Ferne angetreten.
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 Den Geldbeutel hat er mit sich genommen; erst am Vollmondstage kehrt er wieder heim!
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Durch ihr eifriges Zureden verführte sie ihn, riß ihn fort durch ihre glatten Lippen.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Er folgt ihr plötzlich nach wie ein Stier, der zur Schlachtbank geführt wird, und wie ein Hirsch, der ins Netz rennt,
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 bis ihm der Pfeil die Leber spaltet; wie ein Vogel zur Schlinge eilt und weiß nicht, daß es sein Leben gilt.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Nun denn, ihr Söhne, gehorcht mir und merkt auf die Reden meines Mundes.
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Laß dein Herz nicht abbiegen zu ihren Wegen, verirre dich nicht auf ihre Steige.
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 Denn viel sind der Erschlagenen, die sie gefällt hat, und zahlreich sind, die sie alle gemordet hat.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Voller Wege zur Unterwelt ist ihr Haus, die hinabführen zu des Todes Kammern. (Sheol h7585)
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)

< Sprueche 7 >