< Job 25 >

1 Bildad von Suah antwortete und sprach:
Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Sein ist die Herrschermacht und Majestät, der Frieden schafft in seinen Höhen.
“Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
3 Wer kann seine Scharen zählen, und über wem erhebt sich nicht sein Licht?
Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
4 Wie könnte da ein Mensch Recht haben gegen Gott, und rein erscheinen der vom Weib Geborene?
Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
5 Sieh, selbst der Mond, er leuchtet nicht, und die Sterne sind nicht rein in seinen Augen;
Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
6 geschweige denn der Mensch, die Made, und der Menschensohn, der Wurm!
nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”

< Job 25 >