< Job 13 >

1 Sieh', alles hat mein Auge gesehen, mein Ohr gehört und sich's gemerkt!
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Was ihr wißt, weiß ich auch; ich stehe hinter euch nicht zurück.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 Aber ich will zum Allmächtigen reden und mit Gott zu rechten habe ich Lust.
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 Denn wahrlich, ihr seid Lügenschmiede und Flicker von Nichtigem insgesamt.
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 O daß ihr doch ganz stille schwiegt, so könnte das als eure Weisheit gelten!
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 So hört denn die Rüge meines Mundes und merkt auf die Vorwürfe meiner Lippen.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Wollt ihr Gott zu Liebe Unrecht reden und ihm zu Liebe Trug reden?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Wollt ihr für ihn Partei ergreifen oder für Gott streiten?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Wird es gut ablaufen, wenn er euch erforscht, oder wollt ihr ihn narren, wie man Menschen narrt?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Nein, strafen, strafen wird er euch, wenn ihr insgeheim Partei ergreift.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Seine Hoheit wird euch betäuben, und sein Schrecken auf euch fallen.
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Eure Merksprüche sind Aschensprüche, Lehmschanzen sind eure Schanzen.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Laßt mich in Ruhe, so will ich reden, mag über mich ergehen, was da will.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Ich will mein Fleisch in meine Zähne nehmen und mein Leben aufs Spiel setzen.
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Er wird mich töten - ich harre seiner; nur will ich meinen Wandel ihm ins Angesicht darlegen.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 Schon das gereicht mir zum Sieg, daß vor sein Angesicht kein Heuchler tritt.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 So hört denn aufmerksam meine Rede, und meine Darlegung dringe zu euren Ohren.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Wohlan, ich habe den Handel eingeleitet; ich weiß, daß ich Recht behalten werde.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Wer ist's, der mit mir streiten dürfte? - denn dann wollt' ich schweigen und verscheiden!
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 Nur zweierlei thue mir nicht an, dann will ich mich vor deinem Antlitz nicht verbergen:
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Zieh deine Hand von mir zurück und laß deinen Schrecken mich nicht ängstigen;
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 dann rufe, so will ich Rede stehn, oder ich will reden, und du entgegne mir!
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Wieviel Vergehungen und Sünden habe ich denn? Meinen Frevel und meine Sünde laß mich wissen!
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Warum verhüllst du dein Antlitz und erachtest mich für deinen Feind?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Willst du ein verwehtes Blatt aufschrecken und den dürren Halm verfolgen,
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 daß du mir Bitteres als Urteil schreibst und mich die Sünden meiner Jugend erben lässest?
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 daß du meine Füße in den Block legst und alle meine Wege bewachst und dir einen Kreis um meine Sohlen ziehst?
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 Und eben dieser Mann zerfällt wie von Wurmfraß, wie ein Kleid, das die Motte zerfressen hat!
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Job 13 >